Mu Quraan Majid, Tsiku la Qiyaamah latchulidwa ndi mayina osiyanasiyana. Mayina ena mwa awa ndi “Tsiku la Mphotho ndi Kubwezera”, “Tsiku losonkhana”, “Tsiku la Kutayika ndi Kupindula” (lodzataika kwa osakhulupirira ndi la phindu kwa okhulupirira), ndi “Tsiku la Kukumana” (kutanthauza kukumana ndi Allah Talaa. Tikayang’ana mayina awa, timapeza kuti dzina …
Read More »Makhalidwe Abwino a Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)
Farwah bin Nawfal akufotokoza kuti nthawi ina yake, Abdullah bin Masud (radhwiyallahu anhu) adalankhula za Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) ndipo ankamuyamikira kwambiri chifukwa cha zabwino zomwe anali nazo. Iye adati: إن معاذا كان أمة قانتا لله حنيفا “Ndithu, Muaaz (bin Jabal) adali ummah (mtsogoleri wlotsogolera ena kunjira yoongoka), pomwe …
Read More »Mtumiki (Swallallahu ‘alaihi wasallam) asankha Mu’aaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) kukhala Bwanamkubwa wa Yemen
Rasulullah (Swallallahu ‘alaihi wasallam) pomutumiza Mu’aaz (radhwiyallahu ‘anhu) ku Yemen, adamufunsa kuti, “Ndi njira yanji yomwe udzatsatire ukamakapereka chigamulo pa nkhani za Asilamu?” Mu’aaz (Radhwiyallahu ‘anhu) adayankha kuti: “Ndidzagwiritsa ntchito Qur’aan.” Kenako Nabi (Swallallahu ‘alaihi wasallam) adamufunsa kuti: “Ngati lamulo silikupezeka mu Qur’aan udzatani?” Iye adayankha kuti, “Ndidzagwiritsa nctchito mahaadith …
Read More »Kutuluka kwa Dajjaal ndi Ma Fitnah Ake Osiyanasiyana
Dajjaal akadzaonekera padziko lapansi, adzayamba kutulukira ndi kum’mawa kwa dziko, pakati pa Syria ndi Iraq. Pambuyo pake, adzapita ku Isfahaan komwe Ayuda 70,000 adzakhale naye limodzi. (Muslim #2944) Adzayenda padziko lonse lapansi, ndipo kulikonse komwe akupita, adzabweretsa fitnah yaikulu komanso ziphuphu zambiri. Malo awiri okha omwe sadzatha kulowamo ndi Makkah …
Read More »Kuyamika Pa Mdalitso Okhala Ndi Moyo
Dawuud bin Dinaar anali Imaam wamkulu pankhani ya Hadith komanso mphunzitsi wa ma Muhadditheen otchuka, monga Imaam shu’bah (rahimahullah) ndi Imaam Wakii (rahimahullah). Mkatikati mwa moyo wake kunadzabuka mliri ku Khuraasaan kumene ankakhala omwe udakhudza anthu ndipo ambiri adataya miyoyo yawo. Dawuud bin Dinaar (rahimahullah) anali m’gulu la omwe adagwidwa …
Read More »Kudziwa Kwambiri Dini kwa Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)
Abu Muslim Khowlaani (rahimahullah) akufotokoza kuti: “Ndinalowa mumzikiti wa Hims ndipo ndinaona gulu la anthu. Pakati pawo panali anzake makumi atatu ndi awiri a Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) omwe ankakambirana za mahadith kuchokera kwa Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam). Munkumanowu munali mnyamata, amene maso ake anali atapakidwa surma ndipo mano ake …
Read More »Sunnati Ndi Adaab 3
12. Ngati mungadzukire pakati pa usiku, werengani dua yotsatirayi ya masnun ndipo pambuyo pake mutha kupempha kwa Allah Talaa. Insha Allah, dua yanu idzalandiridwa. لَا إِلٰهَ إِلَّا اللهُ وَحْدَهُ لَا شَرِيْكَ لَهُ لَهُ الْمُلْكُ وَلَهُ الْحَمْدُ وَهُوَ عَلٰى كُلِّ شَيْءٍ قَدِيْرْ اَلْحَمْدُ لِلّٰهِ وَسُبْحَانَ اللهِ وَلَا إِلٰهَ إِلَّا اللهُ وَاللهُ …
Read More »Imaam Ahmad bin Hambal (rahimahulla) Kupindura kuchoka kwa Bishr Haafi (rahimahulla)
Nkhani yotsatirayi ikuunikira kumvetsetsa kwakuya kwa dini ndi ma’rifat (kuzindikirika) ya Allah Talaa zomwe Allah Talaa adamudalitsa nazo Bishr Haafi (rahimahulla) zomwe zidachititsa kuti mpaka Imam Ahmad (rahimahulla) amutsanzire: M’nthawi ya Imaam Ahmad bin Hambal (rahimahulla) kunali dotolo wina yemwe ankatchedwa kuti Abdur Rahmaan At-Tabeeb. Ankathandiza Imaam Ahmad bin Hambal …
Read More »Chikondi cha Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) kwa Sayyiduna Muaaz bin Jabal (radhiwyallahu ‘anhu)
Sayyiduna Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) akunena kuti nthawi ina, Nabi (Swallallahu alaihi wasallam) anagwira dzanja langa nati kwa ine, “O Muaaz!”, ndipo ine ndinayankha kuti, “Ndili pano kuti ndikutumikireni.” Rasulullah (Swallallahu alaihi wasallam) kenako anandiuza kuti, “Ndithudi, ndimakukonda (chifukwa cha Allah Ta’ala).” Muaaz bin Jabal (Radhwiyallahu ‘anhu) anayankha kuti, …
Read More »Muaaz (radhwiyallahu ‘anhu) Aswa fano la Amr bin Jamuuh (radhwiyallahu ‘anhu)
M’chaka cha 13 cha nubuwwat, anthu 70 ochokera ku Ansaar anabwera ku Hajj ndipo analowa Chisilamu pamaso pa Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam). Pakati pawo panali Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu) yemwe anali ochokera ku fuko la Banu Salimah la Ansaar, ndipo anali m’gulu la anthu oyambilira ku fuko lawo kulowa …
Read More »
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu