Kusamalitsa pofotokoza Hadith yochokera kwa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam)

Abdullah bin Zubair (Radhwiya Allaahu ‘anhu) akuti nthawi ina adafunsa bambo ake (omwe ndi) Zubair radhwiyallahu ‘anhu kuti, “Bwanji simumafotokoza ma haadiith a Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam), monga momwe amachitira ma Swahaabah ena (Radhwiyallahu anhum)?”

Olemekezeka Zubair (Radhwiya Allahu ‘anhu) anayankha kuti, “Sindinachokepo kumbali ya Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) kuyambira pomwe ndidalowa Chisilamu (le. Ine nditha kukwanitsa kufotokoza mahaadiith ambiri kuchokera kwa iye). Koma kuti, nthawi ina, ndinamumva Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam). akutchulapo kanthu (chifukwa chomwe amachitira mantha kufalitsa ma haadiith, ndinamva Mtumiki (Swallallaahu ‘alaih wasallam) akunena kuti: “Amene wandinamizira mwadala (kupeka ma haadiith ndi kumanena kuti ndi mawu anga) akonzekere kuti nyumba yake ndi kugahena.”

Audio Player

Check Also

Mantha a Abdur Rahman bin Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) kuyankha mlandu ngakhale adawonongera chuma pa ntchito ya Dini.

Shu’bah (Rahimahullah) akuti: Nthawi ina Abdur Rahman bun Auf (Radhwiyallahu ‘anhu) ankasala kudya ndipo nthawi …