{"id":3527,"date":"2025-04-28T07:34:10","date_gmt":"2025-04-28T05:34:10","guid":{"rendered":"https:\/\/ny.alislaam.com\/?p=3527"},"modified":"2025-04-28T07:34:10","modified_gmt":"2025-04-28T05:34:10","slug":"sayyiduna-abdur-rahmaan-bin-auf-radhiyallahu-anhu-apatsidwa-udindo-osankha-khalifah","status":"publish","type":"post","link":"https:\/\/ny.alislaam.com\/?p=3527","title":{"rendered":"Sayyiduna &#8216;Abdur Rahmaan bin &#8216;Auf (Radhiyallahu &#8216;anhu) apatsidwa Udindo osankha Khalifah."},"content":{"rendered":"<p>Pambuyo pake, Sayyiduna &#8220;Umar (radhiyallahu &#8216;anhu) adapanga Shura (gulu la akuluakulu omwe azipanga ziganizo) lokhala ndi ma Swahaabah asanu ndi mmodzi otsatirawa: Ali (radhiyallahu &#8216;anhu), &#8216;Uthmaan (radhiyallahu &#8216;anhu), Zubair (radhiyah &#8216;anhu) Sa&#8217;d (Radhiyallahu &#8216;anhu) ndi Abdur Rahmaan bun &#8216;Auf (radhiyallahu &#8216;anhu).<\/p>\n<p>Pankhani ya ma Sahaabah asanu ndi mmodziwa (Radhiyallahu &#8216;anhum), Umar (Radhiyallahu &#8216;anhu) adanena kuti: &#8220;Sindikupeza kuti anthu ali oyenera kutsata Khilaafah kuposa gulu ili la maSwahaabah (Radhiyallahu &#8216;anhum) chifukwa chakuti Mtumiki (Swalla Allaahu &#8216;alayhi wa aalihi wasallam) adawasiya ali ndi moyo wosangalala padziko lapansi.&#8221;<\/p>\n<p>Pamene Umar (Radhiyallahu &#8216;anhu) adamwalira, Miqdaad bun Aswad (Radhiyallahu &#8216;anhu) adasonkhanitsa anthu a Shura m&#8217;nyumba ya Miswar bun Makhramah (radhiyallahu &#8216;anhu). Kenako adakhala mashyra kuti achite chigamulo pomwe Abu Talhah (Radhiyallahu \u2018anhu) adayimilira kuletsa anthu kulowa ndi kusokoneza Shura.<\/p>\n<p>Anthu a m\u2019Shura adagwirizana kuti atatu aiwo asiya ufulu wawo ndikuupereka kwa ena omwe ali m\u2019Shura. Mwanjira imeneyi, Zubair (radhiya Allahu &#8216;anhu) adapereka ufulu wake kwa Ali (radhiyallahu &#8216;anhu), Sa&#8217;d (radhiyallahu &#8216;anhu) adapereka ufulu wake kwa Abdur Rahmaan bin &#8216;Auf (radhiyallahu &#8216;anhu), ndipo Talhah adasankha &#8216;Ufulu wake&#8217; kw Uthman (Radhiyallahu &#8216;anhu).<\/p>\n<p>Nayenso Abdur Rahmaan bun &#8216;Auf (Radhiyallahu &#8216;anhu) adavomera kusiya ufulu wake wa khilaafah pokhapokha ataloredwa kusankha kuti ndi ndani mwa awiriwa amene asankhidwe kukhala Khalifa. &#8216;Uthmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu) ndi Ali (Radhiyallahu &#8216;anhu) adagwirizana ndi ganizo lake ndipo adalonjeza kuti atsatira ndi mtima onse chisankho chake. Kenako mamembala a Shura adabalalika.<\/p>\n<p>Kwa masiku atatu ndi mausiku atatu otsatira, Abdur Rahmaan bin \u2018Auf (Radhiyallahu \u2018anhu) adapita kwa anthu a mumzinda wa Madinah Munawwarah, kuwafunsa kuti ndi ndani amene akuona kuti ayenera kusankhidwa kukhala Khalifa.<\/p>\n<p>Abdur Rahmaan bin &#8216;Auf (Radhiyallahu &#8216;anhu) sanagone movutikira m&#8217;masiku atatu ndi mausiku amenewa. M\u2019malo mwake, ankapitiriza kuswali, du\u2019aa, istikhaarah ndi kufunsa anthu.<\/p>\n<p>Patatha masiku atatu usana ndi usiku, Abdur Rahmaan bun &#8216;Auf (radhiyallahu &#8216;anhu) anadza kwa mphwake Miswar bun Makhramah (radhiyallahu &#8216;anhu). Pofika. anampeza ali mtulo, namudzutsa iye nanena. \u201cIwe Miswar ukugona?<\/p>\n<p>Kenako Abdur Rahmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu) adamuuza kuti: &#8220;Pita ukamuitane Ali (Radhiyallahu &#8216;anhu) ndi &#8216;Uthmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu).&#8221; Hazrat Miswar (Radhiya Allahu &#8216;anhu) adafunsa kuti: &#8220;Ndiyambe ndindani kumuitana?&#8221; Abdur Rahmaan (Radhiyallahu anhu) adayankha: &#8220;Amene wamfuna.&#8221;<\/p>\n<p>Kenako Miswar (Radhiyallahu &#8216;anhu) adapita kwa Ali (radhiyallahu &#8216;anhu) ndi &#8220;Uthmaan (radhiyallahu &#8216;anhu) akuwauza kuti Hazrat Abdur Rahmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu) akuwaitana. Choncho atatuwa adanyamuka ulendo opita kwa &#8216;Abu Hurahiyah.<\/p>\n<p>Atafika kunyumba ya Miswar (Radhiyallahu &#8216;anhu), adampeza Abdur Rahmaan bin &#8216;Auf (radhiyallahu &#8216;anhu) ali chiyimire kuswali. Atamaliza Swalah yake adatembenukira kwa \u2018Ali (Radhiya Allaahu \u2018anhu) ndi \u2018Uthmaan (Radhiyallahu \u2018anhu) nati: \u201cNdidawafunsa anthu za inu nonse awiri, ndipo sindinapezepo wina aliyense kukhaka opambana pa udindo kuposa awirinu.\u201d Abdur Rahman Radhiyallah anhu adapanga Hazrat Ali (Radhiyallahu &#8216;anhu) ndi Hazrat &#8216;Uthmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu) alonjeza kuti mwa awiriwa, yemwe angamusankhe kukhala Khalifa ndithu adzalamulira mwachilungamo, ndipo amene sasankhidwa adzakondwera ndi chigamulo chomwe chingapangidwe ndikuvomera munthu wina kukhala Khalifa.<\/p>\n<p>Hazrat Abdur Rahmaan (Radhiya Allaahu &#8216;anhu) pambuyo pake adavala nduwira yomwe Mtumiki (Swalla Allaahu &#8216;alayhi wa aalihi wasallam) adamumanga mutu mwake, adakolekera lupanga lake ndikupita ndi Hazrat Ali (radhiyallahu &#8216;anhu) ndi Hazrat &#8216;Uthmaan (radhiyallahu &#8216;anhu) kupita ku musjid. Hazrat Abdur Rahmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu) adatumiza uthenga owayitanira anthu ku Musjid. Choncho, anthu anayamba kusonkhana musjid, kupanga mizere, mpaka musjid idadzadza ndi anthu.<\/p>\n<p>Hazrat &#8216;Uthmaan (Radhiya Allaahu &#8216;anhu) sadathe kupeza malo aliwonse oti akhale choncho chifukwa cha kuchuluka kwake kwa hayaa (kudzichepetsa kwake), adakhala kumbuyo kwa anthu onse mu musjid.<\/p>\n<p>Kenako Hazrat Abdur Rahmaan (Radhiya Allaahu &#8216;anhu) adakwera pa mimbar ya Mtumiki (Swalla Allaahu &#8216;alayhi wa aalihi wa sallam) naima pa malo omwe Mtumiki (Swalla Allaahu &#8216;alayhi wa aalihi wa sallam) ankakhalapo. Adayima pamenepo kwa nthawi yayitali ndikupanga mokweza mawu. Kenako adayankhula kwa anthu kuti: &#8220;E inu anthu! Ine ndakufunsani (za Hazrat Ali (Radhiyallahu &#8216;anhu) ndi Hazrat &#8216;Uthmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu)) mwamseri ndi pagulu, awiriawiri ndi payekhapayekha, ndipo ndapeza kuti simunafanane aliyense mwa inu ndi ma Swahaaba awiriwa.&#8221;<\/p>\n<p>Kenako Hazrat Abdur Rahmaan (Radhiya Allaahu &#8216;anhu) adagwira dzanja la Hazrat &#8220;Uthmaan (Radhiyallahu &#8216;arihu) namulengeza kuti ndiye akhale Khalifah, kenako adamukhanzika Hazrat &#8220;Uthmaan (Radhiyallahu anhu) pa sitepe ya mimbari yomwe ili pansi pake kuti anthu abwere kwa iye ndi kugwirana naye dzanja kulonjeza kuti adzamumvera. Kuchokera mwa anthu onse, Hazrat Ali (Radhiyallahu &#8216;anhu) ndi amene adayamba kubwera ndikulonjeza kuti adzakhala okhulupirika kwa Hazrat &#8216;Uthmaan (Radhiyallahu &#8216;anhu). <em>(Al-Bidaayah-wan-Nihaayah vol 7 tsamba 297-298)<\/em><\/p>\n","protected":false},"excerpt":{"rendered":"<p>Pambuyo pake, Sayyiduna &#8220;Umar (radhiyallahu &#8216;anhu) adapanga Shura (gulu la akuluakulu omwe azipanga ziganizo) lokhala ndi ma Swahaabah asanu ndi mmodzi otsatirawa: Ali (radhiyallahu &#8216;anhu), &#8216;Uthmaan (radhiyallahu &#8216;anhu), Zubair (radhiyah &#8216;anhu) Sa&#8217;d (Radhiyallahu &#8216;anhu) ndi Abdur Rahmaan bun &#8216;Auf (radhiyallahu &#8216;anhu). Pankhani ya ma Sahaabah asanu ndi mmodziwa (Radhiyallahu &#8216;anhum), Umar (Radhiyallahu &#8216;anhu) adanena kuti: &hellip;<\/p>\n","protected":false},"author":3,"featured_media":0,"comment_status":"closed","ping_status":"open","sticky":false,"template":"","format":"standard","meta":{"footnotes":""},"categories":[22],"tags":[],"class_list":["post-3527","post","type-post","status-publish","format-standard","","category-sahaabah"],"_links":{"self":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts\/3527","targetHints":{"allow":["GET"]}}],"collection":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts"}],"about":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/types\/post"}],"author":[{"embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/users\/3"}],"replies":[{"embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Fcomments&post=3527"}],"version-history":[{"count":1,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts\/3527\/revisions"}],"predecessor-version":[{"id":3528,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts\/3527\/revisions\/3528"}],"wp:attachment":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Fmedia&parent=3527"}],"wp:term":[{"taxonomy":"category","embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Fcategories&post=3527"},{"taxonomy":"post_tag","embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Ftags&post=3527"}],"curies":[{"name":"wp","href":"https:\/\/api.w.org\/{rel}","templated":true}]}}