Hazrat Bilaal (Radhiya Allaahu ‘anhu) pa imfa yake

Pamene Hazrat Bilaal (Radhiya Allaahu ‘anhu) adatsala pang’ono kumwalira, mkazi wake adayamba kunena kuti: “Ha! Ndi zomvetsa chisoni bwanji! Mukuchoka m’dziko lino!”

Hazrat Bilaal (Radhiya Allahu anhu) anayankha kuti: “Zili zokondweretsa ndi zosangalatsa kuti mawa tikukakumana ndi abwenzi athu, tikakumana ndi Muhammad (Swalla Allaahu ‘alayhi wa sallam) ndi maswahaba ake.”

Check Also

Olemekezeka Abu Zar (Radhwiyallahu ‘anhu) Kulemekeza Alendo

‘Isa bin ‘Umailah (Rahimahullah) akufotokoza za munthu wina amene adawona khalidwe la Abu Zar (Radhwiyallahu …