Angelo Akukhamukira ku Misonkhano ya Zikr

عن عقبة بن عامر رضي الله عنه قال : قال رسول الله صلى الله عليه وسلم : إن للمساجد أوتادا جلساؤهم الملائكة إن غابوا فقدوهم وإن مرضوا عادوهم وإن رأوهم رحبوا بهم وإن طلبوا حاجة أعانوهم فإذا جلسوا حفت بهم الملائكة من لدن أقدامهم إلى عنان السماء بأيديهم قراطيس الفضة وأقلام الذهب يكتبون الصلاة على النبي صلى الله عليه وسلم ويقولون : اذكروا رحمكم الله زيدوا زادكم الله فإذا استفتحوا الذكر فتحت لهم أبواب السماء واستجيب لهم الدعاء وتطلع عليهم الحور العين وأقبل الله عز وجل عليهم بوجهه ما لم يخوضوا في حديث غيره ويتفرقوا فإذا تفرقوا أقام الزوار يلتمسون حلق الذكر (القربة لابن بشكوال، الرقم: 115، وسنده ضعيف كما في القول البديع صـ 257)

Hazrat Uqbah bin Aamir radhiyallahu anhu akusimba kuti Hazrat Rasulullah adati: “Ndithu, Misikiti ili ndi zikhomo (omwe ndi anthu odzipereka ku musjid, ochita ibaadah, monga ngati zikhomo zimakhomeredwa pansi). anthu oterowo, ngati atachoka ku Musjid, angelo amawasowa, ndipo ngati ali odwala, angelo amawachezetsa, ndipo angelo akawaona amawalandira, ndipo ngati angafunike, angelo amawathandiza kukwaniritsa zosowa zawo (Pamene ali (m’Msikiti kukumbukira Allah), kuwerenga kwa Duroud ndi zina zotero), Angelo amawazungulira kuyambira Kumiyendo yawo mpaka Kumwamba. Manja awo amene akulembera Duruud (yomwe ikuwerengedwa ndi anthu awa) Wonjezerani (zikr ndi Duruud) Allah akuonjezereni (zabwino)!” Pamene anthu awa ayamba kupanga zikr ya Allah, makomo akumwamba amatsekulidwa kwa iwo, mapemphelo awo amayankhidwa, anamwali aku Jannah akusuzumira pansi pawo, ndipo Allah amawaikira Chifundo Chake chapadera pokhapokha ngati Sachita china chilichonse, ndipo sakuchoka. Akachoka munzikiti , angelo amadzuka ndi kufunafuna Misonkhano ina ya zikr.

Chikondi Cha Sayyiduna Abu Bakr (radhwiyallahu anhu) Kumukonda Nabi (sallallahu alaih wasallam)

Nabi (sallallahu alaih wasallam) adawuyamba nsamuko pamodzi ndi Abu Bakr (radhwiyallahu) anhu chakumadzulo, nkatikati mwa ulendowu, nthawi zina Abu Bakr (radhwiyallahu anhu) ankayenda kutsogolo kwa Nabi (sallallahu alaih wasallam), ndipo nthawi zina ankayenda kumbuyo kwake, nthawi zina kumanja kwake ndipo nthawi zina kumanzere kwake.

Nabi (sallallahu alaih wasallam) atazindikira machitidwe achilendowa anamfusa iye kuti, oh Abu bakr! Ndikumakuona ukuyenda pena kutsogolo kwanga ndipo pena kumbuyo kwanga, nthawi zina kumanja kwanga pena kumanzere kwanga, ndichani chikukupangitsa iwe kuchita zimenezi? Sayyiduna Abu Bakr (radhwiyallahu anhu) adayankha nati: nthawi zonse maganizo akandifika oti adani atha kukubwererani kumbuyo kwanu, ndikumathamangira kumbuyo kwanu, ndipo mantha akandifika kuti nkutheka adani akubisalirani kutsogolo kwanu ndikumathamangira kutsogolo kwanu, chimodzimodzinso maganizo akandifika oti adani atha kubwera kudzera kumanja kwanu kapena kumanzere, ndikumapita mbali imeneyo.”

Nabi (sallallahu alaih wasallam) adati, oh Abu bakr! Ukulolera kuika moyo wako pachiswe chifukwa chaine? ndipo Abu Bakr adayankha nati,inde, kwabasi oh Nabi (sallallahu alaih wasallam), ndikulumbilira iye amene adakutumizani kukhala Nabi ndi chipembedzo chenicheni cha Chisilamu!” (Mustadrak Lil Haakim #4268)

Check Also

Kuwerenga Durood musanapange Dua

عن فضالة بن عبيد قال: بينا رسول الله صلى الله عليه وسلم قاعد إذ دخل …