Ubwino Owerenga Quraan Majeed

Muuni Padziko Lapansi ndi chuma cha tsiku lachiweluzo

Abu Zarr (radhwiyallahu anhu) anati: “Nthawi ina ndinamufunsa Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) kuti, ‘E, Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam), chonde ndipatseni malangizo.” Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) anayankha: “Igwiritsitse taqwa; Adati: “E, Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam), chonde ndipatseninso malangizo ena.” Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) adati: “Gwiritsitsani mwamphamvu kuwerenga kwa Qur’an Majiid, pakuti iyi ndi Nuur yanu (kuwala) padziko lapansi, ndi nkhokwe yanu patsiku lomaliza.’”[1]

Njira Yoyeretsera Mtima

Ibnu Umar (radhwiyallahu anhuma) akusimba kuti Rasulullah (swallallahua alaihi wasallam) adati: “Ndithu mitima iyi imachita dzimbiri monga momwe chitsulo chimachitira dzimbiri pamene madzi akumana nacho.” Ma Swahaabah (radhwiyallahu anhum) adafunsa kuti: “E, Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam), njira yoyeretsera mitima ndi yotani? Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) adayankha, “Kukumbukira imfa nthawi zambiri ndi kuwerenga Qur’an Majiid.[2]


[1] صحيح ابن حبان، الرقم: 361، وقد ذكره المنذري في الترغيب والترهيب، الرقم: 2193، بلفظة “عن”، إشارة إلى كونه صحيحا أو حسنا أو ما قاربهما عنده كما بين أصله في مقدمة كتابه 1/50

[2] شعب الإيمان للبيهقي، الرقم: 1859، وإسناده ضعيف كما في المغني عن حمل الأسفار في الأسفار صــ 323

Check Also

Zul Hijjah

Mwezi wa Zul Hijjah uli mgulu la miyezi inayi yopatulika ya kalendala ya Chisilamu. Miyezi …