Sahaabah

Dua ya Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) kumupangira Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu)

Abdullah bin Mas’uud (radhwiyallahu ‘anhu) akufotokoza kuti: Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) atachoka kupita ulendo wa ku nkhondo ya Tabuuk, anthu ena sanapite nawo paulendowo ndipo anasankha kutsala. Ambiri mwa anthuwa anali ma munaafiqiin (achipha maso). Maswahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) akamauza Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) za anthu omwe anatsala, Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi …

Read More »

Olemekezeka Abu Zar (Radhwiyallahu ‘anhu) Kulemekeza Alendo

‘Isa bin ‘Umailah (Rahimahullah) akufotokoza za munthu wina amene adawona khalidwe la Abu Zar (Radhwiyallahu ‘anhu) kwa anansi ake ndi alendo. Akunena kuti: “Nthawi iliyonse Abu Zar radhwiyallahu anhu akamakama mkaka wa mbuzi zake, poyamba ankagaira mkakawu anthu oyandikana nawo nyunba ndi alendo ake kuti ayambe amwa iwowo kenako ankamwa …

Read More »

Kulowa Chisilamu kwa Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu)

Khalidwe lake Asanalowe Chisilamu: Asanalowe Chisilamu, Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu) anali chigawenga. Anali olimba mtima kwambiri kotero kuti popanda kuthandizidwa ndi anzake ena, ankakwanitsa yekha kubera anthu ndikuwachita uchifwamba. Nthawi zina, ankaukira anthu apaulendo atakwera pahatchi, ndipo nthawi zina, ankaukira akuyenda pansi. (Siyar A’laam min Nubalaa 3/373) Pambuyo pake, anasiya …

Read More »

Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) Kubwerera ku Madina Munawwarah

́Allaamah Zurqaani (Rahimahullah) wapereka nkhani iyi kuchokera kwa Haafiz ibn ‘Asaakir (rahimahullah) ndi mndandanda wamphamvu wa osimba nkhani: Atamwalira Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam), zinali zovuta kwa olemekezeka Bilaal (radhwiyallahu ‘anhu) kupitiriza kukhala ku Madinah Munawwarah cha okondeka wake kwambiri Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) ndi …

Read More »

Dua ya Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) kuwapemphera chiongoko ma Quraish.

Olemekezeka ‘Urwah bun Zubair (rahimahullah) anasimba kuti mkazi wina wa m’banja la Banu Najjaar (yemwe ndi Nawwaar bint Maalik, mayi ake a Zaid bin Thaabit (radhwiyallahu ‘anhuma)) adati: “Nyumba yanga inali pamalo okwera ndipo inali imodzi mwa nyumba zapamwamba za Mus. “Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) ankaitana azaan ya Fajr kuchokera …

Read More »

Olemekezeka Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) Ayang’anira ndi Kusunga Mkondo wa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam)

Mfumu yaku Abysinia (Najaashi (rahimahullah)) nthawi ina inatumiza mikondo itatu kwa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) ngati mphatso. Atalandira mikondo itatu ija, Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) adapereka mkondo umodzi kwa Ali (radhwiyallahu ‘anhu), adapereka mkondo wachiwiri kwa Umar (Radhwiyallahu ‘anhu) ndipo adadzisungira yekha …

Read More »

Kumasuridwa kwa Hazrat Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) ndi Nabiy (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) kufuna kuti Hazrat Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) amasuridwe.

Nthawi ina pamene ankalankhula za Hazrat Bilaal (Radhiyallahu ‘anhu), Hazrat Sa’eed bun Musayyib (rahimahullah) adati: khumbo lofuna kulowa Chisilamu linali lalikulu kwambiri mu mtima mwa Hazrat Bilaal (radhwiyallahu ‘anhu). Adakumana ndi mavuto ndi mazunzo osalekeza kuchokera kwa anthu osakhulupirira. Nthawi zonse anthu osakhulupirira akafuna kumukakamiza kusiya Chisilamu, iye adali kukana …

Read More »

Olemekezeka Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) achita Azaan ku Shaam

‘Umar (Radhiyallahu ‘anhu) ulendo wina atapita ku Baitul Muqaddas m’nthawi ya Khilaafat yake, adayendera Jaabiyah (malo ena ake ku Shaam). Ali ku Jaabiyah anthu adadza kwa iye ndikumupempha ngati angamupemphe Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) yemwe ankakhala ku Shaam kuti awachitire azaan chifukwa iye adali muazzin wa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa …

Read More »

Olemekezeka Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) Msungichuma wa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam)

Olemekezeka Abdullah Al-Hawzani (rahimahullah) akufotokoza kuti nthawi ina adakumana ndi Bilaal (radhwiyallahu ‘anhu) ku Halab (mzinda wa Shaam). Atakumana ndi Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) adamufunsa kuti: “E, Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu)! Ndiuze momwe Nabiy (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) ankagwiritsira ntchito chuma chake (pa ntchito ya dini). Bilaal (Radhwiya Allaahu …

Read More »

Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) Aitana Azaan pa Ka’bah

Nthawi ya Fath-e-Makkah (Kugonjetsa kwa Makka), Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adalowa mu Ka’bah Shariif pamodzi ndi Bilaal (radhwiyallahu ‘anhu) komanso Usaamah (radhwiyallahu ‘anhu). Pa nthawiyo, Mzikiti udali odzadza ndi ma Quraishi omwe adali mmizeremizere, akumuyang’ana Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) kuti aone zimene achite ndi momwe awachite …

Read More »