Masunnah Ochita Mumzikiti

26 Osaipitsira mumzikiti. mwachitsanzo kulavulira mumzikiti kapena kumina mumzikiti mpaka zoipazo maminawo kapena malovuwo mkugwera pansi munzikiti.[1]

عن أبي ذر رضي الله عنه قال قال رسول الله صلى الله عليه وسلم عرضت علي أعمال أمتي حسنها وسيئها فوجدت في محاسن أعمالها الأذى يماط عن الطريق ووجدت في مساوئ أعمالها النخاعة تكون في المسجد لا تدفن (صحيح مسلم، الرقم: 553)

Olemekezeka Abuu Zar (radhiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (sallallahu alayhi wasallama); Ntchito zabwino ndi zoipa za ummat wanga zonse zidaonetsedwa kwa ine. ndinapeza kuti zina mwantchito zabwinozo ndi: munthu kuchotsa pamsewu chinthu chimene chingawapatse anthu vuto. Ndipo ndinapezanso kuti muntchito zoipazo ndi mamina amene asiyidwa osakwiliridwa mumzikiti. (amene adagwera pansi)

عن أنس رضي الله عنه قال قال رسول الله صلى الله عليه وسلم البزاق في المسجد خطيئة وكفارتها دفنها (صحيح البخاري، الرقم: 415)

Olemekezeka Anas (radhiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallah alayhi wasallama) adati; Kulavulira mumzikiti ndi tchimo, ndipo chindapusa chake (kulapa kwake) ndikuwakwilira ndi madothi. (Izi zidali munthawi imene swalah ankayipemphera padothi popanda choyalapo kanthu).


[1]

(سورة الحج: 32) وَمَن يُعَظِّمْ شَعَٰٓئِرَ ٱللَّهِ فَإِنَّهَا مِن تَقْوَى ٱلْقُلُوبِ

وَمَنْ أَظْلَمُ مِمَّن مَّنَعَ مَسَٰجِدَ ٱللَّهِ أَن يُذْكَرَ فِيهَا ٱسْمُهُۥ وَسَعَىٰ فِى خَرَابِهَآ أُو۟لَٰٓئِكَ مَا كَانَ لَهُمْ أَن يَدْخُلُوهَآ إِلَّا خَآئِفِينَ لَهُمْ فِى ٱلدُّنْيَا خِزْىٌ وَلَهُمْ فِى ٱلْـَٔاخِرَةِ عَذَابٌ عَظِيمٌ (سورة البقرة: 114)

اتفق الأصحاب على كراهة تشبيك الأصابع في طريقه إلى المسجد وفي المسجد يوم الجمعة وغيره، وكذا سائر أنواع العبث ما دام في الصلاة أو منتظرها لأنه في صلاة (المجموع شرح المهذب 4/391 ، مغني المحتاج 1/652)

ولا يشبك بين أصابعه ولا يفرقع في الطريق ولا في المسجد كما لا يفعل في الصلاة (التهذيب في فقه الإمام الشافعي 2/351)

Check Also

Masunnah Ochita Mumzikiti

27. Khalani mwaulemu ndi modekha pamene muli mumzikiti musakhale moiwala kulemekezeka kwa mzikiti. Anthu ena …