Chikondi chomwe Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) ankamuonetsera Mtumiki (sallallahu alaih wasallam)

Makafiri ali pafupi kuti amuphe sahabah Olemekezeka Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) adamufunsa kuti ungasangalale kuti m’malo mwako timuphe Muhammad ndikuti iweyo tikusiye udzikasangalala ndi banja lako?

Yankho lake lodabwitsa lidali loti ndikulumbira mwa Allah sindingalore kuti ine ndikhale ndi banja langa kumasangalala ndipo Muhammad akuvutika ngakhale kutakhala kubaidwa ndi minga,

Atanva zimenezi Abu Sufyaan adayankha kuti “chikondi chimene maswahabah alinacho pa Mtumiki Muhammad (sallallahu alaih wasallam) sichingapezeke kwina kulikonse pa dziki lino lapansi.”

Check Also

Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu) aluza mano ake pa nkhondo ya Uhud

Pankhondo ya Uhud, Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adamenyedwa koopsa ndi adani ndipo mano awiri …