Kulemekeza kwa Saiid bin Zaid (Radhwiyallahu ‘anhu) kumulemekeza Uthmaan (Radhwiyallahu ‘anhu)

Zanenedwa kuti nthawi ina munthu wina adadza kwa olemekezeka Saiid bin Zaid (Radhwiya-Allahu anhu) nati: “Ndili ndi chikondi chachikulu pa Ali (Radhwiya-Allahu ‘anhu) mu mtima mwanga moti sindikonda china chilichonse monga momwe ndimamukondera.” Saiid bin Zaid (Radhwiya-Allahu ‘anhu) adamuyamikira iye chifukwa cha chikondi ndi ulemu wake kwa Ali (Radhwiyallahu ‘anhu) nati: “Izi nzabwino kwambiri! Muli ndi chikondi mu mtima mwanu pa munthu yemwe ali ochokera ku Jannah (chifukwa Ali (Radhwiya-Allahu anhu) adapatsidwa nkhani yabwino ya Jannah adakali pa dziko pompano kudzera kwa Mtumiki wa Allah SwallaAllaahualayhiwasallam).

Munthuyu pambuyo pake adati: “Ine ndili ndi chidani mu mtima mwanga cha Uthmaan (Radhwiya-Allahu ‘anhu) kotero kuti sindidana ndi china chilichonse ngati momwe ndimamudera iye.” Said bun Zaid (Radhwiya-Allaahu ‘anhu) adamuuza kuti: “Wachita zoipa ndi zolakwa kumuda Uthmaan (Radhwiya-Allahu ‘anhu) dziwa bwino kuti mumtima mwako uli ndi chidani cha munthu amene ali waku Jannah (popeza Uthmaan (Radhwiya-Allahu anhu) adaizidwa zokalowa ku Jannah adakali pa dziko lapansi pompano).

Sa’iid bin Zaid (Radhwiya-Allahu ‘anhu) anasimba Hadith ya Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) nati: “Nthawi ina Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adakwera phiri la Hiraa pamodzi ndi Abu Bakr, Umar, Uthmaan,Aliyy,Talha ndi Zubair. Radhwiya-Allah ‘anhum) Phiri lidayamba kunjenjemera ndi kugwedezeka (chifukwa cha chisangalalo powona kuti anthu akuluakuluwa aima pamenepo).

“Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adaliyankhula phirilo nati: “Khanzikika, iwe Hiraa, popeza pa iwe pali Nabiy, Siddiiq ndi shahiid.”

Check Also

Olemekezeka Abu Zar (Radhwiyallahu ‘anhu) Kulemekeza Alendo

‘Isa bin ‘Umailah (Rahimahullah) akufotokoza za munthu wina amene adawona khalidwe la Abu Zar (Radhwiyallahu …