Munthu Wabwino Kwambiri pa Ummah uwu

Hazrat Abu Dardaa radhiyallah anhu wanena kuti: “Nthaŵi ina yake, Mtumiki (Swallallaahu alaih wasallam). adandiona ndikuyenda kutsogolo kwa Hazrat Abu Bakr (Radhiyallahu ‘anhu) “Pamene Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) adaona izi, adandiuza kuti: “Usayende kutsogolo kwa amene ali wabwino kuposa iwe.

Pambuyo pake Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adafotokoza za ubwino waukulu wa Hazrat Abu Bakr (Radhiyallahu anhu). Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adati: “Abu Bakr (Radhiyallahu ‘anhu) ndi munthu wabwino kwambiri (mu Ummah uno) amene dzuwa lidamutulukira kapena kulowa”.

Check Also

Kudziwa Kwambiri Dini kwa Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)

Abu Muslim Khowlaani (rahimahullah) akufotokoza kuti: “Ndinalowa mumzikiti wa Hims ndipo ndinaona gulu la anthu. …