Chikhulupiliro Chokhazikika cha Ali (radhwiyallahu ‘anhu) pa Lonjezo la Allah Ta’ala

Zanenedwa kuti nthawi ina munthu wopempha adadza kwa Ali (radhwiyallahu ‘anhu) napempha kanthu. Ali (radhwiyallaahu ‘anhu) adatembenukira kwa mmodzi mwa ana ake awiri, Hasan kapena Husain (radhwiyallahu ‘anhuma), nati kwa iye: “Pita kwa amayi ako ukawawuze kuti ine ndati: “Ndidasunga dirham zisanu ndi imodzi. Ndipatseni Dirhamu imodzi mwa zisanu ndi chimodzizo (kuti ndiipereke kwa opemphayu)”

Mwanayo anapita kwa mayi ake omwe ndi Faatimah (radhwiyallahu ‘anha), ndipo pambuyo pake anabwerera ndi uthenga otsatirawu. Adati kwa bambo ake: “Mayi anga anena kuti munawasungiza ndalama zokwana ma dirhamu asanu ndi imodzi ndi cholinga choti agule ufa. Atamva izi Ali (radhwiyallaahu ‘anhu) adati: “Imaan ya kapolo siingakhale yoona ndi yangwiro kufikira atadalira kwambiri zomwe zili m’manja mwa Allah Ta’ala poyerekeza ndi zimene kapolo ali nazo (mwachitsanzo, kapolo adzitsamira kwa Allah Ta’ala ndi malonjezo Ake kuti popereka sadaqah, adzadalitsidwa ndi masalitso pa ntchito yabwino ndi kuti asasiye chuma chake chifukwa choopa umphawi)”

Kenako Ali (radhwiyallaahu ‘anhu) adati kwa mwana wake: “Pita kwa mayi ako ndipo uwauze kuti andipatse madirhamu asanu ndi imodzi (kuti ndimupatse wopemphayu).” Choncho adapita kwa mayi ake ndikubweretsa ma dirham asanu ndi imodzi omwe Ali (radhwiyallaahu ‘anhu) adazipereka kwa opemphayo.

Posakhalitsa munthu wina adadutsa pafupi ndi Ali (radhwiyallahu ‘anhu) ndi ngamira yomwe ankagulitsa. Ali (radhwiyallaahu ‘anhu) adamufunsa: “Kodi mukugulitsa ngamira ndi ndalama zingati?” Munthuyo anayankha nati, Ine ndikugulitsa dirham zana limodzi mphambu makumi anayi. Kenako Ali (radhwiyallahu ‘anhu) adagula ngamira kwa iye. Atagula ngamirayo, Ali (radhiyallahu ‘anhu) adati: “Ngamira ili pano, ndipo tikulipirani pambuyo pake.” Choncho munthuyo anamanga ngamirayo n’kunyamuka.

Kenako munthu wina adadutsa, ndipo ataona ngamirayo, adafunsa: “Kodi ngamira iyi ndi ya ndani?” Ali (radhwiyallahu ‘anhu) adayankha: “Ndi yanga.” Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi mukugulitsa?” Pamene Ali (radhwiyallahu ‘anhu) adayankha kuti akugulitsa, munthuyo adafunsa: “Kodi mukugulitsa ndalama zingati?” Ali (radhwiyallahu ‘anhu) adayankha: “Ndikugulitsa dirham mazana awiri.” Munthuyo anakhutitsidwa ndi mtengowo ndipo analandira choperekacho ndipo anamaliza malondawo nati, “Ndagula kwa iwe. Kenako adapereka madirhamu mazana awiri aja kwa Ali (radhwiyallahu ‘anhu), anatenga ngamira yake nanyamuka.

Ali (radhwiyallaahu ‘anhu) adapita kwa munthu amene adamugulitsa ngamirayo ndikumulipira ndalama zokwana dirham zana limodzi mphambu makumi anayi zomwe adamkongolazo. Pambuyo pake, adabwerera kunyumba kwa mkazi wake olemekezeka Faatimah (radhwiyallahu ‘anha) ndi ma dirham makumi asanu ndi imodzi zomwe adapeza monga phindu (ndipo adampatsa).

Pamene Hazrat Faatimah (radhiyallahu ‘anha) adawona dirham makumi asanu ndi limodzi, adamufunsa: “Ndi chiyani ichi? Kodi ndalamazi zachokera kuti?” Hazrat Ali (radhiya allaahu ‘anhu) adayankha: “Izi ndi zomwe Allah Ta’ala watilonjeza kudzera m’mawu otsatirawa omwe adavumbulutsidwa pa lirime lodalitsika la Mtumiki (swalla allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam).

Kenako Hazrat Ali (radhiya allaahu ‘anhu) adawerenga ndime iyi ya Qur-aan Majeed:

مَن جَاءَ بِالْحَسَنَةِ فَلَهُ عَشْرُ أَمْثَالِهَا

Amene wabweretsa chabwino, adzalandira malipiro owirikiza kakhumi pa zomwe adazichita) (Surat Anoom v. 160).

M’mawu ena, Hazrat Ali (radhiya allahu ‘anhu) adamufotokozera Hazrat Faatimah (radhiyallahu ‘anhu) kuti pamene adapereka dirham zisanu ndi imodzi pa sadaqah, Allah Ta’ala adamdalitsa ndi malipiro ochuluka kuwirikiza kakhumi kuposa zomwe adaononga. anali ndi dirhamu makumi asanu ndi limodzi m’malo mwa dirhamu zisanu ndi imodzi zimene anapereka kwa wopemphapempha.

Check Also

Muvi Oyamba kulasa Mchisilamu

Olemekezeka Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu) adali m’gulu la ma Swahaabah omwe Mtumiki (swallallaahu ‘alayhi wasallam) adawatumiza …