وَالنَّازِعَاتِ غَرْقًا ﴿١﴾ وَالنَّاشِطَاتِ نَشْطًا ﴿٢﴾ وَالسَّابِحَاتِ سَبْحًا ﴿٣﴾ فَالسَّابِقَاتِ سَبْقًا ﴿٤﴾ فَالْمُدَبِّرَاتِ أَمْرًا ﴿٥﴾
Ndikulumbirira (angelo) amene amachotsa (mizimu ya osakhulupirira) mwaukali, ndi (angelo) amene amachotsa (miyoyo ya okhulupirira) moleza, ndi (Angelo) amene amasambira nayo mizimuyo (m’mlengalenga), ndi (Angelo) amene amapikisana (kukwaniritsa malamulo a Allah Ta’ala).
Monga ziliri kuti Sura Nabai idavumbulutsidwa kuti idzakhazikitse chikhulupiriro cha tsiku la Qiyaamah, momwemonso surayi idavumbulutsidwa kuti idzakambe nkhani zina za Qiyaamah.
M’surayi Allah Ta’ala wayamba ndi kulumbilira machitidwe ena a angero ndi cholinga chofuna kutsimikizira anthu kuti tsiku la Qiyaamah ndi lotsimikizika. Choncho, m’ndime yachisanu ndi chimodzi, atalumbirira machitidwe osiyanasiyana a angero, Allah Ta’ala akuyankhula za tsiku la Qiyaamah.
Popeza ndi zachidziwikire kuti Allah Ta’ala walumbirira angero amene amachotsa miyoyo ya anthu ndi kumudziwitsa munthu kuti Qiyaamah ya munthu aliyense imayamba iye akamwalira. Choncho, kwanenedwa momveka bwino kuti: “Amene wamwalira, Qiyaamah yake yayamba.
Ngakhale Qiyaamah yeniyeni ya zolengedwa zonse idzachitikale kumapeto kwa dziko lapansi, komabe popeza moyo otsatira wa munthu umayambika pa akamwalira, imfa ya munthu aliyense imatengedwa ngati Qiyaamah yake.
Tikaonetsetsa, m’ma aya awa Allah Ta’ala akukamba machitidwe asanu a angero. Makhalidwe asanuwa ndi awa:
Khalidwe loyamba
وَالنَّازِعَاتِ غَرْقًا ﴿١﴾
Ndikulumbirira (angelo) amene amatulutsa (mizimu ya osakhulupirira) mwampamvu
M’ndime iyi, Allah Ta’la akufotokoza za angero a imfa amene amachotsa mizimu ya makafiri mwaukali ndi mwankhanza, osawachitira chifundo. Angero amene amachotsa mizimu ya makafiri ndi angero achilango, ndipo mawu oti “mwankhanza” mu Aayah akutanthauza kuwawa kwauzimu osati kuwawa kwakuthupi. Chifukwa chake, anthu omwe ali pafupi ndi munthu wakufayo sangazindikire ululu wa munthu wakufayo monga momwe ululu umamvekera ndi moyo wa munthu wakufayo, osati thupi lake.
Nthawi zina zimaoneka ngati kuti mzimu wa kaafir umachoka m’thupi lake mosavuta, koma zoona zake n’zakuti sizili choncho, monga momwe zilili m’ndime iyi Allah Ta’ala akutiuza za ululu waukulu ndi masautso amene mzimu wa kafiri umakumana nawo yomwalira.
Ubwino Wachiwiri wa Angelo
وَالنَّاشِطَاتِ نَشْطًا ﴿٢﴾
Ndikulumbilira (angelo) amene amatulutsa (mizimu ya okhulupirira) Modekha
M’ndime iyi, Allah Ta’la akufotokoza za angero amene amatulutsa mizimu ya okhulupirira modekha ndi moleza. Angelo amene amachotsa mizimu ya okhulupirira amatchedwa angelo achifundo. Iwo amalamulidwa ndi Allah Ta’ala kuti achite ndi Asilamu mwaubwino ndi wodekha.
Liwu loti “النٰشطٰت” likuchokera ku liwu loti “نشط” lomwe kwenikweni limatanthauza “kumasula mfundo”. Izi zikutanthawuza “kumasula mfundo ya chinthu chomwe chili ndi madzi kapena mpweya, kuti madzi kapena mpweya utuluke mosavuta”. Ili ndi fanizo lotulutsa mizimu ya okhulupirira mofatsa, mosiyana ndi mizimu ya osakhulupirira yomwe imatulutsidwa mwankhanza. Zili ngati kuti mzimu wa okhulupirira unali omangidwa m’thupi lake, ndipo thupi linafunika kutsegulidwa kuti mzimuwo utulutsidwe.
Pankhani imeneyinso, liwu lakuti نَشۡطًا lomwe limamasulira kuti “mosalala” kapena “modekha” limatanthauza kufewa kwauzimu kapena kufatsa, osati ku zochitika zakuthupi. Nthaŵi zina, okhulupirira opembedza amaonedwa akukumana ndi vuto linalake panthaŵi ya imfa yake, komabe, zimenezi sizingatanthauze kwenikweni kuti akukumana ndi vuto linalake lauzimu kapena chilango, ngakhale kuti kuthupi, zingamaoneke choncho kwa awo amene ali nawo pafupi.
Ukatulutsidwa mzimu wa kafiri, chithunzi chonse cha chilango cha barzakh (moyo wa pambuyo pa imfa) chimadza pamaso pake. Imakahala nthawi yochititsa mantha ndi kuopsya kwambiri, ndipo munthu amene wamwalirayo amathedwa nzeru ndi zimenezo. Popeza mzimu, ukuchita mantha kwambiri ndi zochitika zachilango, umayamba kusuntha thupi lonse, kuyesa kubisala kapena kuthawa chilango. Komabe, angero a imfa amauchotsa mzimu wake mwamphamvu, kuutulutsa mwamphamvu ndi mwaukali m’thupi lake, monga momwe mzinga umazulidwira mwamphamvu muubweya onyowa (monga momwe tafotokozera mu Hadith ya olemekezeka Baraa bin Aazib (radhiyallahu ‘anhu) yolembedwa mu Musnad-e-Ahmed).
Komano, mzimu wa Msilamu ukachotsedwa, malipiro aakulu ndi madalitso a tsiku Lomaliza amene wamusungira amaperekedwa kwa iye ndipo amapatsidwa nkhani yabwino ndi yosangalatsa, choncho mzimu wake umachoka m’thupi momasuka ndi chisangalalo chachikulu.
Khalidwe Lachitatu la Angelo
وَالسَّابِحَاتِ سَبْحًا ﴿٣﴾
Ndi amene amasambira (nayo mizimuyo) mu mlengalenga (popita nayo ku malo ake oyembekezera.
Mu ayah iyi, Allah Ta‘ala akulankhula za khalidwe lachitatu la angelo. Angelo omwe akutchulidwa mu ndime iyi ndi angelo a imfa omwe, atatulutsa mzimu wa munthu, amayendayenda mofulumira mu mlengalenga atanyamula mzimu kupita kumwamba kuti akaupereke kwa Allah Ta‘ala.
Mawu akuti “سٰبحٰت” amachokera ku mawu akuti “سبح” omwe amatanthauza “kusambira” kapena “kuyandama”, koma m’nkhaniyi, ponena za angelo, tanthauzo la mawuwa ndi “kuyenda mofulumira m’mwamba”.
Nkhalidwe Lachinayi La Angelo
فَالسّٰبِقٰتِ سَبۡقًا ۙ﴿۴﴾
Ndipo ndi (angelo) omwe amathamanga limodzi pa mpikisano (kuti akwaniritse lamulo la Allah Ta‘ala)
Mu ayah iyi, Allah Ta‘ala akulankhula za momwe angelo a imfa amathamangitsirana kupikisana wina ndi mnzake kuti akwaniritse lamulo la Allah Ta‘ala.
Malinga ndi lamulo la Allah Ta‘ala, angelo amatenga miyoyo ya opembedza kupita nayo kumalo awo abwino, ndi mizimu ya oipa kupita nayo kumalo awo oipa. Pambuyo pofunsidwa m’manda, mzimu wa okhulupirira umasamutsidwira ku malo a Illiyyeen komwe udzasangalala ndi madalitso a Paradaiso, ndipo mzimu wa osakhulupirira umasamutsidwira ku Sijjeen komwe umakazunzika ku Gehena. (Al-Rooh tsamba 134)
Khalidwe Lachisanu La Angelo
فَالۡمُدَبِّرٰتِ اَمۡرًا ۘ﴿۵﴾
Ndi iwo (angelo) omwe amayendetsa malamulo (omwe amapatsidwa ndi Allah Ta‘ala pankhani okhudza mizimu ya akufa)
Mu ayah iyi, Allah Ta‘ala akunena za angelo omwe amayendetsa nkhani za omwe amwalira ndikukwaniritsa zomwe Allah Ta‘ala walamula popereka mphotho kwa mizimu yolungama ndikulanga mizimu yoipa.
Mwanjira ina, ntchito yomaliza ya angelo awa a imfa idzakhala kutonthoza mizimu yolungama ndikubweretsa ululu kwa mizimu yoipa. Mizimu ikafika pamalo awo abwino kapena oipa, angelo omwe alamulidwa kupereka mphotho ndi kutonthoza mizimu yabwino amasonkhanitsa njira zowalipirira ndi kuwatonthoza, ndipo angelo omwe alamulidwa kulanga ndi kupereka mavuto ku mizimu yoipa amakonza njira zowazunzira ndi kuwalanga.
Mphotho ndi Chilango Za M’manda
Pakadali pano Surah ikutsimikizira kuti nthawi ya imfa, angelo adzafika ndikutulutsa mzimu wa munthu. Kenako adzautenga kupita kumwamba ndikuunyamula mwachangu kupita nawo malo ake oyenera. Mzimu wabwino udzasamutsidwa kupita nawo kumalo a ntendere, ndipo mzimu oipa udzasamutsidwa kupita nawo kumalo a mavuto. Kumeneko angelo adzakonza njira zopezera mphotho ndi chitonthozo, kapena chilango ndi ululu kwa mitundu iwiri ya mizimu motsatana.
Mavesiwa akusonyeza kuti mphotho ndi chilango zidzachitika m’manda (ngati m’moyo wa barzakh munthu atachoka padziko lapansi). Pambuyo pake, Tsiku la Qiyaamah likadzafika, chigamulo chidzaperekedwa kuti munthu akalowe ku Jannah, kapena ku Gahena.
Kukamba za momwe mzimu wa munthu olungama kapena ochimwa umachotsedwera ndi angelo a imfa, pali Hadith yayitali ya Olemekezeka Baraa bin Aazib (radhwiyallahu ‘anhu) yomwe yalembedwa mu Musnad-e-Ahmad. Hadith iyi ndi iyi. Baraa bin Aazib (radhwiyallahu ‘anhu) akunena kuti:
Nthawi ina, tinatuluka ndi Rasulullah (Swallallahu ‘alaihi wasallam) kuti tikaswalire nawo maliro a munthu wachi Ansaar. Titafika kumanda, tinapeza kuti manda anali asanakumbidwe. Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) anakhala pansi, ndipo tinakhala momuzungulira, modekha ngati kuti panali mbalame pamitu pathu.
Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) anali ndi ndodo m’manja mwake yomwe ankakanda nayo pansi (popeza ankaganiza kwambiri). Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) kenako ananyamura mutu wake nati kawiri ngati si katatu, “Pemphani chitetezo cha Allah Ta‘ala ku chilango cha manda!”
Pambuyo pake, Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) anati, “Ndithudi, okhulupirira akatsala pang’ono kuchoka padziko lapansi kupita ku Moyo omaliza, angelo amatsika kwa iye kuchokera kumwamba. Nkhope zawo zoyera zimawala kwambiri kotero kuti zimakhala ngati kuti nkhope zawo zonse ndi dzuwa. Amabwera ndi sanda yochokera ku siliki ya ku Jannah, komanso mafuta onunkhira ochokera ku mafuta onunkhira a ku Jannah. Amakhala pafupi naye, komwe angayang’ane.
“Pambuyo pake, mngelo wa imfa amabwera kwa iye ndikukhala pambali pake. Mngeloyu amamulankhula nati, ‘Iwe mzimu oyera! Tuluka, kupita ku chikhululuko cha Allah ndi chimwemwe Chake!’ Mzimuwo umatuluka moyenda bwino, monga momwe dontho la madzi limatulukira m’chikopa cha madzi.
“Angelo amapitirira kukwera nawo mzimu kupita kumwamba. Angelo alionse omwe angakumane nawo amawapempha chilorezo choti adutse. khomo la ntambo umenewo limatsegulidwa kuti adutse, kenako angelo a ntambo otsatira amalandira mzimu ndikuuperekeza ku ntambo otsatira, ndipo izi zimapitirira kwina konseko, mpaka mzimuwo utafika ku ntambo omalizira.
“Kenako Allah Ta’ala amalamula angelo kuti, ‘Lembani m’buku la kapolo wanga kuti malo ake okhalamo akhazikitsidwa kukhala ku Illiyiin, kenako mumubwezeretse padziko lapansi (kumanda ake kuti akafunsidwe), popeza ndidawalenga kuchokera ku dothi ndipo ndidzawabwezeretsa ku dothi, ndi kudzawaukitsanso kuchokera ku dothi.’
“Kenako mzimu umabwezeretsedwa ku thupi m’manda ndipo angelo awiri (Munkar ndi Nakiir) amamubwelera. Amamukhanzika ndikumufunsa kuti, ‘Kodi Mbuye wako ndindani?’ Amayankha kuti, ‘Mbuye wanga ndi Allah.’ Pambuyo pake amamufunsa kuti, ‘Kodi chipembedzo chako ndi chiyani?’ Amayankha kuti, ‘Chipembedzo changa ndi Chisilamu.’ Pomaliza, amamufunsa kuti, ‘Kodi munthu uyu amene adatumizidwa kwa inu ndi ndani?’ Amayankha kuti, ‘Ndi Mtumiki wa Allah (Swallallahu ‘alaihi wasallam).’ Angelo amamufunsa kuti, ‘Wadziwa bwanji zimenezi?’ Iye amayankha kuti ndidawerenga bukhu la Allah ndipo ndidakhulupilira mwa iye ndi kumukhulupilira kuti iye ndi Mtumiki weniweni wa Allah Ta’ala.’
“Kenako kumamveka kufuula kuchokera kumwamba kuti, ‘Ndithudi, kapolo wanga wanena zoona (ndipo wayankha mafunso molondola), choncho mutambasulireni kapeti m’makapeti a ku Jannah, mumuveke zovala za ku Jannah, ndipo mumutsegulire (kutambasura manda ake) khomo la ku Jannah!’ Kotero, mpweya ndi fungo la ku Jannah zimamufikira, ndipo manda ake amatambasuridwa mpaka kothera kuona maso ake.
“Kenako munthu amabwera kwa iye ndi nkhope yokongola, zovala zokongola komanso fungo lokoma. Munthuyo amamuuza kuti, ‘Sangalala ndi zomwe zingakusangalatse! Tsiku ili ndi limene udalonjezedwa (kukumana nalo pamene unali padziko lapansi)!’ Omwalirayo amamufunsa kuti, ‘Ndiwe ndani? Nkhope yako ndi ya munthu amene amabweretsa zabwino!’ Munthuyo amayankha kuti, ‘Ndine ntchito zako zabwino zomwe unkachita.’
“Omwalirayo amati, ‘E, Mbuye wanga! Yambani Qiyaamah! E, Mbuye wanga! Yambani Qiyaamah, kuti ndibwerere ku banja langa ndi chuma changa (ku Jannah)!'”
Kenako Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) adati, “Ndithudi, munthu osakhulupirira akatsala pang’ono kuchoka padziko lapansi ndikupita ku Moyo osatha, angelo amabwera kwa iye kuchokera kumwamba. Angelo awa ali ndi nkhope zakuda, ndipo amakhala ndi matumba a nsalu zopyapyala. Amakhala pafupi naye, mbali imene iyeyo angathe kumawaona.
“Pambuyo pake, mngelo wa imfa amabwera kwa iye ndikukhala pambali pake. Mngeloyu amamulankhula nati, ‘Iwe mzimu onyansa, oipa! Tuluka mwa mkwiyo wa Allah!’ Mzimuwo umayendayenda m’thupi lake (kuyesera kumuthawa mngelo wa imfa kuti asaugwire). Pambuyo pake, mngelo wa imfayu amatulutsa mzimuwo mwamphamvu, monga momwe chikopa chimachotsedwera mwamphamvu kuthipi lake. Mngelo wa imfa amaugwira mzimuwo.
“Mngelo wa imfa akagwira mzimu, angelo ena omwe ali naye samausiya m’manja mwake ngakhale pang’ono mpaka atautenga n’kuuika m’thumba lopanda kanthu. Fungo loipa limatuluka mu mzimu umenewu, ngati fungo loipa kwambiri la mtembo lomwe lingapezeke padziko lapansi.
“Kenako angelo amakwera nawo kumwamba, ndipo gulu lililonse la angelo omwe amadutsana nawo, angelo amenewo amawafunsa kuti, ‘Kodi mzimu oipawu ndi wa ndani?’ Amayankha, ‘Ndi wakutiwakuti, mwana wa wakutiwakuti,’ akumutchura ndi mayina oipa kwambiri omwe anthu ankamuitanira padziko lapansi.
“Kenako angelo amapitiriza kukwera nawo mzimuwo mpaka kukafika kuntambo oyamba. Akafika kjntambo oyamba, amapempha chilolezo cholowa, koma khomo la kumwamba silimatsegulidwa kwa iwo.”
Atatchula izi, Rasulullah (sallallahu ‘alaihi wasallam) adawerenga Ayah yotsatira ya Qur’aan Majiid:
لَا تُفَتَّحُ لَہُمۡ اَبۡوَابُ السَّمَآءِ وَلَا یَدۡخُلُوۡنَ الۡجَنَّۃَ حَتّٰی یَلِجَ الجَمَلُ فِيْ سَمِّ الۡخِیَاطِ
makomo akumwamba sadzatsekulidwa kwa iwo (osakhulupirira), ndipo sakalowa ku Paradiso mpaka ngamira italowa pa diso la singano (i.e. Sadzatha kukalowa ku Jannah). (Surah A’raaf v. 40)
Kenako Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) anapitiriza nati, “Allah Ta‘ala adzanena, ‘Lembani m’buku lake kuti malo ake okhalamo alamulidwa kukhala ku Sijjiin, pansi pa nthaka (Jahannum).’ Pambuyo pake, mzimu wake umaponyedwa mwamphamvu.”
Kenako Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) adawerenga ndime iyi ya Qur-aan:
وَ مَنۡ یُّشۡرِکۡ بِاللهِ فَکَاَنَّمَا خَرَّ مِنَ السَّمَآءِ فَتَخۡطَفُہُ الطَّیۡرُ اَوۡ تَهْوِيْ الرِّیۡحُ فِیۡ مَکَانٍ سَحِیۡقٍ ﴿۳۱﴾
Amene amamphatikiza Allah ndi milungu ina, ali ngati wagwa kuchokera kumwamba, ndipo Mbalame zikumuwakha, kapena mphepo kumponya Kumalo akutali. (Surah Haj v. 31)
Mtumiki (sallallahu ‘alaihi wasallam) anapitiriza nati, “Kenako mzimu wake udzabwerera m’thupi lake, ndipo angelo awiri (Munkar ndi Nakeer) adzabwera kwa iye. Adzamukhanzika pansi namufunsa kuti, ‘Kodi Mbuye wako ndani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Aah! Aah! Sindikudziwa!’ Kenako adzamufunsa kuti, ‘Kodi chipembedzo chako n’chiyani?’ Iye adzati, ‘Aah! Aah! Sindikudziwa!’ Pomaliza, angelo adzamufunsa kuti, ‘Kodi munthu ameneyu anatumizidwa kwa iwe ndi ndani?’ Adzayankhanso kuti, ‘Aah! Aah! Sindikudziwa!’
“Pamenepa, mawu adzafuula kuchokera kumwamba nati, ‘Walephera, choncho mutambasulireni kapeti ya moto, ndipo mutsegulireni chitseko cha moto wa Jahannam.’ Kotero, kutentha kwaukali kwa moto wa Jahannum kudzamufikira, ndipo manda ake adzachepetsedwa ndi kuthina, mpaka (adzakhala akufinyidwa mpaka kufika pamlingo wakuti) nthiti zake kuchokera mbali imodzi zidzalumikizana ndi nthiti za mbali inayo.
“Munthu adzabwera kwa iye amene maonekedwe ake adzakhala owopsa, amene zovala zake zidzakhala zoopsa ndipo fungo lake lidzakhala loipa kwambiri. Munthuyo adzamuuza kuti, ‘Sangalala ndi zomwe zidzakupangitse kudzimvera chisoni! Tsiku ili ndi limene unalonjezedwa (kukumana nalo pamene udali padziko lapansi)!’ Omwalirayo adzamufunsa munthuyo kuti, ‘Ndiwe ndani, chifukwa nkhope yako ndi ya munthu amene amabweretsa zoipa?’ Iye adzayankha kuti, ‘Ndine ntchito zako zoipa.’
“Omwalirayo adzati, ‘E, Ambuye wanga! Musalore Qiyaamah ibwere!’”
M’nkhani ina, zafotokozedwa kuti mzimu wa okhulupirira odzipereka ukakwera kupita kumwamba, ndiye kuti mngelo aliyense pakati pa mitambo ndi dziko lapansi, ndi mngelo aliyense kumtambo ulionse, amamuchitira dua. Zitseko zakumwamba zimatsegulidwa kwa iye, ndipo angelo pakhomo lililonse amapempha kwa Allah Ta‘ala kuti mzimu odzipereka uwu ukwere kudzera pakhomo lake.
Mzimu wa osakhulupirira ukatulutsidwa, umatuluka ndi mitsempha (kutanthauza kuti udzatuluka m’mitsempha yonse ya thupi lake). Mngelo aliyense pakati pa mitambo ndi dziko lapansi, ndi mngelo aliyense kumtambo ulionse, amamutemberera. Zitseko zakumwamba zimatsekedwa, ndipo angelo a khomo lililonse amapempha kwa Allah Ta‘ala kuti mzimu wake usakwere kudzera khomo lake.
يَوْمَ تَرْجُفُ الرَّاجِفَةُ ﴿٦﴾ تَتْبَعُهَا الرَّادِفَةُ ﴿٧﴾ قُلُوبٌ يَوْمَئِذٍ وَاجِفَةٌ ﴿٨﴾ أَبْصَارُهَا خَاشِعَةٌ ﴿٩﴾ يَقُولُونَ أَإِنَّا لَمَرْدُودُونَ فِي الْحَافِرَةِ ﴿١٠﴾ أَإِذَا كُنَّا عِظَامًا نَّخِرَةً ﴿١١﴾ قَالُوا تِلْكَ إِذًا كَرَّةٌ خَاسِرَةٌ ﴿١٢﴾ فَإِنَّمَا هِيَ زَجْرَةٌ وَاحِدَةٌ ﴿١٣﴾ فَإِذَا هُم بِالسَّاهِرَةِ ﴿١٤﴾
(Mudzaukitsidwa) tsiku lomwe kugwedezeka Kudzachititsa Chilichonse kugwedezeka, (ndi) chinthu china chogwedeza pambuyo Pachimenecho (ndiko Kuwomba koyamba kwa lipenga). kuchitika, ndipo kudzatsatiridwa ndi kuwomba kwachiwiri kwa lipenga pambuyo pa zaka makumi anayi). Mitima (ya anthu), tsiku limenelo, idzanjenjemera, (ndipo) maso awo adzadzolika pansi (kuchita manyazi). Iwo (osakhulupirira) akumati, “Kodi tidzabwereradi mwakale (tidzaukitsidwa)? Bwanji! Ngakhale titakhala mafupa ovunda?” Iwo amati, “Pamenepo, kudzakhala kubwerera kotayika.” Kenako (kuwomba kwachiwiri kwa lipenga) kudzakhala kulira kwamphamvu kamodzi kokha (kwa phokoso), ndipo mwadzidzidzi, adzadzutsidwa (ndi kubweretsedwa ku chigwa cha Hashr kuti akaweruzidwe).
يَوْمَ تَرْجُفُ الرَّاجِفَةُ ﴿٦﴾ تَتْبَعُهَا الرَّادِفَةُ ﴿٧﴾
(Mudzaukitsidwa) tsiku limene kugwedezeka kudzapangitsa chilichonse kugwedezeka mwamphamvu, (ndi) kugwedezeka kwina pambuyo pake.
Mu vesi loyambayi, Allah Ta‘ala akukamba za kuwomba koyamba kwa lipenga komwe kudzachitike pa Tsiku la Qiyaamah, ndipo mu vesi lachiwiri, Allah Ta‘ala akunena za kuwomba kwachiwiri kwa lipenga komwe kudzachitike zaka makumi anayi pambuyo pa lipenga loyamba.
Cholinga cha kuwomba koyamba kwa lipenga chidzakhala kupangitsa cholengedwa chilichonse chamoyo kufa, ndikuthetsa dziko lonse lapansi. Cholinga cha kuwomba kwachiwiri kwa lipenga chidzakhala kuukitsanso chilengedwe.
Mu Charabu, mawu akuti “راجفة” amachokera ku liwu loyambira “رجف” lomwe limatanthauza “kugwedeza china chake”.
Ndi chifukwa chake, mu vesi yoyamba, kudzera mu liwu loti “راجفة”, Allah Ta‘ala akusonyeza kugwedezeka komwe kudzachitike pa Tsiku la Qiyaamah. kugwedezekaku kukutanthauza kuwomba koyamba kwa lipenga, komwe chilichonse padziko lapansi chidzayamba kugwedezeka mwamphamvu, zomwe zidzapangitse kuti chilichonse chionongeke, chiwonongeke ndi kutheratu.
Mu Charabu, mawu akuti “رادفة” amachokera ku liwu loyambira “ردف” lomwe limatanthauza “kutsatira kapena kubwera pambuyo pa china chake”.
Ndi chifukwa chake, mu vesi yachiwiri, kudzera mu liwu loti “رادفة”, Allah Ta‘ala akusonyeza kuwomba kwachiwiri kwa lipenga komwe kudzachitike zaka makumi anayi pambuyo pa kuwomba koyamba kwa lipenga.
Kutchuridwa mofanana kwa kuwomba koyamba ndi kwachiwiri kwa lipenga kwalembedwa mu vesi yotsatira ya Qur’aan Majeed
وَنُفِخَ فِي الصُّورِ فَصَعِقَ مَن فِي السَّمَاوَاتِ وَمَن فِي الْأَرْضِ إِلَّا مَن شَاءَ اللَّهُ ۖ ثُمَّ نُفِخَ فِيهِ أُخْرَىٰ فَإِذَا هُمْ قِيَامٌ يَنظُرُونَ ﴿٦٨﴾
Ndipo lipenga lidzaimbidwa (koyamba), ndipo adzakomoka onse akumwamba ndi Padziko lapansi (ndikumwalira), kupatura amene Allah wawafuna (monga Jannah, Jahannum ndi okhala kumeneko). Pambuyo pake, lidzaimbidwanso, ndipo mwadzidzidzi adzauka, uku akuyang’ana modabwa kuti chachitika ndi chani. (Surah Zumar v. 68)
Mu Hadith ya Sunan Tirmizi, zanenedwa kuti pamene magawo awiri mwa atatu a usiku atapita, Rasulullah (sallallahu ‘alaihi wasallam) adadzuka nati:
يا أيها الناس اذكروا الله اذكروا الله جاءت الراجفة تتبعها الرادفة جاء الموت بما فيه
E inu anthu! Kumbukirani Allah, kumbukirani Allah Ta‘ala (kudzera mu salaah ndi kuchita ibaadah popeza Qiyaamah ikubwera posachedwa)! kugwedezeka kudzapangitsa chilichonse kugwedezeka mwamphamvu, (ndi) kugwedeza kwina pambuyo pake. Imfa idzabwera (kwa munthu aliyense) ndi chilichonse chomwe chili mkati mwake (monga zopweteka za imfa). (Musnad Ahmed #21241)
يَقُولُونَ أَإِنَّا لَمَرْدُودُونَ فِي الْحَافِرَةِ ﴿١٠﴾ أَإِذَا كُنَّا عِظَامًا نَّخِرَةً ﴿١١﴾ قَالُوا تِلْكَ إِذًا كَرَّةٌ خَاسِرَةٌ ﴿١٢﴾
(Anthu osakhulupirira) akuyankhula kuti: “Kodi ndi zoona kuti ife tidzaukitsidwanso tikadzamwalira monga tidaliri kale? “Chani?, ngakhale titadzakhala kuti taola ndikutsala mafupa okhaokha?, akumati, ngati zidzakhale choncho ndiye kuti tidzakhala otaika.”
M’mavesi awa, Allah Ta’ala akutidziwitsa za kuyankhula kosakhala bwino kwa osakhulupirira omwe adakana monyoza nkhani yokhudza kukhulupirira za kuuka kwa akufa ndi Qiyaamah. Sanathe kumvetsa momwe zingathekere kuukitsa matupi omwe adaola ndi kunyenyeka mpaka kusanduka fumbi.
Poyankha mawu a osakhulupirirawa, Allah Ta’ala akunena kutsogolo kwa surah imeneyi momwe adalengera kumwamba ndi dziko lapansi, kutsindika pa munthu kuti pamene Allah Ta’ala ali ndi mphamvu zolenga zinthu zosiyanasiyana zodabwitsa monga kumwamba ndi dziko lapansi, zingamuvute bwanji kudzaukitsa munthu yemwe ali m’gulu la zolengedwa zophweka kwambiri poyerekeza ndi kalengedwe ka dzuwa, milalang’amba, ndi zina zotero?
Allah Ta’ala akuti, “Kodi inuyo (anthu) ndi ovuta kwambiri (kwa Allah Ta’ala) kukulengani kapena kumwamba komwe adamanga? Iye adakweza kutalika kwake ndi kulongosora bwino, ndipo waphimba usiku wake ndi mdima, ndipo watulutsa (kuchokera mmenemo) kuwala kwake (zomwe ndi usana wake), ndipo pambuyo pake, Iye anayala dziko lapansi.”
فَإِنَّمَا هِيَ زَجْرَةٌ وَاحِدَةٌ ﴿١٣﴾ فَإِذَا هُم بِالسَّاهِرَةِ ﴿١٤﴾ هَلْ أَتَاكَ حَدِيثُ مُوسَىٰ ﴿١٥﴾
(kulira kwachiwiri kwa lipenga) udzakhala nkuwo wamphamvu omwe udzamveke kamodzi kokha, ndipo mwadzidzidzi, adzadzutsidwa (ndi kubweretsedwa ku chigwa cha Hashr kuti aweruzidwe).
Mawu oti “ساهرة” amatanthauza “pamwamba pa dziko lapansi”. Qiyaamah ikachitika ndipo Allah Ta‘ala kuononga dziko lonse lapansi, Allah Ta‘ala adzapanganso dziko lapansi. Dziko lapansi latsopano limene Allah Ta‘ala adzalipangenso likutchulidwa mu vesi ili ndi mawu oti “ساهرة”.
Dziko latsopanoli likadzalengedwanso, lidzakhala malo okongola komanso osalala. Sipadzakhala mapiri, nyumba kapena chilichonse cha dziko lapansi lakale chomwe chingakhale zizindikiro zodziwika ndi kuperekedwa kwa umwini.
هَلْ أَتَاكَ حَدِيثُ مُوسَىٰ ﴿١٥﴾إِذْ نَادَاهُ رَبُّهُ بِالْوَادِ الْمُقَدَّسِ طُوًى ﴿١٦﴾ اذْهَبْ إِلَىٰ فِرْعَوْنَ إِنَّهُ طَغَىٰ ﴿١٧﴾ فَقُلْ هَل لَّكَ إِلَىٰ أَن تَزَكَّىٰ ﴿١٨﴾ وَأَهْدِيَكَ إِلَىٰ رَبِّكَ فَتَخْشَىٰ ﴿١٩﴾ فَأَرَاهُ الْآيَةَ الْكُبْرَىٰ ﴿٢٠﴾ فَكَذَّبَ وَعَصَىٰ ﴿٢١﴾ ثُمَّ أَدْبَرَ يَسْعَىٰ ﴿٢٢﴾ فَحَشَرَ فَنَادَىٰ ﴿٢٣﴾ فَقَالَ أَنَا رَبُّكُمُ الْأَعْلَىٰ ﴿٢٤﴾ فَأَخَذَهُ اللَّهُ نَكَالَ الْآخِرَةِ وَالْأُولَىٰ ﴿٢٥﴾ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَعِبْرَةً لِّمَن يَخْشَىٰ ﴿٢٦﴾
Kodi nkhani ya Musah (‘alaihis salaam) siidakufikire? (Kumbukira) pamene Mbuye wake adamuitana ku chigwa chodala cha Tuwa; pita kwa Farao chifukwa wapyola malire . Kenako mufunse kuti, “Kodi ukufuna kuyeretsedwa ndikuti ndikutsogole kwa Mbuye wako kuti uzimuopa?” Kenako adamuonetsa chozizwitsa chachikulu, koma adatsutsa ndipo sanamvere. Kenako anatembenuka kubwelera, akuyesetsa kulimbana naye (kumutsutsa Nabi Musah ( alayhis salaam). Kenako adasonkhanitsa (afiti) uku akuitana anthu ake nati, “Ine ndine Mbuye wanu Wapamwambamwamba.” Choncho Allah Ta‘ala adamulanga , ndikumupanga kukhala chitsanzo cha chilango cha moyo omwe ulimkudza komanso cha dziko lino lapansi. Ndithudi, m’menemo muli chizindikiro kwa onse oopa Allah Ta‘ala.
Rasulullah (salallahu ‘alaihi wasallam) ankakhudzika kwambiri ndi mawu a ma kuffaar omwe ankatsutsana ndi Qur’aan Majeed ndipo ankakanira zoti kuli Qiyaamah. Pa chifukwa chimenechi, m’mavesi awa, Allah Ta‘ala akumukhazikitsa mtima pansi Rasulullah (salallahu ‘alaihi wasallam) potchula zomwe zidamuchitikira Nabi Musah (‘alaihis salaam) kwa Firaun, yemwenso adaukana uthenga wa Allah Ta‘ala pamene Nabi Musah (alaihis salaam) ankamuitanira ku Chisilamu.
Mu kuyankhula kwina, Rasulullah (salallahu ‘alaihi wasallam) akutonthozedwa ndi Allah Ta‘ala kuti vuto ili silinabwere kwa iwe wekha, koma Ambiyaa akale (‘alaihimus salaam) naonso adakumana ndi mavuto omwewa chifukwa cha deen. Choncho Allah Ta‘ala adamulanga ndi kumupanga kukhala chitsanzo cha chilango cha Tsiku Lomaliza komanso cha dziko lino lapansi lino.
Mawu oti “نكال” amatanthauza “chilango choopsa kwambiri chomwe chimaperekedwa kwa yemwe wachita chigololo kuti kuchitira ena kuti asadzalakwitsenso chinthu chomwecho.”
Mawu oti “chilango cha Aakhirah” akutanthauza chilango cha Tsiku Lomaliza chomwe chidzaperekedwe kwa Fir’aun. Mawu oti “chilango cha dziko lapansi lino” akutanthauza chilango chomwe chinaperekedwa kwa Fir’aun ndi gulu lake lankhondo padziko lino lapansi momwe adaonongedwera ndi kumira.
أَأَنتُمْ أَشَدُّ خَلْقًا أَمِ السَّمَاءُ ۚ بَنَاهَا ﴿٢٧﴾ رَفَعَ سَمْكَهَا فَسَوَّاهَا ﴿٢٨﴾ وَأَغْطَشَ لَيْلَهَا وَأَخْرَجَ ضُحَاهَا ﴿٢٩﴾ وَالْأَرْضَ بَعْدَ ذَٰلِكَ دَحَاهَا ﴿٣٠﴾ أَخْرَجَ مِنْهَا مَاءَهَا وَمَرْعَاهَا ﴿٣١﴾ وَالْجِبَالَ أَرْسَاهَا ﴿٣٢﴾ مَتَاعًا لَّكُمْ وَلِأَنْعَامِكُمْ ﴿٣٣﴾
Kodi inu (Inu anthu) ndi ovuta kwambiri kulenga (pamaso pa Allah Ta’ala) kapena thambo limene Iye adalimanga posonkhanitsa mbali zake ngati kutalika kwake ndi kulikonza, ndipo adaphimba usiku wake ndi mdima, ndipo adatulutsa kuwala kwake (omwe ndi usana), ndipo pambuyo pake, adayala dziko lapansi. Iye adatulutsa madzi ake ndi udzu wake, ndi mapiri – Iye adawakhazikitsa (padziko lapansi), (zonsezi zidachitika) kuti zikuthandizeni (ndi kugwiritsa ntchito) komanso kuti ziweto zanu zipindule.
مَتَاعًا لَّكُمْ وَلِأَنْعَامِكُمْ ﴿٣٣﴾
(Zonsezi zinachitika) ndi cholinga choti zikupindulireni ( pogwiritsa ntchito) inuyo pamodzi ndi ziweto zanu .
Mu ndime iyi, Allah Ta‘ala akufotokoza kuti Iye analiyala dziko lapansi, anachititsa kuti akasupe atuluke, anachititsa kuti mitsinje iziyenda, ndipo anabweretsa zabwino zake zobisika monga udzu, mitengo, ndi zipatso zomwe zimamera. Anakhazikitsanso mapiri ake kuti dziko lapansi likhale lokhanzikika bwino kuti anthu azikhala m’malo awo okhala. Zonsezi ndi njira yopindulira munthu. Munthu amadya ndi kusangalala ndi zabwino za dziko lapansi ndipo amapatsidwa ziweto zake kuti athe kupindula nazo ngati kudya kapena kukwera. Mwachidule, Allah Ta‘ala anapanga malo okhala padziko lapansi kukhala njira yomuthamdizira munthu, ndipo dongosolo la moyo uno lidzapitirira mpaka kumapeto kwa dziko lapansi.
فَإِذَا جَاءَتِ الطَّامَّةُ الْكُبْرَىٰ ﴿٣٤﴾ يَوْمَ يَتَذَكَّرُ الْإِنسَانُ مَا سَعَىٰ ﴿٣٥﴾ وَبُرِّزَتِ الْجَحِيمُ لِمَن يَرَىٰ ﴿٣٦﴾ فَأَمَّا مَن طَغَىٰ ﴿٣٧﴾ وَآثَرَ الْحَيَاةَ الدُّنْيَا ﴿٣٨﴾ فَإِنَّ الْجَحِيمَ هِيَ الْمَأْوَىٰ ﴿٣٩﴾ وَأَمَّا مَنْ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِ وَنَهَى النَّفْسَ عَنِ الْهَوَىٰ ﴿٤٠﴾ فَإِنَّ الْجَنَّةَ هِيَ الْمَأْوَىٰ ﴿٤١﴾
Choncho tsoka lalikulu likadzafika, tsiku limene munthu adzakumbukira zonse zomwe adachita ( zabwino ndi zoipa padziko lapansi), ndipo Moto wa Jahena udzaonetsedwa kuti onse aone, ndiye amene adapyora malire ndikusankha moyo wa dziko lapansi (kupitirira Moyo Womaliza), ndiye kuti Moto wa Jahena adzakhala malo ake okhalako. Ndipo amene ankaopa kuimilira pamaso pa Mbuye wake, ndipo anadziletsa ku zilakolako (zosaloredwa), ndiye kuti Jannah ndiye malo ake okhalako.
يَوْمَ يَتَذَكَّرُ الْإِنسَانُ مَا سَعَىٰ ﴿٣٥﴾
Tsiku lomwe munthu adzakumbuikire zonse zomwe adachita (zabwino ndi zoipa).
“Tsiku limene munthu adzakumbukira zonse zimene ankayesetsa kuchita” likutanthauza tsiku la chiweruzo kumene munthu adzaganizira ntchito zake zonse, zabwino ndi zoipa. Mu vesi lina, Allah Ta‘ala akufotokozanso kuti, Nthawi imeneyo munthu adzakumbukira, ndipo ndithudi, ali ndi kukumbukira.
فَأَمَّا مَن طَغَىٰ ﴿٣٧﴾ وَآثَرَ الْحَيَاةَ الدُّنْيَا ﴿٣٨﴾ فَإِنَّ الْجَحِيمَ هِيَ الْمَأْوَىٰ ﴿٣٩﴾
Ndipo amene adapyora malire ndikusankha moyo wa dziko lapansi (kusiya omwe ulinkudza), ndiye kuti kumoto ndikomwe adzakafikire ndikukhala malo ake okhalako.
Mu ndime iyi Allah Ta’ala, akufotokoza malo okakhala anthu osakhulupirira omwe sanamumvere Allah ndipo anasankha moyo wa dziko lapansi kuposa omwe ulinkudza. Mu kuyankhula kwina, adakonda zabwino za dziko lapansi kuposa chipembedzo ndipo sanakhulupirire mwa Allah, kotero malo ake omaliza adzakhala ku moto wa Jahannam ndipo chakudya chake chidzakhala zaquum (mtengo waminga waku jahannum) ndipo chakumwa chake chidzakhala hameem (madzi otentha aku jahannum).
وَأَمَّا مَنْ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِ وَنَهَى النَّفْسَ عَنِ الْهَوَىٰ ﴿٤٠﴾ فَإِنَّ الْجَنَّةَ هِيَ الْمَأْوَىٰ ﴿٤١﴾
Ndipo amene ankaopa kudzaima pamaso pa Ambuye wake (kuti apereke kaundura wa tchito zake) ndi kudziletsa ku zilakolako zoipa ndi zosapeweka, ndiye kuti Paradaiso adzakhala malo ake okhalako.
Mu ndime iyi, Allah Ta‘ala akufotokoza malo omwe akakhale anthu okhulupirira omwe ankaopa Allah m’moyo uno wa padziko lapansi ndipo amene ankaopa kudzaima pamaso pa Allah kuti apereke kau dura wake Tsiku Lomaliza.
Kuopa kumeneku kwa mlandu pa tsiku lomaliza kunawaletsa kukwaniritsa zilakolako zawo zakuthupi m’njira za haraam ndipo kunawapangitsa kukumbukira Allah Ta’ala ndikukhala omvera kwa Iye moyk wawo onse. Kwa akapolo otere, Allah Ta’ala akunena kuti malo awo omaliza ndi komwe akupita adzakhala paradaiso omwe Allah Ta’ala waakonzera akapolo Ake opaturika.
Mu Hadith ya Mtumiki swallallahu alaihi wasallam zanenedwa kuti kupatula madalitso omwe afotokozedwa (mu Qur’aan ndi Sunnah,) madalitso a Jannah ndi kufotokozera kwake ndi oti palibe diso lomwe lidawonako, palibe khutu lomwe lidamvapo, ndipo palibe munthu amene anaganizirako za zosangalatsa zake. (Saheeh Bukhaari #4780)
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu