Chilungamo cha Ali (radhwiyallahu ‘anhu)

Ali bun Rabii’ah akusimba kuti nthawi ina Ja’dah bin Hubairah (radhwiyallahu ‘anhu) adadza kwa Ali (radhwiyallahu ‘anhu) nati: “E inu Amiir-ul-Mu’miniin! Anthu awiri akabwera kwa inu (ndi mkangano wawo) Mmodzi mwa awiriwo amakukondani kwambiri kuposa banja lake ndi chuma chake, pomwe winayo ndi woti akadakhoza kukuphani, akadachita. choncho (chifukwa cha udani wake Pa inu) Koma ngakhale zili choncho, mumaweruza bwino mokomera amene akukudani, osati amene amakukondani.

Atamva izi Ali (radhwiyallahu ‘anhu) anamenya pang’ono pachifuwa cha Ja’dah. (radhwiyallahu ‘anhu) ndi dzanja lake (chifukwa cha chikondi ndi kuti apereke chidwi chake ku zomwe ankafuna kumuuza) ndipo kenako anamuuza kuti: “Ngati chiweruzo chikadakhazikika pa ubale umene ndili nawo ndi anthu, ndiye kuti ine ndikadatha kugamula mokomera amene ndamufuna.” Komabe, chiweruzo chagona pa lamulo la Allah Ta’ala (ndipo kwa munthu amene ali pa haq amalandira chiweruzo mokomera iye).

Check Also

Muvi Oyamba kulasa Mchisilamu

Olemekezeka Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu) adali m’gulu la ma Swahaabah omwe Mtumiki (swallallaahu ‘alayhi wasallam) adawatumiza …