Mabala owapeza munjira ya Allah Ta’ala

Hafs bin Khaalid (rahimahullah) akusimba kuti bambo wina wachikulire yemwe adafika kuchokera ku Mewsil adamuuza kuti ndidatsagana ndi Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) pa umodzi mwa maulendo ake. Pa nthawi ya ulendo. Pamene tinali malo otseguka, ouma, Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) ankafunika kusamba. Anatero kwa ine. “Ndibiseni (ndi nsalu kuti ndisambe).” Ndinamubisa motero, ndipo pomubisa, ndinaona mabala amene anali gawo la kuntunda kwa thupi lake chifukwa chobaidwa ndi malupanga. Ndidati kwa iye: “Ndikulumbirira Mulungu! Ndaona zipsera pathupi panu zomwe sindidaonepo wina aliyense.” Zubair (Radhiyallahu ‘anhu) adandifunsa kuti, “Kodi wazionadi?” Nditayankha kuti ndithu ndaona zipserazo, adati: “Ndikulumbirira kwa Allah kuti pali zipsera pathupi langa koma ndidazilandira pamodzi ndi Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) uku ndikumenya nkhondo munjira ya Allah Ta ‘ala yolimbana ndi ma kuffaar, (Tahzeeb-ul-Kamal 9/121)

Urwah (Rahimahullah) akufotokoza kuti, ” Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adalandira zipolopolo zitatu zazikulu pathupi lake kumenyedwa ndi malupanga. Imodzi inali pa phewa lake, ndipo inali yolowa kwambiri moti) ndimatha kulowetsa zala zanga m’menemo (dzenje lomwe linasiyidwa pambuyo pa chilondacho . Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu anapeza mabala awiri pa tsiku la Badr ndi limodzi pa tsiku la Tarmuk).

Check Also

Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu) aluza mano ake pa nkhondo ya Uhud

Pankhondo ya Uhud, Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adamenyedwa koopsa ndi adani ndipo mano awiri …