Tafseer Ya Surah Naba

عَمَّ يَتَسَاءَلُونَ ‎﴿١﴾‏ عَنِ النَّبَإِ الْعَظِيمِ ‎﴿٢﴾‏ الَّذِي هُمْ فِيهِ مُخْتَلِفُونَ ‎﴿٣﴾‏ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ‎﴿٤﴾‏ ثُمَّ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ‎﴿٥﴾‏ أَلَمْ نَجْعَلِ الْأَرْضَ مِهَادًا ‎﴿٦﴾‏ وَالْجِبَالَ أَوْتَادًا ‎﴿٧﴾‏ وَخَلَقْنَاكُمْ أَزْوَاجًا ‎﴿٨﴾‏ وَجَعَلْنَا نَوْمَكُمْ سُبَاتًا ‎﴿٩﴾‏ وَجَعَلْنَا اللَّيْلَ لِبَاسًا ‎﴿١٠﴾‏ وَجَعَلْنَا النَّهَارَ مَعَاشًا ‎﴿١١﴾‏ وَبَنَيْنَا فَوْقَكُمْ سَبْعًا شِدَادًا ‎﴿١٢﴾‏ وَجَعَلْنَا سِرَاجًا وَهَّاجًا ‎﴿١٣﴾‏ وَأَنزَلْنَا مِنَ الْمُعْصِرَاتِ مَاءً ثَجَّاجًا ‎﴿١٤﴾‏ لِّنُخْرِجَ بِهِ حَبًّا وَنَبَاتًا ‎﴿١٥﴾‏ وَجَنَّاتٍ أَلْفَافًا ‎﴿١٦﴾‏ إِنَّ يَوْمَ الْفَصْلِ كَانَ مِيقَاتًا ‎﴿١٧﴾‏ يَوْمَ يُنفَخُ فِي الصُّورِ فَتَأْتُونَ أَفْوَاجًا ‎﴿١٨﴾‏ وَفُتِحَتِ السَّمَاءُ فَكَانَتْ أَبْوَابًا ‎﴿١٩﴾‏ وَسُيِّرَتِ الْجِبَالُ فَكَانَتْ سَرَابًا ‎﴿٢٠﴾‏ إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتْ مِرْصَادًا ‎﴿٢١﴾‏ لِّلطَّاغِينَ مَآبًا ‎﴿٢٢﴾‏ لَّابِثِينَ فِيهَا أَحْقَابًا ‎﴿٢٣﴾‏ لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرْدًا وَلَا شَرَابًا ‎﴿٢٤﴾‏ إِلَّا حَمِيمًا وَغَسَّاقًا ‎﴿٢٥﴾‏ جَزَاءً وِفَاقًا ‎﴿٢٦﴾‏ إِنَّهُمْ كَانُوا لَا يَرْجُونَ حِسَابًا ‎﴿٢٧﴾‏ وَكَذَّبُوا بِآيَاتِنَا كِذَّابًا ‎﴿٢٨﴾‏ وَكُلَّ شَيْءٍ أَحْصَيْنَاهُ كِتَابًا ‎﴿٢٩﴾‏ فَذُوقُوا فَلَن نَّزِيدَكُمْ إِلَّا عَذَابًا ‎﴿٣٠﴾‏ إِنَّ لِلْمُتَّقِينَ مَفَازًا ‎﴿٣١﴾‏ حَدَائِقَ وَأَعْنَابًا ‎﴿٣٢﴾‏ وَكَوَاعِبَ أَتْرَابًا ‎﴿٣٣﴾‏ وَكَأْسًا دِهَاقًا ‎﴿٣٤﴾‏ لَّا يَسْمَعُونَ فِيهَا لَغْوًا وَلَا كِذَّابًا ‎﴿٣٥﴾‏ جَزَاءً مِّن رَّبِّكَ عَطَاءً حِسَابًا ‎﴿٣٦﴾‏ رَّبِّ السَّمَاوَاتِ وَالْأَرْضِ وَمَا بَيْنَهُمَا الرَّحْمَٰنِ ۖ لَا يَمْلِكُونَ مِنْهُ خِطَابًا ‎﴿٣٧﴾‏ يَوْمَ يَقُومُ الرُّوحُ وَالْمَلَائِكَةُ صَفًّا ۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنْ أَذِنَ لَهُ الرَّحْمَٰنُ وَقَالَ صَوَابًا ‎﴿٣٨﴾‏ ذَٰلِكَ الْيَوْمُ الْحَقُّ ۖ فَمَن شَاءَ اتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِ مَآبًا ‎﴿٣٩﴾‏ إِنَّا أَنذَرْنَاكُمْ عَذَابًا قَرِيبًا يَوْمَ يَنظُرُ الْمَرْءُ مَا قَدَّمَتْ يَدَاهُ وَيَقُولُ الْكَافِرُ يَا لَيْتَنِي كُنتُ تُرَابًا ‎﴿٤٠﴾‏

Kodi akufunsana zachani? Za chochitika chachikulu chija, chomwe amatsutsana nacho? Ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kachiwiri, ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kodi sitidaichite nthaka kukhala ngati choyala chapansi, ndi mapiri kukhala ngati zikhomo; Ndipo takulengani awiriawiri (amuna ndi akazi), ndipo Tidalichita tulo tanu kukhala mpumulo. Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake) Ndipo taupanga usana kukhala nthawi yopezera zofunika za pamoyo wanu. Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba; Ndipo tidalenga nyali younikira (dzuwa), ndipo tatsitsa madzi ochuluka kuchokera kumitambo yodzadza ndi mvula;

Ndithu, tsiku lachiweruzo ndi nthawi yake (yomwe idakhazikitsidwa kale). Tsiku lomwe lipenga lidzaimbidwa ndipo inu mudzatuluka muli ambiri. Ndipo thambo lidzatseguridwa ndipo lidzakhala makomo makomo. Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake (ndikukhala fumbi) ndipo adzakhala ngati zideruderu. Ndithu, Jahannam ikuwadikira (oipa). (Ndi) malo a anthu otuluka M’chilamulo cha Mulungu. Adzakhala m’menemo kwa muyaya, Ndipo sadzalawa chilichonse choziziritsa m’menemo ngakhale chakumwa kupatula madzi otentha owira ndi mafinya. (Chilangochi) Ndi malipiro oyenera (olingana ndi machimo awo ndi zochita zawo). Ndithu, iwo sadali akuyembekezera Chiwerengero (cha Allah). Ndipo adazitsutsa zizindikiro zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) kotheratu. Ndipo chilichonse (chochokera m’zochita zawo) tachisunga mochilemba. Choncho Lawani (zipatso ndi zotsatira za zochita zanu), ndipo sitikuonjezerani chinthu china koma Chilango pa mwamba pa chilango.

Ndithu, akapolo owopa Allah adzakhala ndi kupambana kwakukulu, minda ndi zipatso za mphesa, ndi ma buthu (anamwali) ofanana misinkhu, ndi zikho zodzaza ndi zakumwa mpaka Mlomo. M’menemo sakamva mawu opanda pake komanso achabe ngakhale bodza. Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye Wako, Mbuye wakumwamba ndi nthaka ndi zonse zapakati pake, Wachifundo Chambiri. Palibe amene adzakhale ndi mphamvu yolankhula Naye, tsiku lomwe mzimu (Jibraiil [‘alaihis salaam]) Ndi angero adzaimirira m’mizeremizere. Sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloredwe ndi (Mulungu) Wachifundo Chambiri (Allah), ndipo adzanena zolondora. Limenelo ndi tsiku lenileni (losakaikitsa), ndipo amene afuna adzitchinjirize kwa Mbuye wake. Ndithu, Tikukuchenjezani za chilango chomwe chili pafupi, tsiku limene munthu adzayang’ana zimene manja ake adatsogoza, ndipo kafiri (munthu osakhulupilira) adzati: “Ndikadakhala dothi! (ndiye kuti sindikadakumana ndi chilango cha tsiku lareloli).

Ndemanga

عَمَّ يَتَسَاءَلُونَ ‎﴿١﴾‏ عَنِ النَّبَإِ الْعَظِيمِ ‎﴿٢﴾‏ الَّذِي هُمْ فِيهِ مُخْتَلِفُونَ ‎﴿٣﴾‏ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ‎﴿٤﴾‏ ثُمَّ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ‎﴿٥﴾

Akufunsana zachani? Za chochitika chachikulu chomwe amatsutsana nacho? Ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kachiwiri, posachedwapa iwo adzadziwa.

Ma Arabu achikunja sankakhulupilira za Qiyaamah ndipo ankaganiza kuti nzosatheka. Iwo anakana chifukwa ankaona kuti munthu akangosandutsidwa fumbi n’zosatheka kuti wina wake amuukitse.

Olemekezeka Abdullah bin Abbaas (Radhwiya Allaahu ‘anhuma) akusimba kuti pamene kuvumbulutsidwa kwa Qur’an kunkayamba, ma Arabu achikunja apnkakungana pamodzi kuti akambirane za chivumbulutsocho. Ankakambirana za chivumbulutso ndi kutsutsa, makamaka chivumbulutso chokhudza kubwera kwa Qiyaamah (kuuka kwa akufa ndi kukhalapo kwa chiweruzo). Choncho poyankha zokambirana za Arabu achikunja, Allah Ta’ala adavumbulutsa surayi momwe Allah Ta’ala adatsindika za kubwera kwa Qiyaamah.

Allah Ta’ala wayamba surayi ponena kuti: “Kodi akufunsana chiyani? Za chochitika chachikulu chomwe akukangana. zosatheka, posachedwa adzadziwa! Kachiwiri ayi! Posachedwapa adzadziwa!”

Mawu oti “naba” akutchulidwa m’ndime iyi. Mawu akuti “naba” amatanthauza nkhani ina yake. Komabe, molingana ndi ma Mufassireen (oyikira ndemanga Quraan), “naba” siikutanthauza nkhani iliyonse, koma m’malo mwake, ikutanthauza nkhani zina zofunika kapena chochitika chachikulu. Choncho, m’nkhani iyi Allah Ta’ala akuitcha Qiyaamah kuti ndi chochitika chachikulu.

كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ‎﴿٤﴾‏ ثُمَّ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ‎﴿٥﴾‏

Ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kachiwiri, posachedwapa iwo adzadziwa.

Mawu akuti “kalla” ndi otsutsa, ndipo amatanthauza kuti “ayi, ayi.” Mu ndime iyi, zikutanthawuza kuti nkhaniyi siingathe kumveka kudzera mukufunsa ndi kuyankha, kapena kukambirana ndi kutsutsana. Chowona chake chidzadziwika ndi iwo akadzakumana nacho. Ndi chowonadi chotere chomwe chilibe malo okayikirika, kukangana kapena kukana.

Qur’aan Majiid ikunena kuti posachedwa adziwa (ndipo mawu amenewa abwerezedwa kawiri kusonyeza kutsindika). M’mawu ena, akadzafa, adzazindikira zenizeni za dziko lotsatira. Kenako adzaona zoopsa za tsiku lomaliza ndi maso awo.

أَلَمْ نَجْعَلِ الْأَرْضَ مِهَادًا ‎﴿٦﴾‏ وَالْجِبَالَ أَوْتَادًا ‎﴿٧﴾‏ وَخَلَقْنَاكُمْ أَزْوَاجًا ‎﴿٨﴾‏ وَجَعَلْنَا نَوْمَكُمْ سُبَاتًا ‎﴿٩﴾‏ وَجَعَلْنَا اللَّيْلَ لِبَاسًا ‎﴿١٠﴾‏ وَجَعَلْنَا النَّهَارَ مَعَاشًا ‎﴿١١﴾‏ وَبَنَيْنَا فَوْقَكُمْ سَبْعًا شِدَادًا ‎﴿١٢﴾‏ وَجَعَلْنَا سِرَاجًا وَهَّاجًا ‎﴿١٣﴾‏ وَأَنزَلْنَا مِنَ الْمُعْصِرَاتِ مَاءً ثَجَّاجًا ‎﴿١٤﴾‏ لِّنُخْرِجَ بِهِ حَبًّا وَنَبَاتًا ‎﴿١٥﴾‏ وَجَنَّاتٍ أَلْفَافًا ‎﴿١٦﴾

Kodi sitidaichite nthaka kukhala choyala, ndi mapiri kukhala ngati zikhomo; Ndipo takulengani awiriawiri (amuna ndi akazi), ndipo Tidalichita tulo tanu kukhala mpumulo. Ndipo tapanga pamwamba panu mitambo isanu ndi iwiri yamphamvu; Ndipo tidalenga nyali younikira (dzuwa), ndipo tatsitsa madzi ochuluka kuchokera kumitambo yodzadza ndi mvula;

M’ndime izi muli chisonyezero cha Allah Ta’ala mphamvu zonse zomwe adalenga nazo zolengedwa zodabwitsa za chilengedwe chonse. Kudzera mwa Allah Ta’ala pofotokoza za m’mene adalengera chilengedwe chonse ndi zolengedwa zosiyanasiyana, akuonetsa mphamvu Zake za umulungu kwa munthu ndipo akutsimikizira kuti n’kosatheka kwa Iye kuwononga dziko lonse lapansi ndi kulilenganso kachiwiri.

Mu zolengedwa zonse zosiyanasiyana, kutchulidwa kwapadera kwaperekedwa ku chilengedwe cha dziko lapansi, mapiri, anthu, amuna ndi akazi, ndi kulengedwa kwa nyengo zoyenerana ndi moyo wa munthu, thanzi ndi ntchito zake Chimodzi mwa zinthu zomwe zatchulidwa pankhaniyi ndi kufunikira kwa tulo.

Ponena za kufunikira kwa mtendere umenewu, Allah Ta’ala akuti:

وَجَعَلْنَا نَوْمَكُمْ سُبَاتًا ‎﴿٩﴾

“Ndipo tidalichita tulo tanu kukhala mpumulo.”

M’ndime iyi, Allah Ta’ala akutchula mawu oti ‘subaat’. Mawu akuti “subaat” amachokera ku “sabt” kutanthauza kudula. Kugona ndi chinthu chomwe chimachotsa nkhawa ndi madandaulo omwe munthu angakhale nawo, kotero zimampatsa munthu mpumulo omwe sungapezeke ndi china chilichonse. Choncho, ma Mufassiriin amamasulira mawu akuti subaat kuti kupuma.

Kugona ndi gwero lalikulu la mpumulo ku chilengedwe chonse – kwa olemera ndi osauka, kwa ophunzira ndi osaphunzira, kwa mafumu ndi antchito.

Mphatso ya tulo imeneyi imaperekedwa kwa onse mofanana. Ngakhale olemera ndi ochita bwino ali ndi zonse zobweretsa mtendere m’nyumba zawo, monga mabedi, matiresi, mapilo, ndi zina zotero, koma mphatso ya tulo iyi sidalira zinthu ngati zimenezi.

Kaŵirikaŵiri, osauka, opanda pilo kapena zofunda kapena njira iriyonse yosangalalira, amasangalala ndi tulo tamtendere kulikonse kumene angakhale, pamene nthaŵi zina, olemera, ngakhale kuti ali ndi chilichonse zopezera mtendere, amavutika ndi kusowa tulo chifukwa cha nkhaŵa zamdziko ndi kuvutika maganizo. sangagone pokhapokha atamwa mapiritsi ogonetsa.

وَجَعَلْنَا اللَّيْلَ لِبَاسًا ‎﴿١٠﴾

Taupanganso usiku kukhala Chofunda.

M’ndime iyi, Allah Ta’ala akunena za ubwino wa usiku. Kuwala kwa masana kukamazimirira ndipo usiku ndkulowa, munthu mwachibadwa amakhala ndi tulo. Kupyolera mu usiku, Allah Ta’ala amapangitsa bata kukhala ponseponse ndipo sipamakhala phokoso ndi chipwirikiti chilichonse. Choncho, m’ndime iyi Allah Ta’ala akumuonetsa munthu kuti sadangomupatsa munthu tulo ngati mpumulo, komanso adalenga zinthu zapadziko mu nthawi ya usiku zomwe zimakhala zabwino ndi zoyenera kugona tulo kuti tulo ta munthu lisasokonezeke pa chilichonse mwanjira iliyonse.

Kupatulapo zimenezi, tulo limene Allah Ta’ala amampatsa munthu ndiloti limabweretsedwa kwa anthu ndi nyama nthawi imodzi usiku, kuti onse azigona mwamtendere komanso pakhale bata padziko lonse lapansi. Pakadakhala kuti pakhala nthawi zosiyanasiyana zogona kwa zolengedwa zosiyanasiyana, mtendere wamba ndi bata sizikanapezeka.

M’ndime ina, Allah Ta’ala akulongosora kuti kumpatsa munthu ulemelero waukulu wa usiku, umene munthu amakhala okhonza kupuma, ndi kudzera mu chisomo ndi mphamvu za Allah Ta’ala yekha. Allah Ta’ala akuti:

قُلْ أَرَأَيْتُمْ إِن جَعَلَ اللَّهُ عَلَيْكُمُ النَّهَارَ سَرْمَدًا إِلَىٰ يَوْمِ الْقِيَامَةِ مَنْ إِلَٰهٌ غَيْرُ اللَّهِ يَأْتِيكُم بِلَيْلٍ تَسْكُنُونَ فِيهِ ۖ أَفَلَا تُبْصِرُونَ ‎﴿٧٢﴾‏

Nena: “Tandiuzani, Mulungu akadakuikirani tsiku lopitira mpaka tsiku lachimaliziro, Ndi mulungu uti amene angakubweretsereni usiku oti mupumulemo? Ndiye, simukuona?” (Surah Qasas v. 72)

وَجَعَلْنَا النَّهَارَ مَعَاشًا ‎﴿١١﴾

Taupanganso Usana kukhala gwero la zinthu zamoyo.

Pamodzi ndi tulo, munthu amafuna zinthu zina zofunika pamoyo, monga chakudya, zakumwa, zovala, pogona. Pazifukwa izi, munthu akuyenera kupeza zofunika za pamoyo wake mnjira za halaal kuti athe kukwaniritsa zofunika pamoyo. Ngati dziko likanakhala ndi usiku okha popanda masana, ndipo munthu akupitiriza kugona nthawi zonse, kodi angapeze bwanji moyo wake ndi kukwaniritsa zofunika zina za pamoyo? Choncho, Allah Ta’ala adapanga usiku kuti munthu agone, ndipo adaupanga usana kuti munthu agwire ntchito ndi kusakasaka zofunikira za pa moyo.

وَأَنزَلْنَا مِنَ الْمُعْصِرَاتِ مَاءً ثَجَّاجًا ‎﴿١٤﴾‏

Ndipo tawatsitsa madzi ochuluka kuchokera kumitambo yodzaza mvula

Mawu oti “mu’siraat” ndi kuchulukitsa kwa “mu’sirah” kutanthauza “mitambo yodzaza ndi mvula”. Ndime imeneyi ikusonyeza kuti mvula imatsika kuchokera kumitambo, pamene mavesi ena akusonyeza kuti mvula imatsika kuchokera kumwamba. Komabe, palibe kutsutsana pakati pa mavesi onsewa, popeza kuti mitambo ili kumwamba. Choncho, m’ndime imodzi, mvulayo ikunenedwa kuti ikuchokera ku mitambo, ndipo m’ndime ina ikuti ikuchokera kumwamba.

اِنَّ یَوۡمَ الۡفَصۡلِ کَانَ مِیۡقَاتًا ﴿ۙ۱۷﴾

Ndithudi,tsiku lachiwerudzo ndi nthawi imene idakhazikitsidwa kale.

“Tsiku lachiweruzo” Limeneli ndi tsiku la Qiyaamah. (Tsiku lodzauka m’manda)Tsiku louka mmanda lidaikidwa nthawi yake yodziwika,ngati mmene wayankhulira Allah Ta‘ala Muvesi,kuti lidzachitika pamene Lipenga lidzaimbidwe.

Mukulongosora kwina zimaonetsa kuti lipenga lidzaimbidwa kawiri. likadzalizidwa koyamba,dziko lonse lidzatha. likadzalizidwa kachiwiri,anthu onse amdziko lonse,mibadwo yoyambilira komanso yotsirizira idzaukitsidwa kuchokera m’manda, ndipo idzabwera ku Malo ochitikira chiweruzo ali m’magulumagulu uku akukusidwa.

Olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallahu ‘anhu) akusimba kuti; Mtumiki wa Mulungu (Swallallahu ‘alaihi wasallam) adati, “Patsiku lachiwerudzo,anthu adzaukitsidwa m’manda nadzakhala magulu atatu ; Gulu lina lidzayenda ndi mapazi,gulu lina lidzakwera panyama ndipo gulu lina lidzayenda ndi nkhope zawo.” (Sunan Tirmizi #3142)

Mahadith ena akufotokoza kuti kudzakhala magulu khumi osiyanasiyana.Ndipo zikufotokozedwanso kuti,Magulu omwe adzapezeke pamalo achiweruziro adzagawidwa malingana ndi ntchito zawo komanso makharidwe awo.Ndipo palibe kutsutsana kulikonse pakati pamafotokozedwe onsewa,kamba koti mafotokozedwe ena akunena zamagulu ena, ndipo mafotokozedwe ena akunena zamagulu ena.

Check Also

Tafseer Ya Surah Lahab

بِسْمِ اللَّهِ الرَّحْمَٰنِ الرَّحِيمِ تَبَّتْ يَدَا أَبِي لَهَبٍ وَتَبَّ ‎﴿١﴾‏ مَا أَغْنَىٰ عَنْهُ مَالُهُ وَمَا كَسَبَ ‎﴿٢﴾‏ سَيَصْلَىٰ نَارًا …