Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 6

14. Pamene mwatanganidwa ndi kuwerenga Qur’an Majiid, onetsani chidwi chanu pa Qur’an Majiid. Musatanganidwe ndi zokambirana zapadziko lapansi pakati panu mkatikati mowerenga, makamaka pamene Quraan ili yovundukura. Ngati pakufunika kuyankhula, ndiye kuti mutsirize Aayah yomwe mukuiwerengayo, mutseke Quraan mwaulemu, kenako yankhulani. Zanenedwa kuti Ibnu Umar (radhwiyallahu anhuma) akamawerenga Qur’aan Majiid, …

Read More »

Magazi Oyamba Kukhetsedwa Chifukwa cha Chisilamu

Muhammad bin Ishaaq (rahimahullah) anati: Kumayambiriro kwa Chisilamu, ma Swahaabah a Mtumiki (Swallallaahu ‘alaihi wasallam) ankaswali mobisa. Iwo ankapita kuzigwa za Makka Mukarramah kukaswali kuti Swalaah yawo ikhale yobisika kwa osakhulupirira (ndi kuti apulumuke ku mazunzo a anthu osakhulupirira). Tsiku lina Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) adali nawo pamodzi ndi gulu la …

Read More »

Chisilamu Chimaitanira Ku Chiyani?

M’nthawi ya Rasulullah swallallahu alaihi wasallam, anthu osiyanasiyana adayamba kulowa Chisilamu. Uthenga wa Chisilamu ukufalikira ndikufikira madera osiyanasiyana, Aksam bin Saifi rahimahullah mtsogoleri wa banja la Tamiim, adakhala ndi chidwi chofuna kudziwa za Chisilamu. Choncho, adatumiza anthu awiri amtundu wake kuti apite ku Madina Munawwarah kuti akafufuze za Mtumiki swallallahu …

Read More »

kuwakonda ma Answaar

Aamir (rahimahullah) mwana wa Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu), akufotokoza motere: Nthawi ina ndinati kwa bambo anga: “O, bambo anga okondedwa! Ine ndikuona kuti inu mumasonyeza chikondi chowonjezera ndi ulemu kwa ma Answaar poyerekeza ndi anthu ena.” Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) adandifunsa: “E, mwana wanga! Kodi siukusangalatsidwa ndi izi?” ndinayankha, “Ayi! Sindine okondwa. …

Read More »

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 5

13. Iwerengere Qur’an Majeed momveka bwino. Komabe, muyenera kupewa kutengera nyimbo ndi njira za oimba, ndi zina zotero. Baraa bin Aazib (Radhwiyallah anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) anati: “Kongoletsani (kuwerenga kwanu) Qur’an Majeed kudzera m’mawu anu (poiwerenga momveka bwino). Huzaifah (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) …

Read More »

Ulosi wa Rasulullah (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) okhudza Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) Kugonjetsa Qaadisiyyah

Pa mwambo wa Hajjatul Wadaa, Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) adadwala ku Makka Mukarramah ndipo ankaopa kuti amwalira. Rasulullah (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) atabwera kudzamuona, adayamba kulira. Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adamfunsa: “Bwanji ukulira?” Sa’d (Radhwiyallaahu ‘anhu) adayankha: “Ndikuopa kuti ndingamwalilire m’dziko limene ndidachita Hijrah, ndipo kudzera mu kumwalilira kuno, malipiro …

Read More »

Ulaliki Oyamba Nzinda Wa Madinah Munawwarah Pambuyo Pa Nsamuko

Pa nthawi ya nsamuko Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) atalowa mu mzinda odalitsika wa Madina Munawwarah, anthu ambiri adali kuyembekezera mwachidwi kufika kwake. Ena mwa iwo ndi omwe ankamukonda kwambiri Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) monga ma Ansaar (radhwiyallahu anhum) a ku Madina Munawwarah komanso Ayuda ndi ena opembedza mafano omwe ankakhala …

Read More »

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 4

11.Werengani Quraan Majiid mwa tajwiid ndi matchulidwe olondola. Ngakhale mutamawerenga mwachangu, muyenera kuonetsetsa kuti mukuwerenga liwu lililonse momveka bwino ndi tajweed komanso katchulidwe koyenera. وَرَتِّلِ الْقُرْآنَ تَرْتِيلًا Ndipo werengani Qur’an momveka bwino ndi mwa tarteel (mwa pang’onopang’ono). Zanenedwa kuti nthawi ina munthu wina adadza kwa Abdullah bin Mas’uud nati: “Ndimawerenga Surah …

Read More »

Kukhazikika kwa Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) pa Imaan

Abu “Uthmaan (rahimahullah) anasimba kuti Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) adati: “Ndime iyi ya Qur’aan idavumbulutsidwa ponena za ine. وَوَصَّيْنَا الْإِنسَانَ بِوَالِدَيْهِ حُسْنًا ۖ وَإِن جَاهَدَاكَ لِتُشْرِكَ بِي مَا لَيْسَ لَكَ بِهِ عِلْمٌ فَلَا تُطِعْهُمَا Ife tamulamula munthu kuchitira zabwino makolo ake. Ndipo (makolo Anu osakhulupirira) Akakukakamizani kuti Mundiphatikize (ndi chipembedzo Changa) …

Read More »

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 3

8. Umodzi mwa ma ufulu a Quraan Majiid ndi kulingalira zomwe zili mkati mwake ndi matanthauzo ake kuti uchite moyenera malamulo a Quraan Majiid. Choncho, pamodzi ndi kuwerenga Quraan Majiid, munthu ayesetsenso kuphunzira tanthauzo la ma surah osiyanasiyana a Quraan Majiid ndikofunikanso. Izi ziyenera kuchitika pansi pa Aalim oyenerera. Munthu …

Read More »