Nthawi ina, Arwa bint Uwais, neba wa Hazrat Said bin Zaid (Radhwiyallahu ‘anhu), adadza kwa Muhammad bin ‘Amr bin Hazm (Rahimahullah) ndi dandaulo lokhudza neba wake Hazrat Sa’eed bun Zaid (Radhwiyallahu ‘anhu). Ananena kuti adamanga khoma lake m’malo mwake ndipo adapempha Muhammad bin Amr (Rahimahullah) kuti apite kwa iye kuti …
Read More »Sayyiduna Sa’iid Ibn Zaid (Radhwiyallahu ‘anhu) Ayikidwa m’gulu la Otenga nawo gawo pa nkhondo ya Badr
Nkhondo ya Badr isanayambike, Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) atamva kuti gulu la ochita malonda la Ma Quraish, lolemedwa ndi chuma chawo, lachoka ku Shaam (Syria) ndipo likubwerera ku Makkah Mukarramah, adatumiza Talhah bin Ubaidullah ndi Sa’iid radhwiyallahu anhuma kuti akasonkhanitse uthenga okhudza Gululi. Izi zidachitika masiku khumi Rasulullah (Swalla …
Read More »Hazrat Abdur Rahmaan bin Auf (Radhiyallahu ‘anhu) Kusamalira akazi olemekezeka a Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) paulendo wa Hajj
Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adati: “Ndithu, amene angadzasamalire akazi anga ndikadzamwalira, ndiye munthu owona ndi owopa Allah. Atamwalira Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam), Olemekezeka Abdur Rahmaan bun Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) ankakhala myandikana ndi Azwaaj Mutahharaat (akazi olemekezeka a Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam)). …
Read More »Sayyiduna ‘Abdur Rahmaan bin ‘Auf (Radhiyallahu ‘anhu) apatsidwa Udindo osankha Khalifah.
Pambuyo pake, Sayyiduna “Umar (radhiyallahu ‘anhu) adapanga Shura (gulu la akuluakulu omwe azipanga ziganizo) lokhala ndi ma Swahaabah asanu ndi mmodzi otsatirawa: Ali (radhiyallahu ‘anhu), ‘Uthmaan (radhiyallahu ‘anhu), Zubair (radhiyah ‘anhu) Sa’d (Radhiyallahu ‘anhu) ndi Abdur Rahmaan bun ‘Auf (radhiyallahu ‘anhu). Pankhani ya ma Sahaabah asanu ndi mmodziwa (Radhiyallahu ‘anhum), …
Read More »Kuopa kwa Olemekezeka Abdur Rahman bin Auf (radhiyallahu ‘anhu) kufunsidwa
Naufal bin lyaas al Huzali (rahimahullah) adati: ‘Tikakhala pamodzi ndi Abdur Rahman bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu), ndi kukhala naye chifupi kodabwitsa kusangalatsirenji. Tsiku lina, anatitengera kunyumba kwake kuti tikadye, Titakhala pansi kuti tidye ndipo mbale ya chakudya ya nyama ndi mkate inaperekedwa pamaso pathu, iye adayamba kulira. Tidamufunsa: “Nchiyani chikukupangitsa …
Read More »Kulandira Uthenga Wabwino Wamwayi Ndi Chikhululukiro M’maloto
Usiku wina, Hazrat Abdur Rahmaan bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) adakomoka kwa nthawi yayitali chifukwa chakudwala kwake mpaka omwe anali pafupi naye adaganiza kuti mzimu wake wachoka. Anamuphimba ndi nsalu n’kuchokapo. Mkazi wake, Ummu Kulthum bint ‘Uqbah, nthawi yomweyo adapempha thandizo kwa Allah Ta’ala podekha ndi kuswali (monga talamulidwa kutero mu …
Read More »Abdur Rahmaan bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) agwiritsa ntchito Chuma chake pa nkhondo ya Tabuk.
Pamene Allah Ta’ala ankamulamula Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) kuti anyamuke ulendo wa ku Tabuk, ma Swahaabah ambiri adalibe kalikonse panthawiyo zoti athandizikirw kuyende ulendo wautali ndi wotopetsa, makamaka pamene ankayembekezera kukumana ndi gulu lankhondo lachiroma pankhondo yomwe inali ndi zida zokwanira komanso adalipo ambiri. Choncho pofuna kusonkhanitsa pamodzi ndi …
Read More »Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) Kusankha Abdur Rahmaan bin Auf (radhwiya Allahu ‘anhu) kukhala Mtsogoleri wa Asilikali pa nkhondo ya Dumatul Jandal.
M’chaka cha chisanu ndi chimodzi chioangireni Hijrah, m’mwezi wa Sha’baan, Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adalankhula ndi Abdur Rahmaan bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) nati kwa iye: “Konzekeretsa ulendo wako, popeza ndikufuna ndikutumize ku ulendo, mwina lero kapena mawa, Insha Allah. M’mawa mwake, Abdur Rahmaan bun Auf (Radhiyallahu ‘anhu) …
Read More »Mantha a Abdur Rahman bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) kuyankha mlandu ngakhale adawonongera chuma pa ntchito ya Dini.
Shu’bah (Rahimahullah) akuti: Nthawi ina Abdur Rahman bun Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) ankasala kudya ndipo nthawi ya iftaar, chakudya chinabweretsedwa kwa iye. Ataona chakudyacho, Abdur Rahman bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) adati: “Hamzah (Radhwiyallahu ‘anhu) adaphedwa chifukwa cha chikhulupiriro ndipo sitinapeze nsalu yokwanira sanda yake, ndipo anali wabwino kuposa ine. Mus’ab bin …
Read More »Kuwolowa manja kwa Abdur Rahmaan bin Auf (Radhiyallahu ‘anhu)
Miswar bin Makhramah (Radhwiyallahuanhu) akuti: Abdur Rahmaan bun Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) nthawi ina adagulitsa munda wa mpesa kwa Uthman (Radhwiyallahu ‘anhu) pamtengo wa ma dinari zikwi makumi anayi (40,000). Abdur Rahmaan (Radhwiya Allaahu ‘anhu) atalandira ndalamazo kuchokera kwa Uthmaan (Radhwiyallahu ‘anhu), nthawi yomweyo adazigawa kwa akazi odalitsika a Mtumiki (Swalla …
Read More »