Monthly Archives: June 2024

Surah Zokhala ndi nthawi zake zowerenga komanso nthawi zake zosiyanasiyana zomwe zikuyenera kuwerenga 4

9. Werenganinso ayah zitatu zomaliza za Surah Baqarah musanagone. Kwanenedwa kuti Ali (Radhwiyallahu anhu) adati: “Sindikuganiza kuti aliyense wanzeru angagone popanda kuwerenga ma aya (atatu) omaliza a Surah Baqarah, chifukwa ndithu iwowo ndi chuma chochokera pansi pa Arsh. 10. Werengani Surah Faatihah ndi Surah Ikhlaas musanagone. Anas (Radhwiyallahu anhu) akusimba …

Read More »

Surah Zokhala ndi nthawi zake zowerenga komanso nthawi zake zosiyanasiyana zomwe zikuyenera kuwerenga 3

6. werengani Surah Sajdah musanagone. Olemekezeka Jaabir (Radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) sankagona mpaka atawerenga Surah Sajdah ndi Surah Mulk.[1] Khaalid bin Ma’daan rahimahullah, Taabi’ee, adatchula izi: “Ndithu Surah Sajdah idzakangana m’manda poteteza amene ankaiwerenga. Idzati, ‘O, Allah! Ngati ndili ochokera ku chitaab Chanu, muvomereni chiwombolo changa …

Read More »

Kulandira dzina loti ‘Mthandizi Wapadera’ wa Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam)

Pankhondo ya Ahzaab, yomwe imadziwikanso kuti Nkhondo ya Khandaq (Nkhondo ya Ngalande), Asilamu adalandira uthenga kuti Banu Quraizah adaswa lonjezo lawo loti adzakhulupirika kwa Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) ndipo adajoina adani. Kuti atsimikize zomwe zamvekazi, Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) adawafunsa ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) kuti: “Ndani andibweretsere nkhani za anthu …

Read More »