Mabala owapeza munjira ya Allah Ta’ala

Hafs bin Khaalid (rahimahullah) akusimba kuti bambo wina wachikulire yemwe adafika kuchokera ku Mewsil adamuuza kuti ndidatsagana ndi Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) pa umodzi mwa maulendo ake. Pa nthawi ya ulendo. Pamene tinali malo otseguka, ouma, Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) ankafunika kusamba. Anatero kwa ine. “Ndibiseni (ndi nsalu kuti ndisambe).” Ndinamubisa motero, ndipo pomubisa, ndinaona mabala amene anali gawo la kuntunda kwa thupi lake chifukwa chobaidwa ndi malupanga. Ndidati kwa iye: “Ndikulumbirira Mulungu! Ndaona zipsera pathupi panu zomwe sindidaonepo wina aliyense.” Zubair (Radhiyallahu ‘anhu) adandifunsa kuti, “Kodi wazionadi?” Nditayankha kuti ndithu ndaona zipserazo, adati: “Ndikulumbirira kwa Allah kuti pali zipsera pathupi langa koma ndidazilandira pamodzi ndi Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) uku ndikumenya nkhondo munjira ya Allah Ta ‘ala yolimbana ndi ma kuffaar, (Tahzeeb-ul-Kamal 9/121)

Urwah (Rahimahullah) akufotokoza kuti, ” Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adalandira zipolopolo zitatu zazikulu pathupi lake kumenyedwa ndi malupanga. Imodzi inali pa phewa lake, ndipo inali yolowa kwambiri moti) ndimatha kulowetsa zala zanga m’menemo (dzenje lomwe linasiyidwa pambuyo pa chilondacho . Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu anapeza mabala awiri pa tsiku la Badr ndi limodzi pa tsiku la Tarmuk).

Audio Player

Check Also

Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) Kusankha Abdur Rahmaan bin Auf (radhwiya Allahu ‘anhu) kukhala Mtsogoleri wa Asilikali pa nkhondo ya Dumatul Jandal.

M’chaka cha chisanu ndi chimodzi chioangireni Hijrah, m’mwezi wa Sha’baan, Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa …