Ubwino Owerenga Quraan Majeed

Muuni Padziko Lapansi ndi chuma cha tsiku lachiweluzo

Abu Zarr (radhwiyallahu anhu) anati: “Nthawi ina ndinamufunsa Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) kuti, ‘E, Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam), chonde ndipatseni malangizo.” Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) anayankha: “Igwiritsitse taqwa; Adati: “E, Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam), chonde ndipatseninso malangizo ena.” Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) adati: “Gwiritsitsani mwamphamvu kuwerenga kwa Qur’an Majiid, pakuti iyi ndi Nuur yanu (kuwala) padziko lapansi, ndi nkhokwe yanu patsiku lomaliza.’”[1]

Njira Yoyeretsera Mtima

Ibnu Umar (radhwiyallahu anhuma) akusimba kuti Rasulullah (swallallahua alaihi wasallam) adati: “Ndithu mitima iyi imachita dzimbiri monga momwe chitsulo chimachitira dzimbiri pamene madzi akumana nacho.” Ma Swahaabah (radhwiyallahu anhum) adafunsa kuti: “E, Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam), njira yoyeretsera mitima ndi yotani? Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) adayankha, “Kukumbukira imfa nthawi zambiri ndi kuwerenga Qur’an Majiid.[2]


[1] صحيح ابن حبان، الرقم: 361، وقد ذكره المنذري في الترغيب والترهيب، الرقم: 2193، بلفظة “عن”، إشارة إلى كونه صحيحا أو حسنا أو ما قاربهما عنده كما بين أصله في مقدمة كتابه 1/50

[2] شعب الإيمان للبيهقي، الرقم: 1859، وإسناده ضعيف كما في المغني عن حمل الأسفار في الأسفار صــ 323

Check Also

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 7

17. Nkosaloredwa kwa munthu yemwe ali ndi Janaabah kapena mkazi wa Haidh kuwerenga Quraan Majiid. …