Rasulullah swallallahu alaihi wasallam anali olemekezeka kwambiri pa zolengedwa za Allah, Allah adamusankha kukhala Mtumiki Wake omaliza ndipo adamudalitsa ndi dini yolemekezeka kwambiri – dini ya Chisilamu yomwe ndi malamulo abwino kwambiri a moyo kuti munthu atsatire. Munthu akalingalira pa umunthu odalitsika wa Rasulullah swallallahu alaihi wasllam amapeza kuti Allah …
Read More »Chilungamo Cha Sheikh Abdul Qadir Jeelani (rahimahullah)
Sheikh Abdul Qaadir Jeelani (rahimahullah) anali Aalim ndi Wali wa Allah Ta‘ala yemwe anakhalapo m’zaka za mma 600 A.H. Allah Ta‘ala adamudalitsa ndi kulandiridwa kwakukulu kotero kuti anthu ambiri adasintha miyoyo yawo ndi iye. Khalidwe limodzi lodziwika bwino lomwe lidawonekera m’moyo wake linali chilungamo (kuyankhula chilungamo). Pansipa pali nkhani yomwe …
Read More »Kukhala Ndi Nkhawa Pa Maphunziro A Dini A Mwana
Fuko lodalitsidwa ndi maphunziroo a Dini ndi kumvetsetsa komveka bwino komanso ndi fuko lopita chitsogolo komanso lachitukuko lomwe lili ndi tsogolo labwino. Mbali inayi, mtundu opanda maphunziro a Dini ndi kuzindikira koyenera ndi mtundu omwe ukupita kuchiwonongeko ndi kulephera. Ndichifukwa chake Nabi aliyense akatumizidwa ku fuko linalake, ndiye kuti imodzi …
Read More »Kufunikira Koti Mwana Adzicheza Ndi Anthu Abwino
Mu kulera mwana, ndi zofunika kwambiri kuti makolo azionetsetsa kuti mwana wawo nthawi zonse apezeka m’gulu la anthu ochita zabwino ndipo ndikupezeka malo abwino. Malo abwino komanso anthu opembedza adzasiya chikoka chokhanzikika pamtima wa mwanayo zomwe pambuyo pake zidzaumba kaganizidwe kake ndi kawonedwe kake ka moyo. Zotsatira zake, mwanayo adzakula …
Read More »Kumuzindikiritsa Mwana Kwa Allah
Kulera mwana n’kofunika kwambiri ndipo tingakuyerekezere ndi maziko a nyumba. Ngati maziko a nyumba ali olimba, ndiye kuti nyumbayo idzakhalanso yolimba ndipo idzapirira ku nyengo iliyonse. Mosiyana ndi zimenezi, ngati maziko a nyumbayo ndi ofooka komanso ogwedezekagwedezeka, ndiye kuti ndi kugwedezeka pang’ono, nyumbayo idzagwa. Chimodzimodzinso, kulera mwana ndiko maziko amene …
Read More »Ana Olungama – Cholowa Cha Tsiku Lachiweluzo
Zina mwa zabwino zamtengo wapatali za Allah pa munthu ndi mdalitso okhala ndi ana. Mdalitso okhala ndi ana ndi ena mwa Ni’ma yapadera ya Allah, zomwe zatchuridwa mu Quraan Majiid. Allah Akunena: وَاللَّهُ جَعَلَ لَكُم مِّنْ أَنفُسِكُمْ أَزْوَاجًا وَجَعَلَ لَكُم مِّنْ أَزْوَاجِكُم بَنِينَ وَحَفَدَةً وَرَزَقَكُم مِّنَ الطَّيِّبَاتِ Allah adakulengerani akazi …
Read More »Ubwino Osiya Pambuyo Mwana Olungama
Bambo a Nabii Yunus (alayhis salaam) adali munthu Owopa Allah dzina lawo Mattaa. Iwo ndi mkazi wawo kwa nthawi yaitali ankafuna kuti Allah atawadalitsa ndi mwana wamwamuna ndi kumuchita kukhala Mneneri kwa Bani Israeil. Zaka zambiri zidadutsa uku akumapempha mpaka pamapeto pake adaganiza zopita kukasupe odalitsika wa Nabii Ayyoob komwe …
Read More »Mzake wa Nabi Musah ‘Alaihis Salaam ku Jannah
M’chisilamu ntchito iliyonse yabwino ili ndi kuthekera kolumikizitsa munthu ndi Allah ndikumupezetsa sawabu ku umoyo omwe uli nkudza, komabe pali ntchito zina zimene ndi zapederadera pamanso pa Allah ndipo zimatha kukhala njira yopezera ubwino wa Dini yonse ndi ubwino wa dunya pamodzi. Zina mwa ntchito zimenezo ndi kuonetsa kukoma mtima …
Read More »Ntendere Waukulu Wa Allah Pa Akapolo Ndi Kukhala Makolo
Ena mwa madaritso aukuluakulu a Mulungu pa munthu, ndi mdaritso okhala ndi makolo. Mwayi okhalandi makolo ndi mdaritso ofunika kwambiri ndipo ulibe mlowa m’malo komanso umaperekedwa kwa munthu kamodzi kokha m’moyo wake. Monga momwe chisomo cha kukhala ndi moyo chimaperekedwa kamodzi kokha kwa munthu, ndipo chikatha sichidzabwereranso, momwemonso chisomo chokhala …
Read More »Nkhani Ya Munthu Wina Olungama, Olemekezeka Abdullah Bin Marzuuq (Rahimahullah)
Abdullah bin Marzuuq rahmatullah alaihi anali kapolo oopa Allah komanso anali m’nthawi ya ma Muhaddithiin akuluakulu monga Sufyaan bun Uyainah ndi Fudhail bun Iyaadh Rahimahumallah. Poyamba, iye anali okonda moyo wa dziko lapansi ndipo sanali odzipereka ku Dini. Komabe, Allah adamudalitsa ndi tawfiiq (kuthekera) koti alape ndi kukonza moyo wake. …
Read More »
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu