Sahaabah

Kumapeto Kwa Moyo Wa Mu’aaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) Padziko Lapansi

Mtumiki (swallallahu ‘alayhi wasallam) adati, “Munthu amene amamwalira ndi mliri, amakhala wamwalira imfa ya shahid. Mu khilaafat ya Umar (radhwiyallahu ‘anhu), mliri wa Amwaas unakhudza Shaam m’chaka cha 17 pambuyo pa Hijrah. Mu mliriwu Abu Ubaidah (radhwiyallahu ‘anhu), mtsogoleri wa Asilamu ku Shaam, anakhudzidwa nawonso ndipo pambuyo pake anamwalira. Asanamwalire, …

Read More »

Makhalidwe Abwino a Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)

Farwah bin Nawfal akufotokoza kuti nthawi ina yake, Abdullah bin Masud (radhwiyallahu anhu) adalankhula za Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) ndipo ankamuyamikira kwambiri chifukwa cha zabwino zomwe anali nazo. Iye adati: إن معاذا كان أمة قانتا لله حنيفا “Ndithu, Muaaz (bin Jabal) adali ummah (mtsogoleri wlotsogolera ena kunjira yoongoka), pomwe …

Read More »

Mtumiki (Swallallahu ‘alaihi wasallam) asankha Mu’aaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) kukhala Bwanamkubwa wa Yemen

Rasulullah (Swallallahu ‘alaihi wasallam) pomutumiza Mu’aaz (radhwiyallahu ‘anhu) ku Yemen, adamufunsa kuti, “Ndi njira yanji yomwe udzatsatire ukamakapereka chigamulo pa nkhani za Asilamu?” Mu’aaz (Radhwiyallahu ‘anhu) adayankha kuti: “Ndidzagwiritsa ntchito Qur’aan.” Kenako Nabi (Swallallahu ‘alaihi wasallam) adamufunsa kuti: “Ngati lamulo silikupezeka mu Qur’aan udzatani?” Iye adayankha kuti, “Ndidzagwiritsa nctchito mahaadith …

Read More »

Kudziwa Kwambiri Dini kwa Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)

Abu Muslim Khowlaani (rahimahullah) akufotokoza kuti: “Ndinalowa mumzikiti wa Hims ndipo ndinaona gulu la anthu. Pakati pawo panali anzake makumi atatu ndi awiri a Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) omwe ankakambirana za mahadith kuchokera kwa Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam). Munkumanowu munali mnyamata, amene maso ake anali atapakidwa surma ndipo mano ake …

Read More »

Chikondi cha Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) kwa Sayyiduna Muaaz bin Jabal (radhiwyallahu ‘anhu)

Sayyiduna Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) akunena kuti nthawi ina, Nabi (Swallallahu alaihi wasallam) anagwira dzanja langa nati kwa ine, “O Muaaz!”, ndipo ine ndinayankha kuti, “Ndili pano kuti ndikutumikireni.” Rasulullah (Swallallahu alaihi wasallam) kenako anandiuza kuti, “Ndithudi, ndimakukonda (chifukwa cha Allah Ta’ala).” Muaaz bin Jabal (Radhwiyallahu ‘anhu) anayankha kuti, …

Read More »

Kupereka kwa Mu’aaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)

Nthawi ina,Olemekezeka Umar (radhwiyallahu ‘anhu) anatumiza ndalama zagolide mazana anayi kwa Abu ‘Ubaidah bin Jarraah (radhwiyallahu ‘anhu) ndipo analamula mthumwiyi kuti ikadikire pang’ono kuti aone zomwe achite nacho chumacho. Olemekezeka Abu Ubaydah (radhwiyallahu ‘anhu) atalandira ndalamazo, anati, “Allah amuchitire chifundo (kunena Umar).” Kenako anauza kapolo wake wamkazi kuti, “Tenga ndalama …

Read More »

Rasulullah (Swallallahu ‘alaihi wasallam) Amuitana Abdullah bin Mas’ud (radhwiyallahu ‘anhu) ku Moyo Osatha

Salamah bin Tammaam (rahimahullah) akufotokoza kuti: Masiku angapo Abdullah bin Mas’ud (radhiyallahu ‘anhu) asanamwalire, munthu wina adabwera kudzakumana naye. Atakumana naye, munthuyo anamuuza kuti, “Oh Ibnu Mas’ud! Usiku watha, ndinakulota. M’maloto, ndinamuona Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) atakhala pa guwa pomwe iwe unali pansi pake. “Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) anakulankhula nanu …

Read More »

Kusamalitsa kwakukulu Kwa Sayyiduna Abdullah bin Mas’ood (radhiyallahu ‘anhu) Potulutsa mahadith a Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam)

Ole.wkezeka ‘Amr bin Maimoon (rahimahullah) adafotokoza za kusamalitsa kwakukulu kwa Abdullah bin Mas’ood (radhiyallahu ‘anhu) pamene ankatulutsa mahaadith kuchokera kwa Rasulullah (ssallallahu alaihi wasallam). Adanena kuti, “Nthawi ina, Abdullah bin Mas’ood (radhiyallahu ‘anhu) atayamba kunena Hadith yochokera kwa Rasulullah (sallallahu alaihi wasallam), adagwidwa ndi mantha ndi nkhawa kotero kuti madontho …

Read More »

Hazrat Abdullah bin Mas’uud (radhiyallahu ‘anhu) ndi Izindikiri wake a Quraan Majiid

Shaqiiq bin Salamah (rahimahullah), ophunzira wa Abdullah bin Mas’uud (radhiyallahu ‘anhu), akunena kuti nthawi ina yake, Abdullah bin Mas’uud (radhiyallahu ‘anhu) adapereka khutbah. Mu khutbahmo adati, “Ndikulumbira qasam mwa Allah! Ndinaphinzira ma surah oposa makumi asanu ndi awiri a Quraan Kariim mwachindunji kuchokera kwa Rasulullah (sallallahu alaihi wasallam). Ndikulumbira m’dzina …

Read More »