Pankhondo ya Uhud, chimodzi mwa zowawa zowawitsa zomwe zidamuchitikira Rasulullah swallallahu alaihi wasallam kudali kuphedwa kwa amalume ake okondedwa Sayyiduna Hamzah radhwiyallahu anhu Amene adamupha Hamzah sanali wina koma Wahshi bun Harb Nthawi imeneyo ndikuti asadakhale nsilamu, koma Allah Talaa pambuyo pake adamdalitsa ndi Imaan ndi ulemelero okhala Sahaabi. Nkhani …
Read More »Ufulu Wa Anansi (Aneba)
Kuti dziko liziyenda bwino komanso mogwirizana, ndikofunikira kuti munthu aliyense alemekeze ufulu wa anthu ena. Ngati ufulu wa anthu siulemekezedwa ndi kukwaniritsidwa, ndiye kuti chisokonezo ndi mikangano zidzafalikira padziko lonse lapansi. Kuba ndi kulanda chuma kudzakhala paliponse ndipo kuponderezana ndi kuphwanya malamulo kudzakhala chinthu chotchuka kwambiri. Anthu adzapondereza ufulu wa …
Read More »Kukhala Ndi Mtima Okhululukira Ena
Olemekezeka Waa’il bin Hujr (Radhwiya-Allahu anhu) adali Swahaaba otchuka wa Rasulullah (swallallah alaihi wasallam) yemwe ankachokera dela la Yemen ndipo adali ochokera ku banja lachifumu. Zanenedwa kuti atanyamuka ku Yemen kubwera ku Madinah Munawwarah kudzalowa Chisilamu, asadafike Rasulullah Allah adawadziwitsa ma Swahaabah kuti watsala pang’ono kufika. Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) …
Read More »Kufunira Ena Zabwino
Kuchokera mu dongosolo lonse la makhalidwe abwino la Chisilamu, makhalidwe onse omwe Chisilamu chimalimbikitsa ndi odzadza ndi zokopa ndipo amawalitsa kukongola. Kaya ndi kulemekeza okalamba, kapena kuchitira chifundo achinyamata, kapena kukwaniritsa ufulu wa makolo ndi abale anu, zonse zimasonyeza ulemerero wapadera wa Chisilamu. Komabe, moyo wa makhalidwe onse apamwambawa uli …
Read More »Makolo Kutsogolera Mwa Chitsanzo
Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) anali olemekezeka kwambiri pa zolengedwa za Allah, Allah adamusankha kukhala Mtumiki Wake omaliza ndipo adamudalitsa ndi dini yolemekezeka kwambiri – dini ya Chisilamu yomwe ndi malamulo abwino kwambiri a moyo kuti munthu atsatire. Munthu akalingalira pa umunthu odalitsika wa Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) amapeza kuti Allah …
Read More »Chilungamo Cha Sheikh Abdul Qadir Jeelani (rahimahullah)
Sheikh Abdul Qaadir Jeelani (rahimahullah) anali Aalim ndi Wali wa Allah Ta‘ala yemwe anakhalapo m’zaka za mma 600 A.H. Allah Ta‘ala adamudalitsa ndi kulandiridwa kwakukulu kotero kuti anthu ambiri adasintha miyoyo yawo ndi iye. Khalidwe limodzi lodziwika bwino lomwe lidawonekera m’moyo wake linali chilungamo (kuyankhula chilungamo). Pansipa pali nkhani yomwe …
Read More »Kukhala Ndi Nkhawa Pa Maphunziro A Dini A Mwana
Fuko lodalitsidwa ndi maphunziroo a Dini ndi kumvetsetsa komveka bwino komanso ndi fuko lopita chitsogolo komanso lachitukuko lomwe lili ndi tsogolo labwino. Mbali inayi, mtundu opanda maphunziro a Dini ndi kuzindikira koyenera ndi mtundu omwe ukupita kuchiwonongeko ndi kulephera. Ndichifukwa chake Nabi aliyense akatumizidwa ku fuko linalake, ndiye kuti imodzi …
Read More »Kufunikira Koti Mwana Adzicheza Ndi Anthu Abwino
Mu kulera mwana, ndi zofunika kwambiri kuti makolo azionetsetsa kuti mwana wawo nthawi zonse apezeka m’gulu la anthu ochita zabwino ndipo ndikupezeka malo abwino. Malo abwino komanso anthu opembedza adzasiya chikoka chokhanzikika pamtima wa mwanayo zomwe pambuyo pake zidzaumba kaganizidwe kake ndi kawonedwe kake ka moyo. Zotsatira zake, mwanayo adzakula …
Read More »Kumuzindikiritsa Mwana Kwa Allah
Kulera mwana n’kofunika kwambiri ndipo tingakuyerekezere ndi maziko a nyumba. Ngati maziko a nyumba ali olimba, ndiye kuti nyumbayo idzakhalanso yolimba ndipo idzapirira ku nyengo iliyonse. Mosiyana ndi zimenezi, ngati maziko a nyumbayo ndi ofooka komanso ogwedezekagwedezeka, ndiye kuti ndi kugwedezeka pang’ono, nyumbayo idzagwa. Chimodzimodzinso, kulera mwana ndiko maziko amene …
Read More »Ana Olungama – Cholowa Cha Tsiku Lachiweluzo
Zina mwa zabwino zamtengo wapatali za Allah pa munthu ndi mdalitso okhala ndi ana. Mdalitso okhala ndi ana ndi ena mwa Ni’ma yapadera ya Allah, zomwe zatchuridwa mu Quraan Majiid. Allah Akunena: وَاللَّهُ جَعَلَ لَكُم مِّنْ أَنفُسِكُمْ أَزْوَاجًا وَجَعَلَ لَكُم مِّنْ أَزْوَاجِكُم بَنِينَ وَحَفَدَةً وَرَزَقَكُم مِّنَ الطَّيِّبَاتِ Allah adakulengerani akazi …
Read More »
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu