Kutengapo mbali pa Nkhondo ya Badr

Ismaa’eel bin Abi Khaalid akuti Bahiyy (Rahimahullah) adati: “Panali anthu apakavalo awiri okha omwe ankamenyana ndi adani pa nkhondo ya Badr. Wina adali Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) yemwe ankalimbana ndi adani kudzanja lamanja, ndipo winayo adali Miqdaad bun Aswad (Radhwiyallahu ‘anhu), yemwe ankamenya nkhondo kumanzere.

Hishaam bun Urwah akusimba kuti bambo ake Urwah (Rahimahullah) adati: “Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adali atavala nduwira yachikasu tsiku la Badr. Jibreel (‘alaihis salaan) kenako adatsika ali ndi maonekedwe a Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu). nayenso anali atavala nduwira yachikasu).”

Audio Player

Check Also

Mantha a Abdur Rahman bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) kuyankha mlandu ngakhale adawonongera chuma pa ntchito ya Dini.

Shu’bah (Rahimahullah) akuti: Nthawi ina Abdur Rahman bun Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) ankasala kudya ndipo nthawi …