Kuwolowa manja kwa Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu)

Hishaam bun Urwah akufotokoza kuti ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) okwana asanu ndi awiri adamusankha Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) kuti adzatenge udindo ogawa chuma chawo akadzamwalira. Ena mwa ma Swahaabawa anali Olemekezeka Abdur Rahmaan bin ‘Auf (Radhwiyallahu ‘anhu), Olemekezeka Miqdaad (Radhwiyallahu anhu) ndi Olemekezeka Abdullah bin Mas’uud (Radhwiyallahu ‘anhu) atamwalira, Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adatenga udindo ogawa chuma chotsala komanso adasamalira chuma cha ana awo ndiponso ankathandiza anawo pogwiritsa ntchito chuma chake. (Usul Ghasbah 2/211).

Check Also

Kudziwa Kwambiri Dini kwa Muaaz bin Jabal (radhwiyallahu ‘anhu)

Abu Muslim Khowlaani (rahimahullah) akufotokoza kuti: “Ndinalowa mumzikiti wa Hims ndipo ndinaona gulu la anthu. …