admin

Masaail (Nfundo) Zina Zokhudza Kuzithandiza Kuchimbudzi

1. Funso: kodi ndizoloredwa munthu kuwerenga mabukhu monga nyuzi ndi magazini, kapena kugwiritsa ntchito foni, kapenanso kuseweretsa intaneti pamene ali m’nchimbudzi?

Yankho: Chimbudzi ndi malo amene munthu amazithandizirako, Choncho sizabwino kwa munthu kugwiritsa ntchito foni yake kapena kuwerenga uthenga uliwonse kapena kuwerenga nkhani m'nchimbudzi.

Read More »

Kupeza Sawabu Zomasura Akapolo Okwana Khumi (10)

Sayyiduna Baraa bin Aazib (radhwiyallahu anhu) akunena kuti Nabi (sallallahu alaih wasallam) adati, "amene angandiwelengere Durood kamodzi, mmalo mwa Durood imeneyo Allah adzamulipira munthu ameneyo sawabu zokwana khumi adzamufufutira (adzamukhululukira) machimo okwana khumi adzamukwezera ulemelero wake ndimasiteji khumi komanso Durood yomwe adawerengayo idzakhala njira yomupatsa sawabu zomasura akapolo khumi.

Read More »

Kukhululukidwa Machimo

Sayyiduna Abu Burdah (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti, Nabi (sallallahu alaih wasallam) adati,” amene anganditumizire Durood mwa ummah wanga kuchokera pansi pa mtima, Allah adzamdalitsa munthu ameneyo pompatsa zifundo zokwana khumi, adzamukwezera ulemelero wake ndi masiteji okwana khumi ku Jannah, adzamulipira sawabu zokwana khumi ndikumukhululukira machimo okwana khumi.”

Read More »

Kapangidwe Ka Istinja (Kutawasa) Ka Sunnah ~ Gawo Lachisanu

16. Dzithandizeni mutanjuta pansi, ndi makuruhu (zonyasa) kudzithandiza choima.[1] عن عائشة رضي الله عنها قالت من حدثكم أن النبي صلى الله عليه وسلم كان يبول قائما فلا تصدقوه ما كان يبول إلا قاعدا (سنن الترمذي، الرقم: 12)[2] Sayyiduna Aishah (radhwiyallahu anha) akuti, amene angakuuzeni kuti Nabi (sallallahu alaih wasallam) ankadzithandiza …

Read More »

Ma Ulemelero Khumi Amakwezedwa

Sayyiduna Anas bin Maliki (radiyallah anhu) akusimba kuti, Nabi (salallah alayhi wasallam) adati; "Amene angandifunire ine zabwino kamodzi (popanga Durood), Allah Ta´ala adzamutumizira iyeyo madalitso khumi, machimo ake khumi adzakhululukidwa ndiponso levo yake ku Jannah idzakwezedwa ndi masiteji okwanira khumi".

Read More »

Nkhani Yabwino Yochoka Kwa Allah Ta’ala Kwa Awo Amene Amawerenga Durood

Sayyiduna Abdul Rahman bin Aufi (radhwiyallahu anhu) akunena kuti, tsiku lina Nabi (sallallahu alaih alaihi wasallam) adachoka kunyumba kwake ndipo ndidamulondora, kufikira mpaka adalowa m'munda wa tende nagwetsa nkhope yake pansi. Nabi (sallallahu alaihi wasallam) adakhala pasajdah kwanthawi yaitali mpaka ndidaganiza ngati Allah wachotsa nzimu wake. Kenaka ndidapita pafupi kuti ndikaone chomwe chanchitikira Nabi (sallallahu alaih wasallam). 

Read More »