Olemekezeka Abu Bakr (Radhwiyallahu anhu) Kupereka Chuma Chake Kwa Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam)

Olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallah alayhi wasallam) adati: “Palibe chuma cha munthu chomwe chidandipindulira monga chuma cha Abu Bakr (radhiyallahu anhu), atamva izi olemekezeka Abu Bakr (radhwiyallahu anhu) adayamba kulira nati: “Chuma changa ndi zonse ndi zanu.

Pali nkhani ya olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallahu anhu) m’buku lotchedwa Musnad Ahmed, Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) adati: “Palibe chuma (cha munthu) chomwe chidandipindulira monga chuma cha Abu Bakr (radhiyallahu anhu), Abu Bakr (radhwiyallahu anhu) atamva izi anayamba kulira ndipo adati katatu: “Oh, Mtumiki wa Allah (swallallahu alaih wasallam)! Ndithudi, kupyolera mwa inu Allah wandidalitsa ine ndi chilichonse.”

Check Also

Hazrat Abdullah bin Mas’uud (radhiyallahu ‘anhu) ndi Izindikiri wake a Quraan Majiid

Shaqiiq bin Salamah (rahimahullah), ophunzira wa Abdullah bin Mas’uud (radhiyallahu ‘anhu), akunena kuti nthawi ina …