{"id":3745,"date":"2025-09-28T06:53:46","date_gmt":"2025-09-28T04:53:46","guid":{"rendered":"https:\/\/ny.alislaam.com\/?p=3745"},"modified":"2026-02-15T05:40:09","modified_gmt":"2026-02-15T03:40:09","slug":"tafseer-ya-surah-naaziaat","status":"publish","type":"post","link":"https:\/\/ny.alislaam.com\/?p=3745","title":{"rendered":"Tafseer Ya Surah Naazi\u2019aat"},"content":{"rendered":"<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-1\" class=\"aya selected\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0627\u0632\u0650\u0639\u064e\u0627\u062a\u0650 \u063a\u064e\u0631\u0652\u0642\u064b\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-2\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0627\u0634\u0650\u0637\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0646\u064e\u0634\u0652\u0637\u064b\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-3\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0627\u0628\u0650\u062d\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0633\u064e\u0628\u0652\u062d\u064b\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-4\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0627\u0628\u0650\u0642\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0633\u064e\u0628\u0652\u0642\u064b\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0664\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-5\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0627\u0644\u0652\u0645\u064f\u062f\u064e\u0628\u0651\u0650\u0631\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0623\u064e\u0645\u0652\u0631\u064b\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0665\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndikulumbirira (angelo) amene amachotsa (mizimu ya osakhulupirira) mwaukali, ndi (angelo) amene amachotsa (miyoyo ya okhulupirira) moleza, ndi (Angelo) amene amasambira nayo mizimuyo (m\u2019mlengalenga), ndi (Angelo) amene amapikisana (kukwaniritsa malamulo a Allah Ta\u2019ala).<\/em><\/p>\n<p>Monga ziliri kuti Sura Nabai idavumbulutsidwa kuti idzakhazikitse chikhulupiriro cha tsiku la Qiyaamah, momwemonso surayi idavumbulutsidwa kuti idzakambe nkhani zina za Qiyaamah.<\/p>\n<p>M\u2019surayi Allah Ta\u2019ala wayamba ndi kulumbilira machitidwe ena a angero ndi cholinga chofuna kutsimikizira anthu kuti tsiku la Qiyaamah ndi lotsimikizika. Choncho, m\u2019ndime yachisanu ndi chimodzi, atalumbirira machitidwe osiyanasiyana a angero, Allah Ta\u2019ala akuyankhula za tsiku la Qiyaamah.<\/p>\n<p>Popeza ndi zachidziwikire kuti Allah Ta\u2019ala walumbirira angero amene amachotsa miyoyo ya anthu ndi kumudziwitsa munthu kuti Qiyaamah ya munthu aliyense imayamba iye akamwalira. Choncho, kwanenedwa momveka bwino kuti: \u201cAmene wamwalira, Qiyaamah yake yayamba.<\/p>\n<p>Ngakhale Qiyaamah yeniyeni ya zolengedwa zonse idzachitikale kumapeto kwa dziko lapansi, komabe popeza moyo otsatira wa munthu umayambika pa akamwalira, imfa ya munthu aliyense imatengedwa ngati Qiyaamah yake.<\/p>\n<p>Tikaonetsetsa, m\u2019ma aya awa Allah Ta\u2019ala akukamba machitidwe asanu a angero. Makhalidwe asanuwa ndi awa:<\/p>\n<p><strong>Khalidwe loyamba<\/strong><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-1\" class=\"aya selected\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0627\u0632\u0650\u0639\u064e\u0627\u062a\u0650 \u063a\u064e\u0631\u0652\u0642\u064b\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndikulumbirira (angelo) amene amatulutsa (mizimu ya osakhulupirira) mwampamvu<\/em><\/p>\n<p>M\u2019ndime iyi, Allah Ta\u2019la akufotokoza za angero a imfa amene amachotsa mizimu ya makafiri mwaukali ndi mwankhanza, osawachitira chifundo. Angero amene amachotsa mizimu ya makafiri ndi angero achilango, ndipo mawu oti \u201cmwankhanza\u201d mu Aayah akutanthauza kuwawa kwauzimu osati kuwawa kwakuthupi. Chifukwa chake, anthu omwe ali pafupi ndi munthu wakufayo sangazindikire ululu wa munthu wakufayo monga momwe ululu umamvekera ndi moyo wa munthu wakufayo, osati thupi lake.<\/p>\n<p>Nthawi zina zimaoneka ngati kuti mzimu wa kaafir umachoka m\u2019thupi lake mosavuta, koma zoona zake n\u2019zakuti sizili choncho, monga momwe zilili m\u2019ndime iyi Allah Ta\u2019ala akutiuza za ululu waukulu ndi masautso amene mzimu wa kafiri umakumana nawo yomwalira.<\/p>\n<p><strong>Ubwino Wachiwiri wa Angelo<\/strong><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-2\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0627\u0634\u0650\u0637\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0646\u064e\u0634\u0652\u0637\u064b\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndikulumbilira (angelo) amene amatulutsa (mizimu ya okhulupirira) Modekha<\/em><\/p>\n<p>M\u2019ndime iyi, Allah Ta\u2019la akufotokoza za angero amene amatulutsa mizimu ya okhulupirira modekha ndi moleza. Angelo amene amachotsa mizimu ya okhulupirira amatchedwa angelo achifundo. Iwo amalamulidwa ndi Allah Ta\u2019ala kuti achite ndi Asilamu mwaubwino ndi wodekha.<\/p>\n<p>Liwu loti <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u201c\u0627\u0644\u0646\u0670\u0634\u0637\u0670\u062a\u201d<\/span> likuchokera ku liwu loti <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u201c\u0646\u0634\u0637\u201d<\/span> lomwe kwenikweni limatanthauza \u201ckumasula mfundo\u201d. Izi zikutanthawuza &#8220;kumasula mfundo ya chinthu chomwe chili ndi madzi kapena mpweya, kuti madzi kapena mpweya utuluke mosavuta&#8221;. Ili ndi fanizo lotulutsa mizimu ya okhulupirira mofatsa, mosiyana ndi mizimu ya osakhulupirira yomwe imatulutsidwa mwankhanza. Zili ngati kuti mzimu wa okhulupirira unali omangidwa m\u2019thupi lake, ndipo thupi linafunika kutsegulidwa kuti mzimuwo utulutsidwe.<\/p>\n<p>Pankhani imeneyinso, liwu lakuti <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u0646\u064e\u0634\u06e1\u0637\u064b\u0627<\/span> lomwe limamasulira kuti \u201cmosalala\u201d kapena \u201cmodekha\u201d limatanthauza kufewa kwauzimu kapena kufatsa, osati ku zochitika zakuthupi. Ntha\u0175i zina, okhulupirira opembedza amaonedwa akukumana ndi vuto linalake pantha\u0175i ya imfa yake, komabe, zimenezi sizingatanthauze kwenikweni kuti akukumana ndi vuto linalake lauzimu kapena chilango, ngakhale kuti kuthupi, zingamaoneke choncho kwa awo amene ali nawo pafupi.<\/p>\n<p>Ukatulutsidwa mzimu wa kafiri, chithunzi chonse cha chilango cha barzakh (moyo wa pambuyo pa imfa) chimadza pamaso pake. Imakahala nthawi yochititsa mantha ndi kuopsya kwambiri, ndipo munthu amene wamwalirayo amathedwa nzeru ndi zimenezo. Popeza mzimu, ukuchita mantha kwambiri ndi zochitika zachilango, umayamba kusuntha thupi lonse, kuyesa kubisala kapena kuthawa chilango. Komabe, angero a imfa amauchotsa mzimu wake mwamphamvu, kuutulutsa mwamphamvu ndi mwaukali m\u2019thupi lake, monga momwe mzinga umazulidwira mwamphamvu muubweya onyowa (monga momwe tafotokozera mu Hadith ya olemekezeka Baraa bin Aazib (radhiyallahu \u2018anhu) yolembedwa mu Musnad-e-Ahmed).<\/p>\n<p>Komano, mzimu wa Msilamu ukachotsedwa, malipiro aakulu ndi madalitso a tsiku Lomaliza amene wamusungira amaperekedwa kwa iye ndipo amapatsidwa nkhani yabwino ndi yosangalatsa, choncho mzimu wake umachoka m\u2019thupi momasuka ndi chisangalalo chachikulu.<\/p>\n<p>&nbsp;<\/p>\n<p><strong>Khalidwe Lachitatu la Angelo<\/strong><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0627\u0628\u0650\u062d\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0633\u064e\u0628\u0652\u062d\u064b\u0627\u00a0\u200e\ufd3f\u0663\ufd3e<\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndi amene amasambira (nayo mizimuyo) mu mlengalenga (popita nayo ku malo ake oyembekezera.<\/em><\/p>\n<p>Mu ayah iyi, Allah Ta\u2018ala akulankhula za khalidwe lachitatu la angelo. Angelo omwe akutchulidwa mu ndime iyi ndi angelo a imfa omwe, atatulutsa mzimu wa munthu, amayendayenda mofulumira mu mlengalenga atanyamula mzimu kupita kumwamba kuti akaupereke kwa Allah Ta\u2018ala.<\/p>\n<p>Mawu akuti \u201c\u0633\u0670\u0628\u062d\u0670\u062a\u201d amachokera ku mawu akuti \u201c\u0633\u0628\u062d\u201d omwe amatanthauza \u201ckusambira\u201d kapena \u201ckuyandama\u201d, koma m&#8217;nkhaniyi, ponena za angelo, tanthauzo la mawuwa ndi \u201ckuyenda mofulumira m&#8217;mwamba\u201d.<\/p>\n<p><strong>Nkhalidwe Lachinayi La Angelo<\/strong><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u0641\u064e\u0627\u0644\u0633\u0651\u0670\u0628\u0650\u0642\u0670\u062a\u0650 \u0633\u064e\u0628\u06e1\u0642\u064b\u0627 \u06d9\ufd3f\u06f4\ufd3e<\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndipo ndi (angelo) omwe amathamanga limodzi pa mpikisano (kuti akwaniritse lamulo la Allah Ta\u2018ala)<\/em><\/p>\n<p>Mu ayah iyi, Allah Ta\u2018ala akulankhula za momwe angelo a imfa amathamangitsirana kupikisana wina ndi mnzake kuti akwaniritse lamulo la Allah Ta\u2018ala.<\/p>\n<p>Malinga ndi lamulo la Allah Ta\u2018ala, angelo amatenga miyoyo ya opembedza kupita nayo kumalo awo abwino, ndi mizimu ya oipa kupita nayo kumalo awo oipa. Pambuyo pofunsidwa m&#8217;manda, mzimu wa okhulupirira umasamutsidwira ku malo a Illiyyeen komwe udzasangalala ndi madalitso a Paradaiso, ndipo mzimu wa osakhulupirira umasamutsidwira ku Sijjeen komwe umakazunzika ku Gehena. (Al-Rooh tsamba 134)<\/p>\n<p><strong>Khalidwe Lachisanu La Angelo<\/strong><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u0641\u064e\u0627\u0644\u06e1\u0645\u064f\u062f\u064e\u0628\u0650\u0651\u0631\u0670\u062a\u0650 \u0627\u064e\u0645\u06e1\u0631\u064b\u0627 \u06d8\ufd3f\u06f5\ufd3e<\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndi iwo (angelo) omwe amayendetsa malamulo (omwe amapatsidwa ndi Allah Ta\u2018ala pankhani okhudza mizimu ya akufa)<\/em><\/p>\n<p>Mu ayah iyi, Allah Ta\u2018ala akunena za angelo omwe amayendetsa nkhani za omwe amwalira ndikukwaniritsa zomwe Allah Ta\u2018ala walamula popereka mphotho kwa mizimu yolungama ndikulanga mizimu yoipa.<\/p>\n<p>Mwanjira ina, ntchito yomaliza ya angelo awa a imfa idzakhala kutonthoza mizimu yolungama ndikubweretsa ululu kwa mizimu yoipa. Mizimu ikafika pamalo awo abwino kapena oipa, angelo omwe alamulidwa kupereka mphotho ndi kutonthoza mizimu yabwino amasonkhanitsa njira zowalipirira ndi kuwatonthoza, ndipo angelo omwe alamulidwa kulanga ndi kupereka mavuto ku mizimu yoipa amakonza njira zowazunzira ndi kuwalanga.<\/p>\n<p><strong>Mphotho ndi Chilango Za M&#8217;manda<\/strong><\/p>\n<p>Pakadali pano Surah ikutsimikizira kuti nthawi ya imfa, angelo adzafika ndikutulutsa mzimu wa munthu. Kenako adzautenga kupita kumwamba ndikuunyamula mwachangu kupita nawo malo ake oyenera. Mzimu wabwino udzasamutsidwa kupita nawo kumalo a ntendere, ndipo mzimu oipa udzasamutsidwa kupita nawo kumalo a mavuto. Kumeneko angelo adzakonza njira zopezera mphotho ndi chitonthozo, kapena chilango ndi ululu kwa mitundu iwiri ya mizimu motsatana.<\/p>\n<p>Mavesiwa akusonyeza kuti mphotho ndi chilango zidzachitika m&#8217;manda (ngati m&#8217;moyo wa barzakh munthu atachoka padziko lapansi). Pambuyo pake, Tsiku la Qiyaamah likadzafika, chigamulo chidzaperekedwa kuti munthu akalowe ku Jannah, kapena ku Gahena.<\/p>\n<p>Kukamba za momwe mzimu wa munthu olungama kapena ochimwa umachotsedwera ndi angelo a imfa, pali Hadith yayitali ya Olemekezeka Baraa bin Aazib (radhwiyallahu \u2018anhu) yomwe yalembedwa mu Musnad-e-Ahmad. Hadith iyi ndi iyi. Baraa bin Aazib (radhwiyallahu \u2018anhu) akunena kuti:<\/p>\n<p>Nthawi ina, tinatuluka ndi Rasulullah (Swallallahu \u2018alaihi wasallam) kuti tikaswalire nawo maliro a munthu wachi Ansaar. Titafika kumanda, tinapeza kuti manda anali asanakumbidwe. Rasulullah (swallallahu \u2018alaihi wasallam) anakhala pansi, ndipo tinakhala momuzungulira, modekha ngati kuti panali mbalame pamitu pathu.<\/p>\n<p>Rasulullah (swallallahu \u2018alaihi wasallam) anali ndi ndodo m&#8217;manja mwake yomwe ankakanda nayo pansi (popeza ankaganiza kwambiri). Rasulullah (swallallahu \u2018alaihi wasallam) kenako ananyamura mutu wake nati kawiri ngati si katatu, \u201cPemphani chitetezo cha Allah Ta\u2018ala ku chilango cha manda!\u201d<\/p>\n<p>Pambuyo pake, Rasulullah (swallallahu \u2018alaihi wasallam) anati, \u201cNdithudi, okhulupirira akatsala pang\u2019ono kuchoka padziko lapansi kupita ku Moyo omaliza, angelo amatsika kwa iye kuchokera kumwamba. Nkhope zawo zoyera zimawala kwambiri kotero kuti zimakhala ngati kuti nkhope zawo zonse ndi dzuwa. Amabwera ndi sanda yochokera ku siliki ya ku Jannah, komanso mafuta onunkhira ochokera ku mafuta onunkhira a ku Jannah. Amakhala pafupi naye, komwe angayang&#8217;ane.<\/p>\n<p>\u201cPambuyo pake, mngelo wa imfa amabwera kwa iye ndikukhala pambali pake. Mngeloyu amamulankhula nati, \u2018Iwe mzimu oyera! Tuluka, kupita ku chikhululuko cha Allah ndi chimwemwe Chake!\u2019 Mzimuwo umatuluka moyenda bwino, monga momwe dontho la madzi limatulukira m\u2019chikopa cha madzi.<\/p>\n<p>&#8220;Angelo amapitirira kukwera nawo mzimu kupita kumwamba. Angelo alionse omwe angakumane nawo amawapempha chilorezo choti adutse. khomo la ntambo umenewo limatsegulidwa kuti adutse, kenako angelo a ntambo otsatira amalandira mzimu ndikuuperekeza ku ntambo otsatira, ndipo izi zimapitirira kwina konseko, mpaka mzimuwo utafika ku ntambo omalizira.<\/p>\n<p>&#8220;Kenako Allah Ta&#8217;ala amalamula angelo kuti, &#8216;Lembani m&#8217;buku la kapolo wanga kuti malo ake okhalamo akhazikitsidwa kukhala ku Illiyiin, kenako mumubwezeretse padziko lapansi (kumanda ake kuti akafunsidwe), popeza ndidawalenga kuchokera ku dothi ndipo ndidzawabwezeretsa ku dothi, ndi kudzawaukitsanso kuchokera ku dothi.&#8217;<\/p>\n<p>&#8220;Kenako mzimu umabwezeretsedwa ku thupi m&#8217;manda ndipo angelo awiri (Munkar ndi Nakiir) amamubwelera. Amamukhanzika ndikumufunsa kuti, &#8216;Kodi Mbuye wako ndindani?&#8217; Amayankha kuti, &#8216;Mbuye wanga ndi Allah.&#8217; Pambuyo pake amamufunsa kuti, &#8216;Kodi chipembedzo chako ndi chiyani?&#8217; Amayankha kuti, &#8216;Chipembedzo changa ndi Chisilamu.&#8217; Pomaliza, amamufunsa kuti, &#8216;Kodi munthu uyu amene adatumizidwa kwa inu ndi ndani?&#8217; Amayankha kuti, &#8216;Ndi Mtumiki wa Allah (Swallallahu &#8216;alaihi wasallam).&#8217; Angelo amamufunsa kuti, &#8216;Wadziwa bwanji zimenezi?&#8217; Iye amayankha kuti ndidawerenga bukhu la Allah ndipo ndidakhulupilira mwa iye ndi kumukhulupilira kuti iye ndi Mtumiki weniweni wa Allah Ta&#8217;ala.&#8217;<\/p>\n<p>&#8220;Kenako kumamveka kufuula kuchokera kumwamba kuti, &#8216;Ndithudi, kapolo wanga wanena zoona (ndipo wayankha mafunso molondola), choncho mutambasulireni kapeti m&#8217;makapeti a ku Jannah, mumuveke zovala za ku Jannah, ndipo mumutsegulire (kutambasura manda ake) khomo la ku Jannah!&#8217; Kotero, mpweya ndi fungo la ku Jannah zimamufikira, ndipo manda ake amatambasuridwa mpaka kothera kuona maso ake.<\/p>\n<p>&#8220;Kenako munthu amabwera kwa iye ndi nkhope yokongola, zovala zokongola komanso fungo lokoma. Munthuyo amamuuza kuti, &#8216;Sangalala ndi zomwe zingakusangalatse! Tsiku ili ndi limene udalonjezedwa (kukumana nalo pamene unali padziko lapansi)!&#8217; Omwalirayo amamufunsa kuti, &#8216;Ndiwe ndani? Nkhope yako ndi ya munthu amene amabweretsa zabwino!&#8217; Munthuyo amayankha kuti, &#8216;Ndine ntchito zako zabwino zomwe unkachita.&#8217;<\/p>\n<p>&#8220;Omwalirayo amati, &#8216;E, Mbuye wanga! Yambani Qiyaamah! E, Mbuye wanga! Yambani Qiyaamah, kuti ndibwerere ku banja langa ndi chuma changa (ku Jannah)!'&#8221;<\/p>\n<p>Kenako Rasulullah (swallallahu \u2018alaihi wasallam) adati, \u201cNdithudi, munthu osakhulupirira akatsala pang\u2019ono kuchoka padziko lapansi ndikupita ku Moyo osatha, angelo amabwera kwa iye kuchokera kumwamba. Angelo awa ali ndi nkhope zakuda, ndipo amakhala ndi matumba a nsalu zopyapyala. Amakhala pafupi naye, mbali imene iyeyo angathe kumawaona.<\/p>\n<p>\u201cPambuyo pake, mngelo wa imfa amabwera kwa iye ndikukhala pambali pake. Mngeloyu amamulankhula nati, \u2018Iwe mzimu onyansa, oipa! Tuluka mwa mkwiyo wa Allah!\u2019 Mzimuwo umayendayenda m\u2019thupi lake (kuyesera kumuthawa mngelo wa imfa kuti asaugwire). Pambuyo pake, mngelo wa imfayu amatulutsa mzimuwo mwamphamvu, monga momwe chikopa chimachotsedwera mwamphamvu kuthipi lake. Mngelo wa imfa amaugwira mzimuwo.<\/p>\n<p>\u201cMngelo wa imfa akagwira mzimu, angelo ena omwe ali naye samausiya m\u2019manja mwake ngakhale pang\u2019ono mpaka atautenga n\u2019kuuika m\u2019thumba lopanda kanthu. Fungo loipa limatuluka mu mzimu umenewu, ngati fungo loipa kwambiri la mtembo lomwe lingapezeke padziko lapansi.<\/p>\n<p>\u201cKenako angelo amakwera nawo kumwamba, ndipo gulu lililonse la angelo omwe amadutsana nawo, angelo amenewo amawafunsa kuti, \u2018Kodi mzimu oipawu ndi wa ndani?\u2019 Amayankha, \u2018Ndi wakutiwakuti, mwana wa wakutiwakuti,\u2019 akumutchura ndi mayina oipa kwambiri omwe anthu ankamuitanira padziko lapansi.<\/p>\n<p>\u201cKenako angelo amapitiriza kukwera nawo mzimuwo mpaka kukafika kuntambo oyamba. Akafika kjntambo oyamba, amapempha chilolezo cholowa, koma khomo la kumwamba silimatsegulidwa kwa iwo.\u201d<\/p>\n<p>Atatchula izi, Rasulullah (sallallahu \u2018alaihi wasallam) adawerenga Ayah yotsatira ya Qur\u2019aan Majiid:<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u0644\u064e\u0627 \u062a\u064f\u0641\u064e\u062a\u064e\u0651\u062d\u064f \u0644\u064e\u06c1\u064f\u0645\u06e1\u00a0 \u0627\u064e\u0628\u06e1\u0648\u064e\u0627\u0628\u064f \u0627\u0644\u0633\u064e\u0651\u0645\u064e\u0622\u0621\u0650\u00a0 \u0648\u064e\u0644\u064e\u0627 \u06cc\u064e\u062f\u06e1\u062e\u064f\u0644\u064f\u0648\u06e1\u0646\u064e \u0627\u0644\u06e1\u062c\u064e\u0646\u064e\u0651\u06c3\u064e \u062d\u064e\u062a\u0651\u0670\u06cc \u06cc\u064e\u0644\u0650\u062c\u064e \u0627\u0644\u062c\u064e\u0645\u064e\u0644\u064f \u0641\u0650\u064a\u0652 \u0633\u064e\u0645\u0650\u0651 \u0627\u0644\u06e1\u062e\u0650\u06cc\u064e\u0627\u0637\u0650<\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>makomo akumwamba sadzatsekulidwa kwa iwo (osakhulupirira), ndipo sakalowa ku Paradiso mpaka ngamira italowa pa diso la singano (i.e. Sadzatha kukalowa ku Jannah). (Surah A\u2019raaf v. 40)<\/em><\/p>\n<p>Kenako Rasulullah (swallallahu \u2018alaihi wasallam) anapitiriza nati, \u201cAllah Ta\u2018ala adzanena, \u2018Lembani m\u2019buku lake kuti malo ake okhalamo alamulidwa kukhala ku Sijjiin, pansi pa nthaka (Jahannum).\u2019 Pambuyo pake, mzimu wake umaponyedwa mwamphamvu.\u201d<\/p>\n<p>Kenako Rasulullah (Swalla Allaahu \u2018alayhi wa aalihi wa sallam) adawerenga ndime iyi ya Qur-aan:<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u0648\u064e \u0645\u064e\u0646\u06e1 \u06cc\u064f\u0651\u0634\u06e1\u0631\u0650\u06a9\u06e1 \u0628\u0650\u0627\u0644\u0644\u0647\u0650 \u0641\u064e\u06a9\u064e\u0627\u064e\u0646\u064e\u0651\u0645\u064e\u0627 \u062e\u064e\u0631\u064e\u0651\u00a0 \u0645\u0650\u0646\u064e \u0627\u0644\u0633\u064e\u0651\u0645\u064e\u0622\u0621\u0650 \u0641\u064e\u062a\u064e\u062e\u06e1\u0637\u064e\u0641\u064f\u06c1\u064f \u0627\u0644\u0637\u064e\u0651\u06cc\u06e1\u0631\u064f\u00a0 \u0627\u064e\u0648\u06e1 \u062a\u064e\u0647\u0652\u0648\u0650\u064a\u0652 \u0627\u0644\u0631\u0650\u0651\u06cc\u06e1\u062d\u064f \u0641\u0650\u06cc\u06e1 \u0645\u064e\u06a9\u064e\u0627\u0646\u064d\u00a0 \u0633\u064e\u062d\u0650\u06cc\u06e1\u0642\u064d \ufd3f\u06f3\u06f1\ufd3e<\/p>\n<p>Amene amamphatikiza Allah ndi milungu ina, ali ngati wagwa kuchokera kumwamba, ndipo Mbalame zikumuwakha, kapena mphepo kumponya Kumalo akutali. (Surah Haj v. 31)<\/p>\n<p>Mtumiki (sallallahu \u2018alaihi wasallam) anapitiriza nati, \u201cKenako mzimu wake udzabwerera m\u2019thupi lake, ndipo angelo awiri (Munkar ndi Nakeer) adzabwera kwa iye. Adzamukhanzika pansi namufunsa kuti, \u2018Kodi Mbuye wako ndani?\u2019 Iye adzayankha kuti, \u2018Aah! Aah! Sindikudziwa!\u2019 Kenako adzamufunsa kuti, \u2018Kodi chipembedzo chako n\u2019chiyani?\u2019 Iye adzati, \u2018Aah! Aah! Sindikudziwa!\u2019 Pomaliza, angelo adzamufunsa kuti, \u2018Kodi munthu ameneyu anatumizidwa kwa iwe ndi ndani?\u2019 Adzayankhanso kuti, \u2018Aah! Aah! Sindikudziwa!\u2019<\/p>\n<p>\u201cPamenepa, mawu adzafuula kuchokera kumwamba nati, \u2018Walephera, choncho mutambasulireni kapeti ya moto, ndipo mutsegulireni chitseko cha moto wa Jahannam.\u2019 Kotero, kutentha kwaukali kwa moto wa Jahannum kudzamufikira, ndipo manda ake adzachepetsedwa ndi kuthina, mpaka (adzakhala akufinyidwa mpaka kufika pamlingo wakuti) nthiti zake kuchokera mbali imodzi zidzalumikizana ndi nthiti za mbali inayo.<\/p>\n<p>\u201cMunthu adzabwera kwa iye amene maonekedwe ake adzakhala owopsa, amene zovala zake zidzakhala zoopsa ndipo fungo lake lidzakhala loipa kwambiri. Munthuyo adzamuuza kuti, \u2018Sangalala ndi zomwe zidzakupangitse kudzimvera chisoni! Tsiku ili ndi limene unalonjezedwa (kukumana nalo pamene udali padziko lapansi)!\u2019 Omwalirayo adzamufunsa munthuyo kuti, \u2018Ndiwe ndani, chifukwa nkhope yako ndi ya munthu amene amabweretsa zoipa?\u2019 Iye adzayankha kuti, \u2018Ndine ntchito zako zoipa.\u2019<\/p>\n<p>\u201cOmwalirayo adzati, \u2018E, Ambuye wanga! Musalore Qiyaamah ibwere!\u2019\u201d<\/p>\n<p>M&#8217;nkhani ina, zafotokozedwa kuti mzimu wa okhulupirira odzipereka ukakwera kupita kumwamba, ndiye kuti mngelo aliyense pakati pa mitambo ndi dziko lapansi, ndi mngelo aliyense kumtambo ulionse, amamuchitira dua. Zitseko zakumwamba zimatsegulidwa kwa iye, ndipo angelo pakhomo lililonse amapempha kwa Allah Ta\u2018ala kuti mzimu odzipereka uwu ukwere kudzera pakhomo lake.<\/p>\n<p>Mzimu wa osakhulupirira ukatulutsidwa, umatuluka ndi mitsempha (kutanthauza kuti udzatuluka m&#8217;mitsempha yonse ya thupi lake). Mngelo aliyense pakati pa mitambo ndi dziko lapansi, ndi mngelo aliyense kumtambo ulionse, amamutemberera. Zitseko zakumwamba zimatsekedwa, ndipo angelo a khomo lililonse amapempha kwa Allah Ta\u2018ala kuti mzimu wake usakwere kudzera khomo lake.<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-6\" class=\"aya selected\">\u064a\u064e\u0648\u0652\u0645\u064e \u062a\u064e\u0631\u0652\u062c\u064f\u0641\u064f \u0627\u0644\u0631\u0651\u064e\u0627\u062c\u0650\u0641\u064e\u0629\u064f\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0666\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-7\" class=\"aya\">\u062a\u064e\u062a\u0652\u0628\u064e\u0639\u064f\u0647\u064e\u0627 \u0627\u0644\u0631\u0651\u064e\u0627\u062f\u0650\u0641\u064e\u0629\u064f\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0667\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-8\" class=\"aya\">\u0642\u064f\u0644\u064f\u0648\u0628\u064c \u064a\u064e\u0648\u0652\u0645\u064e\u0626\u0650\u0630\u064d \u0648\u064e\u0627\u062c\u0650\u0641\u064e\u0629\u064c\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0668\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-9\" class=\"aya\">\u0623\u064e\u0628\u0652\u0635\u064e\u0627\u0631\u064f\u0647\u064e\u0627 \u062e\u064e\u0627\u0634\u0650\u0639\u064e\u0629\u064c\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0669\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-10\" class=\"aya\">\u064a\u064e\u0642\u064f\u0648\u0644\u064f\u0648\u0646\u064e \u0623\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e\u0627 \u0644\u064e\u0645\u064e\u0631\u0652\u062f\u064f\u0648\u062f\u064f\u0648\u0646\u064e \u0641\u0650\u064a \u0627\u0644\u0652\u062d\u064e\u0627\u0641\u0650\u0631\u064e\u0629\u0650\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0660\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-11\" class=\"aya\">\u0623\u064e\u0625\u0650\u0630\u064e\u0627 \u0643\u064f\u0646\u0651\u064e\u0627 \u0639\u0650\u0638\u064e\u0627\u0645\u064b\u0627 \u0646\u0651\u064e\u062e\u0650\u0631\u064e\u0629\u064b\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0661\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-12\" class=\"aya\">\u0642\u064e\u0627\u0644\u064f\u0648\u0627 \u062a\u0650\u0644\u0652\u0643\u064e \u0625\u0650\u0630\u064b\u0627 \u0643\u064e\u0631\u0651\u064e\u0629\u064c \u062e\u064e\u0627\u0633\u0650\u0631\u064e\u0629\u064c\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0662\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-13\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e\u0645\u064e\u0627 \u0647\u0650\u064a\u064e \u0632\u064e\u062c\u0652\u0631\u064e\u0629\u064c \u0648\u064e\u0627\u062d\u0650\u062f\u064e\u0629\u064c\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0663\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-14\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0630\u064e\u0627 \u0647\u064f\u0645 \u0628\u0650\u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0627\u0647\u0650\u0631\u064e\u0629\u0650\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0664\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>(Mudzaukitsidwa) tsiku lomwe kugwedezeka Kudzachititsa Chilichonse kugwedezeka, (ndi) chinthu china chogwedeza pambuyo Pachimenecho (ndiko Kuwomba koyamba kwa lipenga). kuchitika, ndipo kudzatsatiridwa ndi kuwomba kwachiwiri kwa lipenga pambuyo pa zaka makumi anayi). Mitima (ya anthu), tsiku limenelo, idzanjenjemera, (ndipo) maso awo adzadzolika pansi (kuchita manyazi). Iwo (osakhulupirira) akumati, \u201cKodi tidzabwereradi mwakale (tidzaukitsidwa)? Bwanji! Ngakhale titakhala mafupa ovunda?\u201d Iwo amati, \u201cPamenepo, kudzakhala kubwerera kotayika.\u201d Kenako (kuwomba kwachiwiri kwa lipenga) kudzakhala kulira kwamphamvu kamodzi kokha (kwa phokoso), ndipo mwadzidzidzi, adzadzutsidwa (ndi kubweretsedwa ku chigwa cha Hashr kuti akaweruzidwe).<\/em><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-6\" class=\"aya selected\">\u064a\u064e\u0648\u0652\u0645\u064e \u062a\u064e\u0631\u0652\u062c\u064f\u0641\u064f \u0627\u0644\u0631\u0651\u064e\u0627\u062c\u0650\u0641\u064e\u0629\u064f\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0666\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-7\" class=\"aya\">\u062a\u064e\u062a\u0652\u0628\u064e\u0639\u064f\u0647\u064e\u0627 \u0627\u0644\u0631\u0651\u064e\u0627\u062f\u0650\u0641\u064e\u0629\u064f\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0667\ufd3e\u200f<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>(Mudzaukitsidwa) tsiku limene kugwedezeka kudzapangitsa chilichonse kugwedezeka mwamphamvu, (ndi) kugwedezeka kwina pambuyo pake.<\/em><\/p>\n<p>Mu vesi loyambayi, Allah Ta\u2018ala akukamba za kuwomba koyamba kwa lipenga komwe kudzachitike pa Tsiku la Qiyaamah, ndipo mu vesi lachiwiri, Allah Ta\u2018ala akunena za kuwomba kwachiwiri kwa lipenga komwe kudzachitike zaka makumi anayi pambuyo pa lipenga loyamba.<\/p>\n<p>Cholinga cha kuwomba koyamba kwa lipenga chidzakhala kupangitsa cholengedwa chilichonse chamoyo kufa, ndikuthetsa dziko lonse lapansi. Cholinga cha kuwomba kwachiwiri kwa lipenga chidzakhala kuukitsanso chilengedwe.<\/p>\n<p>Mu Charabu, mawu akuti <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u201c\u0631\u0627\u062c\u0641\u0629\u201d<\/span> amachokera ku liwu loyambira <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u201c\u0631\u062c\u0641\u201d<\/span> lomwe limatanthauza \u201ckugwedeza china chake\u201d.<br \/>\nNdi chifukwa chake, mu vesi yoyamba, kudzera mu liwu loti \u201c<span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u0631\u0627\u062c\u0641\u0629\u201d<\/span>, Allah Ta\u2018ala akusonyeza kugwedezeka komwe kudzachitike pa Tsiku la Qiyaamah. kugwedezekaku kukutanthauza kuwomba koyamba kwa lipenga, komwe chilichonse padziko lapansi chidzayamba kugwedezeka mwamphamvu, zomwe zidzapangitse kuti chilichonse chionongeke, chiwonongeke ndi kutheratu.<\/p>\n<p>Mu Charabu, mawu akuti <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u201c\u0631\u0627\u062f\u0641\u0629\u201d<\/span> amachokera ku liwu loyambira \u201c\u0631\u062f\u0641\u201d lomwe limatanthauza \u201ckutsatira kapena kubwera pambuyo pa china chake\u201d.<\/p>\n<p>Ndi chifukwa chake, mu vesi yachiwiri, kudzera mu liwu loti<span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\"> \u201c\u0631\u0627\u062f\u0641\u0629\u201d<\/span>, Allah Ta\u2018ala akusonyeza kuwomba kwachiwiri kwa lipenga komwe kudzachitike zaka makumi anayi pambuyo pa kuwomba koyamba kwa lipenga.<\/p>\n<p>Kutchuridwa mofanana kwa kuwomba koyamba ndi kwachiwiri kwa lipenga kwalembedwa mu vesi yotsatira ya Qur\u2019aan Majeed<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u0648\u064e\u0646\u064f\u0641\u0650\u062e\u064e \u0641\u0650\u064a \u0627\u0644\u0635\u0651\u064f\u0648\u0631\u0650 \u0641\u064e\u0635\u064e\u0639\u0650\u0642\u064e \u0645\u064e\u0646 \u0641\u0650\u064a \u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0645\u064e\u0627\u0648\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0648\u064e\u0645\u064e\u0646 \u0641\u0650\u064a \u0627\u0644\u0652\u0623\u064e\u0631\u0652\u0636\u0650 \u0625\u0650\u0644\u0651\u064e\u0627 \u0645\u064e\u0646 \u0634\u064e\u0627\u0621\u064e \u0627\u0644\u0644\u0651\u064e\u0647\u064f<span class=\"sign\">\u00a0\u06d6<\/span>\u00a0\u062b\u064f\u0645\u0651\u064e \u0646\u064f\u0641\u0650\u062e\u064e \u0641\u0650\u064a\u0647\u0650 \u0623\u064f\u062e\u0652\u0631\u064e\u0649\u0670 \u0641\u064e\u0625\u0650\u0630\u064e\u0627 \u0647\u064f\u0645\u0652 \u0642\u0650\u064a\u064e\u0627\u0645\u064c \u064a\u064e\u0646\u0638\u064f\u0631\u064f\u0648\u0646\u064e\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0666\u0668\ufd3e<\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndipo lipenga lidzaimbidwa (koyamba), ndipo adzakomoka onse akumwamba ndi Padziko lapansi (ndikumwalira), kupatura amene Allah wawafuna (monga Jannah, Jahannum ndi okhala kumeneko). Pambuyo pake, lidzaimbidwanso, ndipo mwadzidzidzi adzauka, uku akuyang&#8217;ana modabwa kuti chachitika ndi chani. (Surah Zumar v. 68)<\/em><\/p>\n<p>Mu Hadith ya Sunan Tirmizi, zanenedwa kuti pamene magawo awiri mwa atatu a usiku atapita, Rasulullah (sallallahu \u2018alaihi wasallam) adadzuka nati:<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 16pt;\">\u064a\u0627 \u0623\u064a\u0647\u0627 \u0627\u0644\u0646\u0627\u0633 \u0627\u0630\u0643\u0631\u0648\u0627 \u0627\u0644\u0644\u0647 \u0627\u0630\u0643\u0631\u0648\u0627 \u0627\u0644\u0644\u0647 \u062c\u0627\u0621\u062a \u0627\u0644\u0631\u0627\u062c\u0641\u0629 \u062a\u062a\u0628\u0639\u0647\u0627 \u0627\u0644\u0631\u0627\u062f\u0641\u0629 \u062c\u0627\u0621 \u0627\u0644\u0645\u0648\u062a \u0628\u0645\u0627 \u0641\u064a\u0647<\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>E inu anthu! Kumbukirani Allah, kumbukirani Allah Ta\u2018ala (kudzera mu salaah ndi kuchita ibaadah popeza Qiyaamah ikubwera posachedwa)! kugwedezeka kudzapangitsa chilichonse kugwedezeka mwamphamvu, (ndi) kugwedeza kwina pambuyo pake. Imfa idzabwera (kwa munthu aliyense) ndi chilichonse chomwe chili mkati mwake (monga zopweteka za imfa). (Musnad Ahmed #21241)<\/em><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u00a0<span id=\"79-10\" class=\"aya selected\">\u064a\u064e\u0642\u064f\u0648\u0644\u064f\u0648\u0646\u064e \u0623\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e\u0627 \u0644\u064e\u0645\u064e\u0631\u0652\u062f\u064f\u0648\u062f\u064f\u0648\u0646\u064e \u0641\u0650\u064a \u0627\u0644\u0652\u062d\u064e\u0627\u0641\u0650\u0631\u064e\u0629\u0650\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0660\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-11\" class=\"aya\">\u0623\u064e\u0625\u0650\u0630\u064e\u0627 \u0643\u064f\u0646\u0651\u064e\u0627 \u0639\u0650\u0638\u064e\u0627\u0645\u064b\u0627 \u0646\u0651\u064e\u062e\u0650\u0631\u064e\u0629\u064b\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0661\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-12\" class=\"aya\">\u0642\u064e\u0627\u0644\u064f\u0648\u0627 \u062a\u0650\u0644\u0652\u0643\u064e \u0625\u0650\u0630\u064b\u0627 \u0643\u064e\u0631\u0651\u064e\u0629\u064c \u062e\u064e\u0627\u0633\u0650\u0631\u064e\u0629\u064c\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0662\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>(Anthu osakhulupirira) akuyankhula kuti: \u201cKodi ndi zoona kuti ife tidzaukitsidwanso tikadzamwalira monga tidaliri kale? &#8220;Chani?, ngakhale titadzakhala kuti taola ndikutsala mafupa okhaokha?, akumati, ngati zidzakhale choncho ndiye kuti tidzakhala otaika.&#8221;<\/em><\/p>\n<p>M&#8217;mavesi awa, Allah Ta&#8217;ala akutidziwitsa za kuyankhula kosakhala bwino kwa osakhulupirira omwe adakana monyoza nkhani yokhudza kukhulupirira za kuuka kwa akufa ndi Qiyaamah. Sanathe kumvetsa momwe zingathekere kuukitsa matupi omwe adaola ndi kunyenyeka mpaka kusanduka fumbi.<\/p>\n<p>Poyankha mawu a osakhulupirirawa, Allah Ta&#8217;ala akunena kutsogolo kwa surah imeneyi momwe adalengera kumwamba ndi dziko lapansi, kutsindika pa munthu kuti pamene Allah Ta&#8217;ala ali ndi mphamvu zolenga zinthu zosiyanasiyana zodabwitsa monga kumwamba ndi dziko lapansi, zingamuvute bwanji kudzaukitsa munthu yemwe ali m&#8217;gulu la zolengedwa zophweka kwambiri poyerekeza ndi kalengedwe ka dzuwa, milalang&#8217;amba, ndi zina zotero?<\/p>\n<p>Allah Ta&#8217;ala akuti, &#8220;Kodi inuyo (anthu) ndi ovuta kwambiri (kwa Allah Ta&#8217;ala) kukulengani kapena kumwamba komwe adamanga? Iye adakweza kutalika kwake ndi kulongosora bwino, ndipo waphimba usiku wake ndi mdima, ndipo watulutsa (kuchokera mmenemo) kuwala kwake (zomwe ndi usana wake), ndipo pambuyo pake, Iye anayala dziko lapansi.&#8221;<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-13\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e\u0645\u064e\u0627 \u0647\u0650\u064a\u064e \u0632\u064e\u062c\u0652\u0631\u064e\u0629\u064c \u0648\u064e\u0627\u062d\u0650\u062f\u064e\u0629\u064c\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0663\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-14\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0630\u064e\u0627 \u0647\u064f\u0645 \u0628\u0650\u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0627\u0647\u0650\u0631\u064e\u0629\u0650\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0664\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-15\" class=\"aya\">\u0647\u064e\u0644\u0652 \u0623\u064e\u062a\u064e\u0627\u0643\u064e \u062d\u064e\u062f\u0650\u064a\u062b\u064f \u0645\u064f\u0648\u0633\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0665\ufd3e\u200f<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>(kulira kwachiwiri kwa lipenga) udzakhala nkuwo wamphamvu omwe udzamveke kamodzi kokha, ndipo mwadzidzidzi, adzadzutsidwa (ndi kubweretsedwa ku chigwa cha Hashr kuti aweruzidwe).<\/em><\/p>\n<p>Mawu oti <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u201c\u0633\u0627\u0647\u0631\u0629\u201d<\/span> amatanthauza \u201cpamwamba pa dziko lapansi\u201d. Qiyaamah ikachitika ndipo Allah Ta\u2018ala kuononga dziko lonse lapansi, Allah Ta\u2018ala adzapanganso dziko lapansi. Dziko lapansi latsopano limene Allah Ta\u2018ala adzalipangenso likutchulidwa mu vesi ili ndi mawu oti <span class=\"\" style=\"font-family: 'Traditional Arabic'; font-size: 14pt;\">\u201c\u0633\u0627\u0647\u0631\u0629\u201d<\/span>.<\/p>\n<p>Dziko latsopanoli likadzalengedwanso, lidzakhala malo okongola komanso osalala. Sipadzakhala mapiri, nyumba kapena chilichonse cha dziko lapansi lakale chomwe chingakhale zizindikiro zodziwika ndi kuperekedwa kwa umwini.<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u00a0<span id=\"79-15\" class=\"aya selected\">\u0647\u064e\u0644\u0652 \u0623\u064e\u062a\u064e\u0627\u0643\u064e \u062d\u064e\u062f\u0650\u064a\u062b\u064f \u0645\u064f\u0648\u0633\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0665\ufd3e\u200f<\/span><\/span><span id=\"79-16\" class=\"aya selected\">\u0625\u0650\u0630\u0652 \u0646\u064e\u0627\u062f\u064e\u0627\u0647\u064f \u0631\u064e\u0628\u0651\u064f\u0647\u064f \u0628\u0650\u0627\u0644\u0652\u0648\u064e\u0627\u062f\u0650 \u0627\u0644\u0652\u0645\u064f\u0642\u064e\u062f\u0651\u064e\u0633\u0650 \u0637\u064f\u0648\u064b\u0649\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0666\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-17\" class=\"aya\">\u0627\u0630\u0652\u0647\u064e\u0628\u0652 \u0625\u0650\u0644\u064e\u0649\u0670 \u0641\u0650\u0631\u0652\u0639\u064e\u0648\u0652\u0646\u064e \u0625\u0650\u0646\u0651\u064e\u0647\u064f \u0637\u064e\u063a\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0667\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-18\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0642\u064f\u0644\u0652 \u0647\u064e\u0644 \u0644\u0651\u064e\u0643\u064e \u0625\u0650\u0644\u064e\u0649\u0670 \u0623\u064e\u0646 \u062a\u064e\u0632\u064e\u0643\u0651\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0668\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-19\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0623\u064e\u0647\u0652\u062f\u0650\u064a\u064e\u0643\u064e \u0625\u0650\u0644\u064e\u0649\u0670 \u0631\u064e\u0628\u0651\u0650\u0643\u064e \u0641\u064e\u062a\u064e\u062e\u0652\u0634\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0661\u0669\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-20\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0623\u064e\u0631\u064e\u0627\u0647\u064f \u0627\u0644\u0652\u0622\u064a\u064e\u0629\u064e \u0627\u0644\u0652\u0643\u064f\u0628\u0652\u0631\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0660\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-21\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0643\u064e\u0630\u0651\u064e\u0628\u064e \u0648\u064e\u0639\u064e\u0635\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0661\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-22\" class=\"aya\">\u062b\u064f\u0645\u0651\u064e \u0623\u064e\u062f\u0652\u0628\u064e\u0631\u064e \u064a\u064e\u0633\u0652\u0639\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0662\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-23\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u062d\u064e\u0634\u064e\u0631\u064e \u0641\u064e\u0646\u064e\u0627\u062f\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0663\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-24\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0642\u064e\u0627\u0644\u064e \u0623\u064e\u0646\u064e\u0627 \u0631\u064e\u0628\u0651\u064f\u0643\u064f\u0645\u064f \u0627\u0644\u0652\u0623\u064e\u0639\u0652\u0644\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0664\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-25\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0623\u064e\u062e\u064e\u0630\u064e\u0647\u064f \u0627\u0644\u0644\u0651\u064e\u0647\u064f \u0646\u064e\u0643\u064e\u0627\u0644\u064e \u0627\u0644\u0652\u0622\u062e\u0650\u0631\u064e\u0629\u0650 \u0648\u064e\u0627\u0644\u0652\u0623\u064f\u0648\u0644\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0665\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-26\" class=\"aya\">\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e \u0641\u0650\u064a \u0630\u064e\u0670\u0644\u0650\u0643\u064e \u0644\u064e\u0639\u0650\u0628\u0652\u0631\u064e\u0629\u064b \u0644\u0651\u0650\u0645\u064e\u0646 \u064a\u064e\u062e\u0652\u0634\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0666\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Kodi nkhani ya Musah (\u2018alaihis salaam) siidakufikire? (Kumbukira) pamene Mbuye wake adamuitana ku chigwa chodala cha Tuwa; pita kwa Farao chifukwa wapyola malire . Kenako mufunse kuti, \u201cKodi ukufuna kuyeretsedwa ndikuti ndikutsogole kwa Mbuye wako kuti uzimuopa?\u201d Kenako adamuonetsa chozizwitsa chachikulu, koma adatsutsa ndipo sanamvere. Kenako anatembenuka kubwelera, akuyesetsa kulimbana naye (kumutsutsa Nabi Musah ( alayhis salaam). Kenako adasonkhanitsa (afiti) uku akuitana anthu ake nati, \u201cIne ndine Mbuye wanu Wapamwambamwamba.\u201d Choncho Allah Ta\u2018ala adamulanga , ndikumupanga kukhala chitsanzo cha chilango cha moyo omwe ulimkudza komanso cha dziko lino lapansi. Ndithudi, m\u2019menemo muli chizindikiro kwa onse oopa Allah Ta\u2018ala.<\/em><\/p>\n<p>Rasulullah (salallahu \u2018alaihi wasallam) ankakhudzika kwambiri ndi mawu a ma kuffaar omwe ankatsutsana ndi Qur\u2019aan Majeed ndipo ankakanira zoti kuli Qiyaamah. Pa chifukwa chimenechi, m\u2019mavesi awa, Allah Ta\u2018ala akumukhazikitsa mtima pansi Rasulullah (salallahu \u2018alaihi wasallam) potchula zomwe zidamuchitikira Nabi Musah (\u2018alaihis salaam) kwa Firaun, yemwenso adaukana uthenga wa Allah Ta\u2018ala pamene Nabi Musah (alaihis salaam) ankamuitanira ku Chisilamu.<\/p>\n<p>Mu kuyankhula kwina, Rasulullah (salallahu \u2018alaihi wasallam) akutonthozedwa ndi Allah Ta\u2018ala kuti vuto ili silinabwere kwa iwe wekha, koma Ambiyaa akale (\u2018alaihimus salaam) naonso adakumana ndi mavuto omwewa chifukwa cha deen. Choncho Allah Ta\u2018ala adamulanga ndi kumupanga kukhala chitsanzo cha chilango cha Tsiku Lomaliza komanso cha dziko lino lapansi lino.<\/p>\n<p>Mawu oti \u201c\u0646\u0643\u0627\u0644\u201d amatanthauza \u201cchilango choopsa kwambiri chomwe chimaperekedwa kwa yemwe wachita chigololo kuti kuchitira ena kuti asadzalakwitsenso chinthu chomwecho.\u201d<\/p>\n<p>Mawu oti \u201cchilango cha Aakhirah\u201d akutanthauza chilango cha Tsiku Lomaliza chomwe chidzaperekedwe kwa Fir\u2019aun. Mawu oti \u201cchilango cha dziko lapansi lino\u201d akutanthauza chilango chomwe chinaperekedwa kwa Fir\u2019aun ndi gulu lake lankhondo padziko lino lapansi momwe adaonongedwera ndi kumira.<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-27\" class=\"aya\">\u0623\u064e\u0623\u064e\u0646\u062a\u064f\u0645\u0652 \u0623\u064e\u0634\u064e\u062f\u0651\u064f \u062e\u064e\u0644\u0652\u0642\u064b\u0627 \u0623\u064e\u0645\u0650 \u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0645\u064e\u0627\u0621\u064f<span class=\"sign\">\u00a0\u06da<\/span>\u00a0\u0628\u064e\u0646\u064e\u0627\u0647\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0667\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-28\" class=\"aya\">\u0631\u064e\u0641\u064e\u0639\u064e \u0633\u064e\u0645\u0652\u0643\u064e\u0647\u064e\u0627 \u0641\u064e\u0633\u064e\u0648\u0651\u064e\u0627\u0647\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0668\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-29\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0623\u064e\u063a\u0652\u0637\u064e\u0634\u064e \u0644\u064e\u064a\u0652\u0644\u064e\u0647\u064e\u0627 \u0648\u064e\u0623\u064e\u062e\u0652\u0631\u064e\u062c\u064e \u0636\u064f\u062d\u064e\u0627\u0647\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0662\u0669\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-30\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0652\u0623\u064e\u0631\u0652\u0636\u064e \u0628\u064e\u0639\u0652\u062f\u064e \u0630\u064e\u0670\u0644\u0650\u0643\u064e \u062f\u064e\u062d\u064e\u0627\u0647\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0660\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-31\" class=\"aya\">\u0623\u064e\u062e\u0652\u0631\u064e\u062c\u064e \u0645\u0650\u0646\u0652\u0647\u064e\u0627 \u0645\u064e\u0627\u0621\u064e\u0647\u064e\u0627 \u0648\u064e\u0645\u064e\u0631\u0652\u0639\u064e\u0627\u0647\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0661\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-32\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0627\u0644\u0652\u062c\u0650\u0628\u064e\u0627\u0644\u064e \u0623\u064e\u0631\u0652\u0633\u064e\u0627\u0647\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0662\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-33\" class=\"aya\">\u0645\u064e\u062a\u064e\u0627\u0639\u064b\u0627 \u0644\u0651\u064e\u0643\u064f\u0645\u0652 \u0648\u064e\u0644\u0650\u0623\u064e\u0646\u0652\u0639\u064e\u0627\u0645\u0650\u0643\u064f\u0645\u0652\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0663\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Kodi inu (Inu anthu) ndi ovuta kwambiri kulenga (pamaso pa Allah Ta\u2019ala) kapena thambo limene Iye adalimanga posonkhanitsa mbali zake ngati kutalika kwake ndi kulikonza, ndipo adaphimba usiku wake ndi mdima, ndipo adatulutsa kuwala kwake (omwe ndi usana), ndipo pambuyo pake, adayala dziko lapansi. Iye adatulutsa madzi ake ndi udzu wake, ndi mapiri &#8211; Iye adawakhazikitsa (padziko lapansi), (zonsezi zidachitika) kuti zikuthandizeni (ndi kugwiritsa ntchito) komanso kuti ziweto zanu zipindule.<\/em><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u00a0<span id=\"79-33\" class=\"aya\">\u0645\u064e\u062a\u064e\u0627\u0639\u064b\u0627 \u0644\u0651\u064e\u0643\u064f\u0645\u0652 \u0648\u064e\u0644\u0650\u0623\u064e\u0646\u0652\u0639\u064e\u0627\u0645\u0650\u0643\u064f\u0645\u0652\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0663\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>(Zonsezi zinachitika) ndi cholinga choti zikupindulireni ( pogwiritsa ntchito) inuyo pamodzi ndi ziweto zanu .<\/em><\/p>\n<p>Mu ndime iyi, Allah Ta\u2018ala akufotokoza kuti Iye analiyala dziko lapansi, anachititsa kuti akasupe atuluke, anachititsa kuti mitsinje iziyenda, ndipo anabweretsa zabwino zake zobisika monga udzu, mitengo, ndi zipatso zomwe zimamera. Anakhazikitsanso mapiri ake kuti dziko lapansi likhale lokhanzikika bwino kuti anthu azikhala m&#8217;malo awo okhala. Zonsezi ndi njira yopindulira munthu. Munthu amadya ndi kusangalala ndi zabwino za dziko lapansi ndipo amapatsidwa ziweto zake kuti athe kupindula nazo ngati kudya kapena kukwera. Mwachidule, Allah Ta\u2018ala anapanga malo okhala padziko lapansi kukhala njira yomuthamdizira munthu, ndipo dongosolo la moyo uno lidzapitirira mpaka kumapeto kwa dziko lapansi.<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\">\u00a0<span id=\"79-34\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0630\u064e\u0627 \u062c\u064e\u0627\u0621\u064e\u062a\u0650 \u0627\u0644\u0637\u0651\u064e\u0627\u0645\u0651\u064e\u0629\u064f \u0627\u0644\u0652\u0643\u064f\u0628\u0652\u0631\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0664\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-35\" class=\"aya\">\u064a\u064e\u0648\u0652\u0645\u064e \u064a\u064e\u062a\u064e\u0630\u064e\u0643\u0651\u064e\u0631\u064f \u0627\u0644\u0652\u0625\u0650\u0646\u0633\u064e\u0627\u0646\u064f \u0645\u064e\u0627 \u0633\u064e\u0639\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0665\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-36\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0628\u064f\u0631\u0651\u0650\u0632\u064e\u062a\u0650 \u0627\u0644\u0652\u062c\u064e\u062d\u0650\u064a\u0645\u064f \u0644\u0650\u0645\u064e\u0646 \u064a\u064e\u0631\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0666\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-37\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0623\u064e\u0645\u0651\u064e\u0627 \u0645\u064e\u0646 \u0637\u064e\u063a\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0667\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-38\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0622\u062b\u064e\u0631\u064e \u0627\u0644\u0652\u062d\u064e\u064a\u064e\u0627\u0629\u064e \u0627\u0644\u062f\u0651\u064f\u0646\u0652\u064a\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0668\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-39\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e \u0627\u0644\u0652\u062c\u064e\u062d\u0650\u064a\u0645\u064e \u0647\u0650\u064a\u064e \u0627\u0644\u0652\u0645\u064e\u0623\u0652\u0648\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0669\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-40\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0623\u064e\u0645\u0651\u064e\u0627 \u0645\u064e\u0646\u0652 \u062e\u064e\u0627\u0641\u064e \u0645\u064e\u0642\u064e\u0627\u0645\u064e \u0631\u064e\u0628\u0651\u0650\u0647\u0650 \u0648\u064e\u0646\u064e\u0647\u064e\u0649 \u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0641\u0652\u0633\u064e \u0639\u064e\u0646\u0650 \u0627\u0644\u0652\u0647\u064e\u0648\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0664\u0660\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-41\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e \u0627\u0644\u0652\u062c\u064e\u0646\u0651\u064e\u0629\u064e \u0647\u0650\u064a\u064e \u0627\u0644\u0652\u0645\u064e\u0623\u0652\u0648\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0664\u0661\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Choncho tsoka lalikulu likadzafika, tsiku limene munthu adzakumbukira zonse zomwe adachita ( zabwino ndi zoipa padziko lapansi), ndipo Moto wa Jahena udzaonetsedwa kuti onse aone, ndiye amene adapyora malire ndikusankha moyo wa dziko lapansi (kupitirira Moyo Womaliza), ndiye kuti Moto wa Jahena adzakhala malo ake okhalako. Ndipo amene ankaopa kuimilira pamaso pa Mbuye wake, ndipo anadziletsa ku zilakolako (zosaloredwa), ndiye kuti Jannah ndiye malo ake okhalako.<\/em><\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-35\" class=\"aya\">\u064a\u064e\u0648\u0652\u0645\u064e \u064a\u064e\u062a\u064e\u0630\u064e\u0643\u0651\u064e\u0631\u064f \u0627\u0644\u0652\u0625\u0650\u0646\u0633\u064e\u0627\u0646\u064f \u0645\u064e\u0627 \u0633\u064e\u0639\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0665\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p>Tsiku lomwe munthu adzakumbuikire zonse zomwe adachita (zabwino ndi zoipa).<\/p>\n<p>\u201cTsiku limene munthu adzakumbukira zonse zimene ankayesetsa kuchita\u201d likutanthauza tsiku la chiweruzo kumene munthu adzaganizira ntchito zake zonse, zabwino ndi zoipa. Mu vesi lina, Allah Ta\u2018ala akufotokozanso kuti, Nthawi imeneyo munthu adzakumbukira, ndipo ndithudi, ali ndi kukumbukira.<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-37\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0623\u064e\u0645\u0651\u064e\u0627 \u0645\u064e\u0646 \u0637\u064e\u063a\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0667\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-38\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0622\u062b\u064e\u0631\u064e \u0627\u0644\u0652\u062d\u064e\u064a\u064e\u0627\u0629\u064e \u0627\u0644\u062f\u0651\u064f\u0646\u0652\u064a\u064e\u0627\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0668\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-39\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e \u0627\u0644\u0652\u062c\u064e\u062d\u0650\u064a\u0645\u064e \u0647\u0650\u064a\u064e \u0627\u0644\u0652\u0645\u064e\u0623\u0652\u0648\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0663\u0669\ufd3e\u200f<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndipo amene adapyora malire ndikusankha moyo wa dziko lapansi (kusiya omwe ulinkudza), ndiye kuti kumoto ndikomwe adzakafikire ndikukhala malo ake okhalako.<\/em><\/p>\n<p>Mu ndime iyi Allah Ta&#8217;ala, akufotokoza malo okakhala anthu osakhulupirira omwe sanamumvere Allah ndipo anasankha moyo wa dziko lapansi kuposa omwe ulinkudza. Mu kuyankhula kwina, adakonda zabwino za dziko lapansi kuposa chipembedzo ndipo sanakhulupirire mwa Allah, kotero malo ake omaliza adzakhala ku moto wa Jahannam ndipo chakudya chake chidzakhala zaquum (mtengo waminga waku jahannum) ndipo chakumwa chake chidzakhala hameem (madzi otentha aku jahannum).<\/p>\n<p class=\"\" dir=\"RTL\" style=\"text-align: center; font-family: usmaan_taha; font-size: 16pt; line-height: 38px;\"><span id=\"79-40\" class=\"aya\">\u0648\u064e\u0623\u064e\u0645\u0651\u064e\u0627 \u0645\u064e\u0646\u0652 \u062e\u064e\u0627\u0641\u064e \u0645\u064e\u0642\u064e\u0627\u0645\u064e \u0631\u064e\u0628\u0651\u0650\u0647\u0650 \u0648\u064e\u0646\u064e\u0647\u064e\u0649 \u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0641\u0652\u0633\u064e \u0639\u064e\u0646\u0650 \u0627\u0644\u0652\u0647\u064e\u0648\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0664\u0660\ufd3e\u200f<\/span><\/span>\u00a0<span id=\"79-41\" class=\"aya\">\u0641\u064e\u0625\u0650\u0646\u0651\u064e \u0627\u0644\u0652\u062c\u064e\u0646\u0651\u064e\u0629\u064e \u0647\u0650\u064a\u064e \u0627\u0644\u0652\u0645\u064e\u0623\u0652\u0648\u064e\u0649\u0670\u00a0<span class=\"ayaNumber\">\u200e\ufd3f\u0664\u0661\ufd3e<\/span><\/span><\/p>\n<p style=\"text-align: center;\"><em>Ndipo amene ankaopa kudzaima pamaso pa Ambuye wake (kuti apereke kaundura wa tchito zake) ndi kudziletsa ku zilakolako zoipa ndi zosapeweka, ndiye kuti Paradaiso adzakhala malo ake okhalako.<\/em><\/p>\n<p>Mu ndime iyi, Allah Ta\u2018ala akufotokoza malo omwe akakhale anthu okhulupirira omwe ankaopa Allah m&#8217;moyo uno wa padziko lapansi ndipo amene ankaopa kudzaima pamaso pa Allah kuti apereke kau dura wake Tsiku Lomaliza.<\/p>\n<p>Kuopa kumeneku kwa mlandu pa tsiku lomaliza kunawaletsa kukwaniritsa zilakolako zawo zakuthupi m&#8217;njira za haraam ndipo kunawapangitsa kukumbukira Allah Ta&#8217;ala ndikukhala omvera kwa Iye moyk wawo onse. Kwa akapolo otere, Allah Ta&#8217;ala akunena kuti malo awo omaliza ndi komwe akupita adzakhala paradaiso omwe Allah Ta&#8217;ala waakonzera akapolo Ake opaturika.<\/p>\n<p>Mu Hadith ya Mtumiki swallallahu alaihi wasallam zanenedwa kuti kupatula madalitso omwe afotokozedwa (mu Qur\u2019aan ndi Sunnah,) madalitso a Jannah ndi kufotokozera kwake ndi oti palibe diso lomwe lidawonako, palibe khutu lomwe lidamvapo, ndipo palibe munthu amene anaganizirako za zosangalatsa zake. (Saheeh Bukhaari #4780)<\/p>\n","protected":false},"excerpt":{"rendered":"<p>\u0648\u064e\u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0627\u0632\u0650\u0639\u064e\u0627\u062a\u0650 \u063a\u064e\u0631\u0652\u0642\u064b\u0627\u00a0\u200e\ufd3f\u0661\ufd3e\u200f\u00a0\u0648\u064e\u0627\u0644\u0646\u0651\u064e\u0627\u0634\u0650\u0637\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0646\u064e\u0634\u0652\u0637\u064b\u0627\u00a0\u200e\ufd3f\u0662\ufd3e\u200f\u00a0\u0648\u064e\u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0627\u0628\u0650\u062d\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0633\u064e\u0628\u0652\u062d\u064b\u0627\u00a0\u200e\ufd3f\u0663\ufd3e\u200f\u00a0\u0641\u064e\u0627\u0644\u0633\u0651\u064e\u0627\u0628\u0650\u0642\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0633\u064e\u0628\u0652\u0642\u064b\u0627\u00a0\u200e\ufd3f\u0664\ufd3e\u200f\u00a0\u0641\u064e\u0627\u0644\u0652\u0645\u064f\u062f\u064e\u0628\u0651\u0650\u0631\u064e\u0627\u062a\u0650 \u0623\u064e\u0645\u0652\u0631\u064b\u0627\u00a0\u200e\ufd3f\u0665\ufd3e Ndikulumbirira (angelo) amene amachotsa (mizimu ya osakhulupirira) mwaukali, ndi (angelo) amene amachotsa (miyoyo ya okhulupirira) moleza, ndi (Angelo) amene amasambira nayo mizimuyo (m\u2019mlengalenga), ndi (Angelo) amene amapikisana (kukwaniritsa malamulo a Allah Ta\u2019ala). Monga ziliri kuti Sura Nabai idavumbulutsidwa kuti idzakhazikitse chikhulupiriro cha tsiku la Qiyaamah, momwemonso surayi idavumbulutsidwa kuti &hellip;<\/p>\n","protected":false},"author":3,"featured_media":3262,"comment_status":"closed","ping_status":"open","sticky":false,"template":"","format":"standard","meta":{"footnotes":""},"categories":[20],"tags":[],"class_list":["post-3745","post","type-post","status-publish","format-standard","has-post-thumbnail","","category-tafseer"],"_links":{"self":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts\/3745","targetHints":{"allow":["GET"]}}],"collection":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts"}],"about":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/types\/post"}],"author":[{"embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/users\/3"}],"replies":[{"embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Fcomments&post=3745"}],"version-history":[{"count":14,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts\/3745\/revisions"}],"predecessor-version":[{"id":3774,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/posts\/3745\/revisions\/3774"}],"wp:featuredmedia":[{"embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=\/wp\/v2\/media\/3262"}],"wp:attachment":[{"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Fmedia&parent=3745"}],"wp:term":[{"taxonomy":"category","embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Fcategories&post=3745"},{"taxonomy":"post_tag","embeddable":true,"href":"https:\/\/ny.alislaam.com\/index.php?rest_route=%2Fwp%2Fv2%2Ftags&post=3745"}],"curies":[{"name":"wp","href":"https:\/\/api.w.org\/{rel}","templated":true}]}}