Sahaabah

Kumwalira kwa Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu)

Olemekezeka Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu) atatsala pang’ono kumwalira, panalibe wina aliyense kupatula mkazi wake ndi kapolo wake. Anawalangiza kuti, “Mundisambitse ndi kundiveka sanda (ndikamwalira). Kenako tengani thupi langa ndi kuliyika pamsewu. Uzani gulu la anthu lomwe liyambilire kudutsa kuti, “Uyu ndi Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu),Otsatira wa Rasulullah (swallallahu ‘alayhi wasallam). …

Read More »

Olemekezeka Abu Zarr adzudzula wantchito wake

Tsiku lina munthu ochokera ku fuko la Banu Sulaim anabwera kwa Abu Zarr (radhwiyallahu anhu) ndipo anamuuza kuti: “Ndikufuna kukhala nanu kuti ndipindule ndi maphunziro anu a malamulo a Allah Ta’ala ndi ma sunnah a Nabi swallallahu alaihi wasallam Inenso ndidzathandiza wantchito wanu kusamalira ngamila.” Abu Zarr radhwiyallahu anhu anayankha …

Read More »

Olemekezeka Abu Zarr (radhwiyallahu ‘anhu) asamukira ku Shaam ndi Rabadhah

Zidatengera Abu Zarr Ghifaari (radhiyallahu ‘anhu) kuphunzira moyo wa Rasulullah (sallallahu ‘alaihi wasallam) osasamala za moyo wadziko lapansi komanso kudziletsa ndi kumvera machenjezo amphamvu kwa omwe ali ndi chuma koma osagwiritsa ntchito moyenera, Abu Zarr (radhwiyallahu ‘anhu) adayamba kudana ndi dziko lapansi kotero kuti sanasunge chuma ndipo sankakonda kuona anthu …

Read More »

Kusalilabadira kwa Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu) Ddziko Lapansi

Abu Zar Ghifaari (Radhwiyallahu ‘anhu) anali Sahaabi yemwe ankafanana ndi Nabiy Isa (‘alaihis salaam) m’maonekedwe ake komanso kukongola kwake. Rasulullah (sallallahu ‘alaihi wasallam) anati, “Aliyense amene akufuna kumuona Isa bin Maryam (‘alaihis salaam) Taqwa yake, chilungamo chake, ndi kudzipereka kwake (pa ibaadah), ayenera kumuyang’ana Abu Zar” (Majmauz Zawaaid #15817) Chimodzimodzinso, …

Read More »

Kutsatira kwa Abu Zar (radhiyallahu ‘anhu) Malangizo a Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam

Ma’roor bin Suwaid (rahimahullah) akufotokoza izi: Nthawi ina tinadutsa kwa Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu) ku Rabzah ndipo tinaona kuti anali atavala zovala ziwiri. Chimodzi chinali chakale, pomwe china chinali chatsopano, ndipo kapolo wake nayenso anali atavala zovala ziwiri, zomwe chimodzi chinali chatsopano ndipo china chinali chakale. Kenako tidati kwa Abu …

Read More »

Dua ya Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) kumupangira Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu)

Abdullah bin Mas’uud (radhwiyallahu ‘anhu) akufotokoza kuti: Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) atachoka kupita ulendo wa ku nkhondo ya Tabuuk, anthu ena sanapite nawo paulendowo ndipo anasankha kutsala. Ambiri mwa anthuwa anali ma munaafiqiin (achipha maso). Maswahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) akamauza Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi wasallam) za anthu omwe anatsala, Rasulullah (Sallallahu ‘alaihi …

Read More »

Olemekezeka Abu Zar (Radhwiyallahu ‘anhu) Kulemekeza Alendo

‘Isa bin ‘Umailah (Rahimahullah) akufotokoza za munthu wina amene adawona khalidwe la Abu Zar (Radhwiyallahu ‘anhu) kwa anansi ake ndi alendo. Akunena kuti: “Nthawi iliyonse Abu Zar radhwiyallahu anhu akamakama mkaka wa mbuzi zake, poyamba ankagaira mkakawu anthu oyandikana nawo nyunba ndi alendo ake kuti ayambe amwa iwowo kenako ankamwa …

Read More »

Kulowa Chisilamu kwa Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu)

Khalidwe lake Asanalowe Chisilamu: Asanalowe Chisilamu, Abu Zar (radhwiyallahu ‘anhu) anali chigawenga. Anali olimba mtima kwambiri kotero kuti popanda kuthandizidwa ndi anzake ena, ankakwanitsa yekha kubera anthu ndikuwachita uchifwamba. Nthawi zina, ankaukira anthu apaulendo atakwera pahatchi, ndipo nthawi zina, ankaukira akuyenda pansi. (Siyar A’laam min Nubalaa 3/373) Pambuyo pake, anasiya …

Read More »

Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) Kubwerera ku Madina Munawwarah

́Allaamah Zurqaani (Rahimahullah) wapereka nkhani iyi kuchokera kwa Haafiz ibn ‘Asaakir (rahimahullah) ndi mndandanda wamphamvu wa osimba nkhani: Atamwalira Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam), zinali zovuta kwa olemekezeka Bilaal (radhwiyallahu ‘anhu) kupitiriza kukhala ku Madinah Munawwarah cha okondeka wake kwambiri Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) ndi …

Read More »