Masunna Ndi Aadaab (Miyambo)

Ma Sunnah Komanso Miyambo Ya Jumu’ah 4

11. Werengani durood mochuluka. Olemekezeka Aws bin Aws radhwiyallahu anhu akufotokoza kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) adati: “Masiku abwino kwambiri ndi tsiku la Jumuah. 12. Yesetsani kuwerenga duruud chikwi chimodzi (ka 1000) tsiku la Jumuah. Olemekezeka Anas radhwiyallahu anhu akusimba kuti Mtumiki swallallahu alaihi wasallam adati: “Amene amawerenga duruud pa …

Read More »

Ma Sunnah Komanso Miyambo Ya Jumu’ah 3

9. Ngati n’kotheka, yendani wapansi popita ku musjid kukaswali swalaah ya Jumu’ah. Phanzi lirilonse lomwe mungaponye, mudzalandira mphotho ya kusala kudya kwa chaka chimodzi ndi Tahajjud. Olemekezeka Aws bin Aws Thaqafi radhwiya-Allah anhu akuti, “Ndidamva Rasulullah swallallahu alaihi wasallam akunena kuti, ‘Munthu amene amachita ghusl tsiku la Jumu’ah ndipo amapita …

Read More »

Ma Sunnah Komanso Miyambo Ya Jumu’ah 2

8. Pitani mwamsanga ku mzikiti kukaswali Jumu’ah, momwe mungapitire mwamsanga ndi momweso mungalandilire mphotho yochuluka. Olemekezeka Abu Hurairah radhwiya-Allahu ‘anhu akusimba kuti Rasulullah swallallahu alaihi wasallam adati, “Amene amasamba ngati momwe amasambira akakhala ndi janaabah (i.e. amasamba mosamaritsa monga momwe amachitira akakhala ndi janaabah), ndikupita ku Jumu’ah Salaah moyambilira, amalandira …

Read More »

Ma Sunnah Komanso Miyambo Ya Jumu’ah 1

1. Werengani Surah Dukhaan Lachinayi usiku. Olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallah anhu) akunena kuti Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) adati, munthu amene amawerenga Surah Haa-meem Ad-Dukhaan usiku wa Jumu’ah ( Lachinayi usiku), machimo ake adzakhululukidwa.” 2. Sambani (ghusl) Lachisanu. Munthu amene amasamba Lachisanu, machimo ake ang’onoang’ono amakhululukidwa. Olemekezeka Abu Bakr Siddeeg (radhwiyallahj …

Read More »

Ubwino wa Jumuah

Kukhululukidwa Kwa Machimo kudzera mukuswali Jumuah Abu Hurairah (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) adati: “Machimo omwe achitika pakati pa Jumu’ah ziwiri, ngati sali machimo akuluakulu, Allah amakhululuka. Tsiku Lopatulika kwa Okhulupirira Ibnu Abbaas (radhwiyallahu anhuma) adanena kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) adati: “Tsiku ili (tsiku la Jumu’ah) …

Read More »

Jumuah

Tsiku la Jumu’ah ndi lofunikira kwambiri mu Chisilamu. Izi ndi zina mwa zabwino zazikulu za Allah pa Ummah uwu ndipo ndichinthu chodziwika bwino m’Chisilamu. Rasulullah (sallallahu ‘alaihi wasallam) adati: “Tsiku la Jumu’ah ndi sayyidul ayyaam (lomwe ndi mtsogoleri wa masiku onse), ndi tsiku lalikulu kwambiri (kuchokera m’masiku a msabata) pamaso …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 10

30. Popanga musaafah, ingogwirani manja a munthuyo, Palibe chifukwa chogwirana chanza ndikumavinitsa monga amachitira ma kuffaar. Chimodzimodzinso sizoyenera kupanga musaafahah uku ndikumapsopsona dzanja lake ndikumasisita pachifuwa chake popeza machitidwewa alibe maziko mu Dini. 31. Popanga musaafah, musagwire manja a munthu winayo momufinya mpaka kumupweteka. 32. Musafulumire kuchotsa manja anu mukapanga …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 9

27. Wina asapereke salaamu pomlonjera munthu amene si Msilamu. Ngati amene sali Msilamu apereka moni wa salaamu, ayankhe pongonena kuti “Wa alaik” (ndi pa inu), ndipo ngati ambiri omwe si Asilamu apereka salaam kwa munthu, ayenera kuyankha kuti “Wa alaikum” (ndi kwa inu nonse). 28. Akakumana Asilamu awiri, akamaliza salaam, …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 8

26. Ndi adab (makhalidwe a usilamu) kuti pamene munthu wina akuyenda, wina wakhala pansi, ndiye kuti oyendayo ayambe kupereka salaamu ndi kupereka moni. Chimodzimodzinso, pamene wina ali m’sitima yapamadzi ndipo wina akuyenda, ndiye kuti okwerayo ayenera kuyamba kupereka salamu ndi kupereka moni. Chimodzimodzinso, achichepere ayenera kupereka moni kwa akuluakulu, ndipo …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 7

21. Pamene mukudzithandiza, musapereke salaamu kwa munthu aliyense kapena kuyankha salamu ya munthu aliyense. Chimodzimodzinso, ngati munthu akudzithandiza, musamupatse salaamu. 22. Muyenera kupereka salaamu kwa akulu akulu anu modzichepetsa komaso ndi motsitsa mawu. 23. Ngati mwalonjeza kupereka salaamu ya munthu kwa wina, zimakhala Waajib kwa iwe kukwaniritsa lonjezo ndi kupereka …

Read More »