Minda ya chikondi

Zotsatira Za Kuipa Kwa Vinyo. Mankhwala Ozunguza Ubongo Ndi Zoledzeretsa

Tikayerekeza dini ya Chisilamu ndi zipembedzo zakale, timapeza kuti Chisilamu sichinangolongosora machimo ndi ntchito zoipa kuti ndi haraam, komanso chinafotokoza njira zomwe zimatsogolera ku uchimo ndi zoipa ngati haraam. Izi zidachitika kuti zimuteteze munthu kuti asagwere mu uchimo. Taganizirani chitsanzo cha mowa chomwe chinali choloredwa m’zipembedzo zakale, koma chanenedwa kuti …

Read More »

Zinthu Zomwe Zimachititsa Kuti Mdalitso Wa Allah Uchoke

Kuipa Kojambula Zithunzi Tiku lina Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) kulibe ali koyenda, Bibi Aaishah adapachika katani yokhala ndi zithunzi za zinthu zamoyo pakhomo. Nthawiyo Sayyidah Aaishah (radhwiyallahu anha) sankadziwa kuti zithunzi za zinthu zamoyo zinali zoletsedwa. Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) atafika kunyumba kwake ndipo maso ake anagwera pa katanilo anakwiya …

Read More »

Tsiku La Chiweruzo – Tsiku Lodzakhudwa Kwa Anthu Ambiri

Mu Quraan Majid, Tsiku la Qiyaamah latchulidwa ndi mayina osiyanasiyana. Mayina ena mwa awa ndi “Tsiku la Mphotho ndi Kubwezera”, “Tsiku losonkhana”, “Tsiku la Kutayika ndi Kupindula” (lodzataika kwa osakhulupirira ndi la phindu kwa okhulupirira), ndi “Tsiku la Kukumana” (kutanthauza kukumana ndi Allah Talaa. Tikayang’ana mayina awa, timapeza kuti dzina …

Read More »

Kuyamika Pa Mdalitso Okhala Ndi Moyo

Dawuud bin Dinaar anali Imaam wamkulu pankhani ya Hadith komanso mphunzitsi wa ma Muhadditheen otchuka, monga Imaam shu’bah (rahimahullah) ndi Imaam Wakii (rahimahullah). Mkatikati mwa moyo wake kunadzabuka mliri ku Khuraasaan kumene ankakhala omwe udakhudza anthu ndipo ambiri adataya miyoyo yawo. Dawuud bin Dinaar (rahimahullah) anali m’gulu la omwe adagwidwa …

Read More »

Imaam Ahmad bin Hambal (rahimahulla) Kupindura kuchoka kwa Bishr Haafi (rahimahulla)

Nkhani yotsatirayi ikuunikira kumvetsetsa kwakuya kwa dini ndi ma’rifat (kuzindikirika) ya Allah Talaa zomwe Allah Talaa adamudalitsa nazo Bishr Haafi (rahimahulla) zomwe zidachititsa kuti mpaka Imam Ahmad (rahimahulla) amutsanzire: M’nthawi ya Imaam Ahmad bin Hambal (rahimahulla) kunali dotolo wina yemwe ankatchedwa kuti Abdur Rahmaan At-Tabeeb. Ankathandiza Imaam Ahmad bin Hambal …

Read More »

Munthu Olungama Kwambiri – Fudhail Bin Iyaaz Rahimahullah

Fudhail bun Iyaaz (Rahimahullah) aDali Muhaddith olemekezeka komanso oyera mtima wa m’nthawi yake. Allah Talaa adamdalitsa ndi ulemelero wapamwamba kwambiri mu Hadith kotero kuti ambiri mwa ma Muhadith otsogola, monga Abdullah bin Mubaarak, Sufyaan bun Uyainah ndi Imaam Shaafi’e (Rahimahullah) adafotokoza Hadith kuchokera kwa iye. Zanenedwa kuti Fudhail (Rahimahullah) asanadalitsidwe …

Read More »

Osataya Chiyembekezo Mu Kusinthika Kwa Munthu Aliyense

  Abdullah bin Maslamah Q’anabi (rahimahullah) anali m’gulu la ma Muhadditheen otsogola mu nthawi yake. Iye anali mtsogoleri wa ma Muhadditheen ambiri otchuka, ngati Imaam Bukhaari, Imaam Muslim ndi Imaam Abu Dawood (rahimahullah) Zikunenedwa kuti pachiyambi cha moyo wake, ankacheza ndi anthu oipa ndipo ankamwa mowa. Komabe, atakumana ndi Muhaddith …

Read More »

Nkhani Yokhudza Kulowa Chisilamu Kwa Sayyiduna Wahshi Radhwiyallahu Anhu

Pankhondo ya Uhud, chimodzi mwa zowawa zowawitsa zomwe zidamuchitikira Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) kudali kuphedwa kwa amalume ake okondedwa Sayyiduna Hamzah (radhwiyallahu anhu) Amene adamupha Hamzah sanali wina koma Wahshi bun Harb Nthawi imeneyo ndikuti asadakhale nsilamu, koma Allah Talaa pambuyo pake adamdalitsa ndi Imaan ndi ulemelero okhala Sahaabi. Nkhani …

Read More »

Ufulu Wa Anansi (Aneba)

Kuti dziko liziyenda bwino komanso mogwirizana, ndikofunikira kuti munthu aliyense alemekeze ufulu wa anthu ena. Ngati ufulu wa anthu siulemekezedwa ndi kukwaniritsidwa, ndiye kuti chisokonezo ndi mikangano zidzafalikira padziko lonse lapansi. Kuba ndi kulanda chuma kudzakhala paliponse ndipo kuponderezana ndi kuphwanya malamulo kudzakhala chinthu chotchuka kwambiri. Anthu adzapondereza ufulu wa …

Read More »

Kukhala Ndi Mtima Okhululukira Ena

Olemekezeka Waa’il bin Hujr (Radhwiya-Allahu anhu) adali Swahaaba otchuka wa Rasulullah (swallallah alaihi wasallam) yemwe ankachokera dela la Yemen ndipo adali ochokera ku banja lachifumu. Zanenedwa kuti atanyamuka ku Yemen kubwera ku Madinah Munawwarah kudzalowa Chisilamu, asadafike Rasulullah Allah adawadziwitsa ma Swahaabah kuti watsala pang’ono kufika. Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) …

Read More »