Ma Ubwino Okhudza Kupereka Salaam

Ubwino Oyambilira kupanga Salaam

Olemekezeka Abdullah bun Masuud (Allah asangalale naye) akusimba kuti Rasulullah (madalitso ndi mtendere zikhale pa iye) adati: “Amene amayambilira kupereka Salaam ndi osadzitukumura.”[1]

Njira Yokhanzikitsira Chikondi

Olemekezeka Abu Hurairah (Allah asangalare naye) akusimba kuti Rasulullah (madalitso ndi mtendere zipite kwa iye) adati: “Simudzalowa ku Paradiso pokhapokha mutakhulupilira, ndipo simungakhale okhulupilira kwenikweni kufikira mutakondana pakati panu?[2]

Ntchito Yapamwamba Mchisilamu

Olemekezeka Abdullah bin Amr (Allah asangalale naye) akunena kuti munthu wina adamufunsa Rasulullah (madaritso ndi mtendere zipite kwa iye) kuti: “Ndi chikharidwe chanji ndi nchitidwe wa Chisilamu zomwe zili zoyamikirika ndi zabwino?” Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale pa iye) adati: “Kudyetsa zolengedwa ndi kupereka moni wachisilanu (kupereka salaam) kwa anthu, kaya mukuwadziwa kapena ayi.”[3]

Imabweretsa Madalitso Mnyumba

Olemekezeka Anas (Radhwiyallahu anhu) adati: Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) nthawi ina adandiuza: “E, iwe mwana wanga okondedwa! Ukalowa m’nyumba mwako, upereke salamu ku banja lako. Iyi ndi njira yopezera madaritso kwa iwe ndi banja lako.[4]


[1] شعب الإيمان للبيهقي، الرقم: 8407، وقال المناوي في فيض القدير، الرقم: 3191، وفيه أبو الأحوص قال ابن معين: ليس بشيء وأورده الذهبي في الضعفاء

[2] صحيح مسلم، الرقم: 54

[3] صحيح البخاري ، الرقم: 12

[4] سنن الترمذي، الرقم: 2698، وقال: هذا حديث حسن غريب

Check Also

Ma Sunnah Komanso Miyambo Ya Jumu’ah 1

1. Werengani Surah Dukhaan Lachinayi usiku. Olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallah anhu) akunena kuti Rasulullah (swallallahu …