Chikondi chomwe Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) ankamuonetsera Mtumiki (sallallahu alaih wasallam)

Makafiri ali pafupi kuti amuphe sahabah Olemekezeka Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) adamufunsa kuti ungasangalale kuti m’malo mwako timuphe Muhammad ndikuti iweyo tikusiye udzikasangalala ndi banja lako?

Yankho lake lodabwitsa lidali loti ndikulumbira mwa Allah sindingalore kuti ine ndikhale ndi banja langa kumasangalala ndipo Muhammad akuvutika ngakhale kutakhala kubaidwa ndi minga,

Atanva zimenezi Abu Sufyaan adayankha kuti “chikondi chimene maswahabah alinacho pa Mtumiki Muhammad (sallallahu alaih wasallam) sichingapezeke kwina kulikonse pa dziki lino lapansi.”

Check Also

Kudziwa Kwambiri Dini kwa Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)

Abu Muslim Khowlaani (rahimahullah) akufotokoza kuti: “Ndinalowa mumzikiti wa Hims ndipo ndinaona gulu la anthu. …