Ntendere Waukulu Wa Allah Pa Akapolo Ndi Kukhala Makolo

Ena mwa madaritso aukuluakulu a Mulungu pa munthu, ndi mdaritso okhala ndi makolo. Mwayi okhalandi makolo ndi mdaritso ofunika kwambiri ndipo ulibe mlowa m’malo komanso umaperekedwa kwa munthu kamodzi kokha m’moyo wake.

Monga momwe chisomo cha kukhala ndi moyo chimaperekedwa kamodzi kokha kwa munthu, ndipo chikatha sichidzabwereranso, momwemonso chisomo chokhala ndi makolo, chikachotsedwa, sichingabwezeretsedwenso.

Mtendere ulionse omwe munthu ali nawo uli ndi maufulu ena omwe ali nawo. Pamene Mwayi okhala ndi makolo uli mgulu la zabwino kwambiri, ndiye kuti maufulu omwe ali nawo ndi ena mwa maufulu ofunikira kwambiri mu chisilamu.

Quraan yolemekezeka ndi Mahadith ndi zodzadza ndi malamulo ndi malangizo okhudza kufunikira kwakukulu kokwaniritsa maufulu a makolo ndikuwachitira zabwino zochuluka.

Mu Quraan Majiid Allah Taala wanena kuti:

وَقَضَىٰ رَبُّكَ أَلَّا تَعْبُدُوا إِلَّا إِيَّاهُ وَبِالْوَالِدَيْنِ إِحْسَانًا ۚ إِمَّا يَبْلُغَنَّ عِندَكَ الْكِبَرَ أَحَدُهُمَا أَوْ كِلَاهُمَا فَلَا تَقُل لَّهُمَا أُفٍّ وَلَا تَنْهَرْهُمَا وَقُل لَّهُمَا قَوْلًا كَرِيمًا ‎﴿٢٣﴾‏

Mbuye wako walamula kuti musapembedze aliyense koma lye, ndi kuti muchitire zabwino makolo anu. Ngati mmodzi wa iwo kapena onse awiri akalamba, Usanene kwa iwo: “Uff (mawu achipongwe kapena mawu aukali kapena mkwiyo)”, Ndipo osawakalipira, ndipo uwalankhule ndi mawu aulemu. “

M’ Hadith zidanenedwa kuti Chisangalalo cha Allah Taala chili m’chisangalalo cha makolo, ndipo mkwiyo wa Allah Taala uli m’kuipidwa kwa makolo”

Makolo Anu ndi Jannah Yanu kapena Jahannum

Tsiku lina Swahaabi wina adafunsa kwa Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) za ufulu wa makolo. Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Iwo (makolo) ndi Jannah yako kapena Jahannam yako.”

M’mawu ena, ngati wina ali wachifundo ndi wachikondi kwa makolo ake ndi kuwamvera mu zinthu zonse zoloredwa, adzadalitsidwa ndi Jannah. Koma ngati wawanyoza ndi kuwachitira nkhanza komanso mwano, ndiye kuti kuwazunza kwake ndi chifukwa choti adzalowe ku moto wa Jahannam.

Check Also

Swalaah Ndi Kiyi Yaku Jannah

Chisilam ndi njira yokhayo imene imamutsogolera munthu ku chikondi cha Allah Ta’ala komanso chimamutsogolera Jannah. …