Chikondi chomwe Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) ankamuonetsera Mtumiki (sallallahu alaih wasallam)

Makafiri ali pafupi kuti amuphe sahabah Olemekezeka Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) adamufunsa kuti ungasangalale kuti m’malo mwako timuphe Muhammad ndikuti iweyo tikusiye udzikasangalala ndi banja lako?

Yankho lake lodabwitsa lidali loti ndikulumbira mwa Allah sindingalore kuti ine ndikhale ndi banja langa kumasangalala ndipo Muhammad akuvutika ngakhale kutakhala kubaidwa ndi minga,

Atanva zimenezi Abu Sufyaan adayankha kuti “chikondi chimene maswahabah alinacho pa Mtumiki Muhammad (sallallahu alaih wasallam) sichingapezeke kwina kulikonse pa dziki lino lapansi.”

Check Also

Abu Zar (radhiyallahu ‘anhu) Apereka Uphungu kwa Mtsogoleri wa Asilikali Kuti Atsatire Chilungamo

Imaam Bayhaqi (rahimahullah) akunena kuti: Yazid bin Abi Sufyaan (radhiyallahu ‘anhu) pamene adali bwanamkubwa wa …