Olemekezeka Abu Bakr (Radhwiyallahu anhu) Kupereka Chuma Chake Kwa Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam)

Olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallah alayhi wasallam) adati: “Palibe chuma cha munthu chomwe chidandipindulira monga chuma cha Abu Bakr (radhiyallahu anhu), atamva izi olemekezeka Abu Bakr (radhwiyallahu anhu) adayamba kulira nati: “Chuma changa ndi zonse ndi zanu.

Pali nkhani ya olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallahu anhu) m’buku lotchedwa Musnad Ahmed, Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) adati: “Palibe chuma (cha munthu) chomwe chidandipindulira monga chuma cha Abu Bakr (radhiyallahu anhu), Abu Bakr (radhwiyallahu anhu) atamva izi anayamba kulira ndipo adati katatu: “Oh, Mtumiki wa Allah (swallallahu alaih wasallam)! Ndithudi, kupyolera mwa inu Allah wandidalitsa ine ndi chilichonse.”

Audio Player

Check Also

Mantha a Abdur Rahman bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) kuyankha mlandu ngakhale adawonongera chuma pa ntchito ya Dini.

Shu’bah (Rahimahullah) akuti: Nthawi ina Abdur Rahman bun Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) ankasala kudya ndipo nthawi …