عَمَّ يَتَسَاءَلُونَ ﴿١﴾ عَنِ النَّبَإِ الْعَظِيمِ ﴿٢﴾ الَّذِي هُمْ فِيهِ مُخْتَلِفُونَ ﴿٣﴾ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿٤﴾ ثُمَّ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿٥﴾ أَلَمْ نَجْعَلِ الْأَرْضَ مِهَادًا ﴿٦﴾ وَالْجِبَالَ أَوْتَادًا ﴿٧﴾ وَخَلَقْنَاكُمْ أَزْوَاجًا ﴿٨﴾ وَجَعَلْنَا نَوْمَكُمْ سُبَاتًا ﴿٩﴾ وَجَعَلْنَا اللَّيْلَ لِبَاسًا ﴿١٠﴾ وَجَعَلْنَا النَّهَارَ مَعَاشًا ﴿١١﴾ وَبَنَيْنَا فَوْقَكُمْ سَبْعًا شِدَادًا ﴿١٢﴾ وَجَعَلْنَا سِرَاجًا وَهَّاجًا ﴿١٣﴾ وَأَنزَلْنَا مِنَ الْمُعْصِرَاتِ مَاءً ثَجَّاجًا ﴿١٤﴾ لِّنُخْرِجَ بِهِ حَبًّا وَنَبَاتًا ﴿١٥﴾ وَجَنَّاتٍ أَلْفَافًا ﴿١٦﴾ إِنَّ يَوْمَ الْفَصْلِ كَانَ مِيقَاتًا ﴿١٧﴾ يَوْمَ يُنفَخُ فِي الصُّورِ فَتَأْتُونَ أَفْوَاجًا ﴿١٨﴾ وَفُتِحَتِ السَّمَاءُ فَكَانَتْ أَبْوَابًا ﴿١٩﴾ وَسُيِّرَتِ الْجِبَالُ فَكَانَتْ سَرَابًا ﴿٢٠﴾ إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتْ مِرْصَادًا ﴿٢١﴾ لِّلطَّاغِينَ مَآبًا ﴿٢٢﴾ لَّابِثِينَ فِيهَا أَحْقَابًا ﴿٢٣﴾ لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرْدًا وَلَا شَرَابًا ﴿٢٤﴾ إِلَّا حَمِيمًا وَغَسَّاقًا ﴿٢٥﴾ جَزَاءً وِفَاقًا ﴿٢٦﴾ إِنَّهُمْ كَانُوا لَا يَرْجُونَ حِسَابًا ﴿٢٧﴾ وَكَذَّبُوا بِآيَاتِنَا كِذَّابًا ﴿٢٨﴾ وَكُلَّ شَيْءٍ أَحْصَيْنَاهُ كِتَابًا ﴿٢٩﴾ فَذُوقُوا فَلَن نَّزِيدَكُمْ إِلَّا عَذَابًا ﴿٣٠﴾ إِنَّ لِلْمُتَّقِينَ مَفَازًا ﴿٣١﴾ حَدَائِقَ وَأَعْنَابًا ﴿٣٢﴾ وَكَوَاعِبَ أَتْرَابًا ﴿٣٣﴾ وَكَأْسًا دِهَاقًا ﴿٣٤﴾ لَّا يَسْمَعُونَ فِيهَا لَغْوًا وَلَا كِذَّابًا ﴿٣٥﴾ جَزَاءً مِّن رَّبِّكَ عَطَاءً حِسَابًا ﴿٣٦﴾ رَّبِّ السَّمَاوَاتِ وَالْأَرْضِ وَمَا بَيْنَهُمَا الرَّحْمَٰنِ ۖ لَا يَمْلِكُونَ مِنْهُ خِطَابًا ﴿٣٧﴾ يَوْمَ يَقُومُ الرُّوحُ وَالْمَلَائِكَةُ صَفًّا ۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنْ أَذِنَ لَهُ الرَّحْمَٰنُ وَقَالَ صَوَابًا ﴿٣٨﴾ ذَٰلِكَ الْيَوْمُ الْحَقُّ ۖ فَمَن شَاءَ اتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِ مَآبًا ﴿٣٩﴾ إِنَّا أَنذَرْنَاكُمْ عَذَابًا قَرِيبًا يَوْمَ يَنظُرُ الْمَرْءُ مَا قَدَّمَتْ يَدَاهُ وَيَقُولُ الْكَافِرُ يَا لَيْتَنِي كُنتُ تُرَابًا ﴿٤٠﴾
Kodi akufunsana zachani? Za chochitika chachikulu chija, chomwe amatsutsana nacho? Ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kachiwiri, ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kodi sitidaichite nthaka kukhala ngati choyala chapansi, ndi mapiri kukhala ngati zikhomo; Ndipo takulengani awiriawiri (amuna ndi akazi), ndipo Tidalichita tulo tanu kukhala mpumulo. Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake) Ndipo taupanga usana kukhala nthawi yopezera zofunika za pamoyo wanu. Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba; Ndipo tidalenga nyali younikira (dzuwa), ndipo tatsitsa madzi ochuluka kuchokera kumitambo yodzadza ndi mvula;
Ndithu, tsiku lachiweruzo ndi nthawi yake (yomwe idakhazikitsidwa kale). Tsiku lomwe lipenga lidzaimbidwa ndipo inu mudzatuluka muli ambiri. Ndipo thambo lidzatseguridwa ndipo lidzakhala makomo makomo. Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake (ndikukhala fumbi) ndipo adzakhala ngati zideruderu. Ndithu, Jahannam ikuwadikira (oipa). (Ndi) malo a anthu otuluka M’chilamulo cha Mulungu. Adzakhala m’menemo kwa muyaya, Ndipo sadzalawa chilichonse choziziritsa m’menemo ngakhale chakumwa kupatula madzi otentha owira ndi mafinya. (Chilangochi) Ndi malipiro oyenera (olingana ndi machimo awo ndi zochita zawo). Ndithu, iwo sadali akuyembekezera Chiwerengero (cha Allah). Ndipo adazitsutsa zizindikiro zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) kotheratu. Ndipo chilichonse (chochokera m’zochita zawo) tachisunga mochilemba. Choncho Lawani (zipatso ndi zotsatira za zochita zanu), ndipo sitikuonjezerani chinthu china koma Chilango pa mwamba pa chilango.
Ndithu, akapolo owopa Allah adzakhala ndi kupambana kwakukulu, minda ndi zipatso za mphesa, ndi ma buthu (anamwali) ofanana misinkhu, ndi zikho zodzaza ndi zakumwa mpaka Mlomo. M’menemo sakamva mawu opanda pake komanso achabe ngakhale bodza. Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye Wako, Mbuye wakumwamba ndi nthaka ndi zonse zapakati pake, Wachifundo Chambiri. Palibe amene adzakhale ndi mphamvu yolankhula Naye, tsiku lomwe mzimu (Jibraiil [‘alaihis salaam]) Ndi angero adzaimirira m’mizeremizere. Sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloredwe ndi (Mulungu) Wachifundo Chambiri (Allah), ndipo adzanena zolondora. Limenelo ndi tsiku lenileni (losakaikitsa), ndipo amene afuna adzitchinjirize kwa Mbuye wake. Ndithu, Tikukuchenjezani za chilango chomwe chili pafupi, tsiku limene munthu adzayang’ana zimene manja ake adatsogoza, ndipo kafiri (munthu osakhulupilira) adzati: “Ndikadakhala dothi! (ndiye kuti sindikadakumana ndi chilango cha tsiku lareloli).
Ndemanga
عَمَّ يَتَسَاءَلُونَ ﴿١﴾ عَنِ النَّبَإِ الْعَظِيمِ ﴿٢﴾ الَّذِي هُمْ فِيهِ مُخْتَلِفُونَ ﴿٣﴾ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿٤﴾ ثُمَّ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿٥﴾
Akufunsana zachani? Za chochitika chachikulu chomwe amatsutsana nacho? Ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kachiwiri, posachedwapa iwo adzadziwa.
Ma Arabu achikunja sankakhulupilira za Qiyaamah ndipo ankaganiza kuti nzosatheka. Iwo anakana chifukwa ankaona kuti munthu akangosandutsidwa fumbi n’zosatheka kuti wina wake amuukitse.
Olemekezeka Abdullah bin Abbaas (Radhwiya Allaahu ‘anhuma) akusimba kuti pamene kuvumbulutsidwa kwa Qur’an kunkayamba, ma Arabu achikunja apnkakungana pamodzi kuti akambirane za chivumbulutsocho. Ankakambirana za chivumbulutso ndi kutsutsa, makamaka chivumbulutso chokhudza kubwera kwa Qiyaamah (kuuka kwa akufa ndi kukhalapo kwa chiweruzo). Choncho poyankha zokambirana za Arabu achikunja, Allah Ta’ala adavumbulutsa surayi momwe Allah Ta’ala adatsindika za kubwera kwa Qiyaamah.
Allah Ta’ala wayamba surayi ponena kuti: “Kodi akufunsana chiyani? Za chochitika chachikulu chomwe akukangana. zosatheka, posachedwa adzadziwa! Kachiwiri ayi! Posachedwapa adzadziwa!”
Mawu oti “naba” akutchulidwa m’ndime iyi. Mawu akuti “naba” amatanthauza nkhani ina yake. Komabe, molingana ndi ma Mufassireen (oyikira ndemanga Quraan), “naba” siikutanthauza nkhani iliyonse, koma m’malo mwake, ikutanthauza nkhani zina zofunika kapena chochitika chachikulu. Choncho, m’nkhani iyi Allah Ta’ala akuitcha Qiyaamah kuti ndi chochitika chachikulu.
كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿٤﴾ ثُمَّ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿٥﴾
Ayi! Posachedwapa adzadziwa. Kachiwiri, posachedwapa iwo adzadziwa.
Mawu akuti “kalla” ndi otsutsa, ndipo amatanthauza kuti “ayi, ayi.” Mu ndime iyi, zikutanthawuza kuti nkhaniyi siingathe kumveka kudzera mukufunsa ndi kuyankha, kapena kukambirana ndi kutsutsana. Chowona chake chidzadziwika ndi iwo akadzakumana nacho. Ndi chowonadi chotere chomwe chilibe malo okayikirika, kukangana kapena kukana.
Qur’aan Majiid ikunena kuti posachedwa adziwa (ndipo mawu amenewa abwerezedwa kawiri kusonyeza kutsindika). M’mawu ena, akadzafa, adzazindikira zenizeni za dziko lotsatira. Kenako adzaona zoopsa za tsiku lomaliza ndi maso awo.
أَلَمْ نَجْعَلِ الْأَرْضَ مِهَادًا ﴿٦﴾ وَالْجِبَالَ أَوْتَادًا ﴿٧﴾ وَخَلَقْنَاكُمْ أَزْوَاجًا ﴿٨﴾ وَجَعَلْنَا نَوْمَكُمْ سُبَاتًا ﴿٩﴾ وَجَعَلْنَا اللَّيْلَ لِبَاسًا ﴿١٠﴾ وَجَعَلْنَا النَّهَارَ مَعَاشًا ﴿١١﴾ وَبَنَيْنَا فَوْقَكُمْ سَبْعًا شِدَادًا ﴿١٢﴾ وَجَعَلْنَا سِرَاجًا وَهَّاجًا ﴿١٣﴾ وَأَنزَلْنَا مِنَ الْمُعْصِرَاتِ مَاءً ثَجَّاجًا ﴿١٤﴾ لِّنُخْرِجَ بِهِ حَبًّا وَنَبَاتًا ﴿١٥﴾ وَجَنَّاتٍ أَلْفَافًا ﴿١٦﴾
Kodi sitidaichite nthaka kukhala choyala, ndi mapiri kukhala ngati zikhomo; Ndipo takulengani awiriawiri (amuna ndi akazi), ndipo Tidalichita tulo tanu kukhala mpumulo. Ndipo tapanga pamwamba panu mitambo isanu ndi iwiri yamphamvu; Ndipo tidalenga nyali younikira (dzuwa), ndipo tatsitsa madzi ochuluka kuchokera kumitambo yodzadza ndi mvula;
M’ndime izi muli chisonyezero cha Allah Ta’ala mphamvu zonse zomwe adalenga nazo zolengedwa zodabwitsa za chilengedwe chonse. Kudzera mwa Allah Ta’ala pofotokoza za m’mene adalengera chilengedwe chonse ndi zolengedwa zosiyanasiyana, akuonetsa mphamvu Zake za umulungu kwa munthu ndipo akutsimikizira kuti n’kosatheka kwa Iye kuwononga dziko lonse lapansi ndi kulilenganso kachiwiri.
Mu zolengedwa zonse zosiyanasiyana, kutchulidwa kwapadera kwaperekedwa ku chilengedwe cha dziko lapansi, mapiri, anthu, amuna ndi akazi, ndi kulengedwa kwa nyengo zoyenerana ndi moyo wa munthu, thanzi ndi ntchito zake Chimodzi mwa zinthu zomwe zatchulidwa pankhaniyi ndi kufunikira kwa tulo.
Ponena za kufunikira kwa mtendere umenewu, Allah Ta’ala akuti:
وَجَعَلْنَا نَوْمَكُمْ سُبَاتًا ﴿٩﴾
“Ndipo tidalichita tulo tanu kukhala mpumulo.”
M’ndime iyi, Allah Ta’ala akutchula mawu oti ‘subaat’. Mawu akuti “subaat” amachokera ku “sabt” kutanthauza kudula. Kugona ndi chinthu chomwe chimachotsa nkhawa ndi madandaulo omwe munthu angakhale nawo, kotero zimampatsa munthu mpumulo omwe sungapezeke ndi china chilichonse. Choncho, ma Mufassiriin amamasulira mawu akuti subaat kuti kupuma.
Kugona ndi gwero lalikulu la mpumulo ku chilengedwe chonse – kwa olemera ndi osauka, kwa ophunzira ndi osaphunzira, kwa mafumu ndi antchito.
Mphatso ya tulo imeneyi imaperekedwa kwa onse mofanana. Ngakhale olemera ndi ochita bwino ali ndi zonse zobweretsa mtendere m’nyumba zawo, monga mabedi, matiresi, mapilo, ndi zina zotero, koma mphatso ya tulo iyi sidalira zinthu ngati zimenezi.
Kaŵirikaŵiri, osauka, opanda pilo kapena zofunda kapena njira iriyonse yosangalalira, amasangalala ndi tulo tamtendere kulikonse kumene angakhale, pamene nthaŵi zina, olemera, ngakhale kuti ali ndi chilichonse zopezera mtendere, amavutika ndi kusowa tulo chifukwa cha nkhaŵa zamdziko ndi kuvutika maganizo. sangagone pokhapokha atamwa mapiritsi ogonetsa.
وَجَعَلْنَا اللَّيْلَ لِبَاسًا ﴿١٠﴾
Taupanganso usiku kukhala Chofunda.
M’ndime iyi, Allah Ta’ala akunena za ubwino wa usiku. Kuwala kwa masana kukamazimirira ndipo usiku ndkulowa, munthu mwachibadwa amakhala ndi tulo. Kupyolera mu usiku, Allah Ta’ala amapangitsa bata kukhala ponseponse ndipo sipamakhala phokoso ndi chipwirikiti chilichonse. Choncho, m’ndime iyi Allah Ta’ala akumuonetsa munthu kuti sadangomupatsa munthu tulo ngati mpumulo, komanso adalenga zinthu zapadziko mu nthawi ya usiku zomwe zimakhala zabwino ndi zoyenera kugona tulo kuti tulo ta munthu lisasokonezeke pa chilichonse mwanjira iliyonse.
Kupatulapo zimenezi, tulo limene Allah Ta’ala amampatsa munthu ndiloti limabweretsedwa kwa anthu ndi nyama nthawi imodzi usiku, kuti onse azigona mwamtendere komanso pakhale bata padziko lonse lapansi. Pakadakhala kuti pakhala nthawi zosiyanasiyana zogona kwa zolengedwa zosiyanasiyana, mtendere wamba ndi bata sizikanapezeka.
M’ndime ina, Allah Ta’ala akulongosora kuti kumpatsa munthu ulemelero waukulu wa usiku, umene munthu amakhala okhonza kupuma, ndi kudzera mu chisomo ndi mphamvu za Allah Ta’ala yekha. Allah Ta’ala akuti:
قُلْ أَرَأَيْتُمْ إِن جَعَلَ اللَّهُ عَلَيْكُمُ النَّهَارَ سَرْمَدًا إِلَىٰ يَوْمِ الْقِيَامَةِ مَنْ إِلَٰهٌ غَيْرُ اللَّهِ يَأْتِيكُم بِلَيْلٍ تَسْكُنُونَ فِيهِ ۖ أَفَلَا تُبْصِرُونَ ﴿٧٢﴾
Nena: “Tandiuzani, Mulungu akadakuikirani tsiku lopitira mpaka tsiku lachimaliziro, Ndi mulungu uti amene angakubweretsereni usiku oti mupumulemo? Ndiye, simukuona?” (Surah Qasas v. 72)
وَجَعَلْنَا النَّهَارَ مَعَاشًا ﴿١١﴾
Taupanganso Usana kukhala gwero la zinthu zamoyo.
Pamodzi ndi tulo, munthu amafuna zinthu zina zofunika pamoyo, monga chakudya, zakumwa, zovala, pogona. Pazifukwa izi, munthu akuyenera kupeza zofunika za pamoyo wake mnjira za halaal kuti athe kukwaniritsa zofunika pamoyo. Ngati dziko likanakhala ndi usiku okha popanda masana, ndipo munthu akupitiriza kugona nthawi zonse, kodi angapeze bwanji moyo wake ndi kukwaniritsa zofunika zina za pamoyo? Choncho, Allah Ta’ala adapanga usiku kuti munthu agone, ndipo adaupanga usana kuti munthu agwire ntchito ndi kusakasaka zofunikira za pa moyo.
وَأَنزَلْنَا مِنَ الْمُعْصِرَاتِ مَاءً ثَجَّاجًا ﴿١٤﴾
Ndipo tawatsitsa madzi ochuluka kuchokera kumitambo yodzaza mvula
Mawu oti “mu’siraat” ndi kuchulukitsa kwa “mu’sirah” kutanthauza “mitambo yodzaza ndi mvula”. Ndime imeneyi ikusonyeza kuti mvula imatsika kuchokera kumitambo, pamene mavesi ena akusonyeza kuti mvula imatsika kuchokera kumwamba. Komabe, palibe kutsutsana pakati pa mavesi onsewa, popeza kuti mitambo ili kumwamba. Choncho, m’ndime imodzi, mvulayo ikunenedwa kuti ikuchokera ku mitambo, ndipo m’ndime ina ikuti ikuchokera kumwamba.
اِنَّ یَوۡمَ الۡفَصۡلِ کَانَ مِیۡقَاتًا ﴿ۙ۱۷﴾
Ndithudi,tsiku lachiwerudzo ndi nthawi imene idakhazikitsidwa kale.
“Tsiku lachiweruzo” Limeneli ndi tsiku la Qiyaamah. (Tsiku lodzauka m’manda)Tsiku louka mmanda lidaikidwa nthawi yake yodziwika,ngati mmene wayankhulira Allah Ta‘ala Muvesi,kuti lidzachitika pamene Lipenga lidzaimbidwe.
Mukulongosora kwina zimaonetsa kuti lipenga lidzaimbidwa kawiri. likadzalizidwa koyamba,dziko lonse lidzatha. likadzalizidwa kachiwiri,anthu onse amdziko lonse,mibadwo yoyambilira komanso yotsirizira idzaukitsidwa kuchokera m’manda, ndipo idzabwera ku Malo ochitikira chiweruzo ali m’magulumagulu uku akukusidwa.
Olemekezeka Abu Hurairah (radhwiyallahu ‘anhu) akusimba kuti; Mtumiki wa Mulungu (Swallallahu ‘alaihi wasallam) adati, “Patsiku lachiwerudzo,anthu adzaukitsidwa m’manda nadzakhala magulu atatu ; Gulu lina lidzayenda ndi mapazi,gulu lina lidzakwera panyama ndipo gulu lina lidzayenda ndi nkhope zawo.” (Sunan Tirmizi #3142)
Mahadith ena akufotokoza kuti kudzakhala magulu khumi osiyanasiyana.Ndipo zikufotokozedwanso kuti,Magulu omwe adzapezeke pamalo achiweruziro adzagawidwa malingana ndi ntchito zawo komanso makharidwe awo.Ndipo palibe kutsutsana kulikonse pakati pamafotokozedwe onsewa,kamba koti mafotokozedwe ena akunena zamagulu ena, ndipo mafotokozedwe ena akunena zamagulu ena.
وَسُيِّرَتِ الْجِبَالُ فَكَانَتْ سَرَابًا
Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake (ndikukhala fumbi) ndipo adzakhala ngati zideruderu.
Mawu oti “suyyirat” (Adzachotsedwa) akutanthauza kuti mapiri, omwe ndi aakulu, okhanzikika komanso osasunthika adzachoka kulimba kwake ndipo adzasunthidwa kuchoka pamalo awo. Adzakhala ngati tinthu ting’onoting’ono ta fumbi tikuuluka m’mlengalenga.
Mawu akuti “saraab” kwenikweni amatanthauza “kuzimiririka” ndipo amatanthauzanso kuti zideruderu, chifukwa ngati zideruderu zimasowa munthu akaziyandikira. M’mawu ena, mapiri aakulu, amphamvu ndi ochititsa manthawo adzakhala ngati maso amadzi—madzi amene munthu woyenda m’chipululu amawaona kuchokera kutali, koma oyenda m’chipululu akafika pafupi, amazindikira kuti zimene amazionazo zinali zongopeka chabe.
Momwemonso mapiri, aakulu ndi amphamvu monga momwe adzaonekere Qiyaamah isadadze, adzasanduka ophwanyika ndi kuuluka ngati fumbi pambuyo pa kuyamba kwa Qiyaamah, kotero adzazimiririka ngati matope.
إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتْ مِرْصَادًا ﴿٢١﴾
Ndithu, Jahannum ili tcheru kudikilira.
Mawu oti “mirsaad” amatanthauza kubisalira kapena kukhala tcheru ndi kubwera kwa munthu wina wake
Kutengera momwe iliri nkhaniyi, Jahannum ikutanthauza mlatho umene uli pamwamba pa Jahannum umene angelo a chilango ndi malipiro akudikira.
Ndithu, amene kudalembedwa kukalowa ku Jahannam, Angelo a chilango akuwadikira, ndipo akamadzadutsa, adzawagwira ndi kuwapititsa ku Jahannum.
Nawonso angero oyang’ana za antuu ochita zabwino nawo ali tcheru kuwadikira amene akuyenera kulowa ku Jannat, ndipo adzadikira kuti adzatsaganewo waku Jannah.
Olemekezeka Hasan Basri (rahimahullah) adanena kuti padzakhala malo omwe angelo azidzapangira chipikicheni pomwe ndi pamlatho wa Jahannum. Aliyense okhala ndi chilorezo cholowa ku Jannah, adzaloredwa ndi angero kuti alowe; Koma iwo omwe adzapande kukhala ndi chilorezo cholowa ku Jannah, angelowa adzamuletsa kulowako.
لِّلطَّاغِينَ مَآبًا ﴿٢٢﴾
(Ndi) malo a anthu otuluka M’chilamulo cha Allah.
Ndime zam’mbuyomu zikuonetsa kuti mlatho wa Jahannum ndi malo obisaliridwa anthu onse, anthu abwino kapena oipa, pakuti onse adzayenera kudutsa mlathowo nthawi yoti awuoloke. Komabe, m’ndime iyi Allah Ta’ala akufotokozanso kuti Jahannum simalo a anthu olungama, koma ndi malo a anthu otuluka m’chilamulo cha Allah.
Choncho, mawu oti “taaghi” akutanthauza “munthu amene wapyola malire ponyoza malamulo a Allah Ta’ala”. Izi zikukamba za kaafir amene watsutsa ndi kukana ulamuliro wa Allah Ta’ala kwathunthu ndi kutsutsana ndi Chisilamu.
Angatanthauzenso magulu a Asilamu omwe adadzipatura okha ku chiphunzitso cha Qur-aan Yolemekezeka ndi Sunnah, ngakhale kuti sadatsatire kufr mwachonse ngati makafiri.
Magulu amenewa ndi monga ma Rawaafid, Khawaarij, Mu’tazilah ndi ena. Iwo amene zina mwa Zikhulupiriro zawo zimawapangitsa kukhala Makafiri, adzakhala mgulu limodzi ndi magulu ndime iyi ikunena.
لَّابِثِينَ فِيهَا أَحْقَابًا ﴿٢٣﴾
Adzakhala m’menemo muyaya
Mawu oti “ahqaab” ndi kuchuluka kwa “hiqbah” ndipo amatanthauza “mibadwo” kapena “nthawi yaitali”.
Akatswiri amasiyana maganizo pa tanthauzo lenileni la mawuwa.
Allaamah Ibnu Jariir (rahimahullah) adalemba kuti Hazrat Ali (radhwiyallahu ‘anhu) akunena kuti nthawi ya hiqbah ndi zaka makumi asanu ndi atatu, ndipo chaka chilichonse imakhala ndi miyezi khumi ndi iwiri, ndipo mwezi uliwonse umakhala ndi masiku makumi atatu, ndipo tsiku lililonse likufanana ndi zaka chikwi chimodzi.
Pa chifukwa chimenechi, hiqbah imodzi, yonse, idzakhala kuti ndi zaka mamiliyoni makumi awiri ndi makumi asanu ndi atatu mphambu zisanu ndi zitatu.
Hazrat Abu Hurairah, Hazrat Abdullah bun Umar, Hazrat ibnu Abbaas (radhwiyallahu anhum) ndi enanso amati hiqba imodzi imaimira zaka makumi asanu ndi awiri, zaka makumi asanu ndi atatu. Maganizo ena onse ndi ofanana ndi zomwe tafotokozazi.
Anthu ena amatsutsa ponena kuti anthu a ku Jahannum, akadzakhala kuti akhala mu Jahannum kwa zaka zambiri, adzatulutsidwa ku Jahannum. Chifukwa chomwe amafotokozera ndikuti ngakhale kutalika kwa hiqbah ndi kotani, komabe ndi nthawi yochepa ndipo pamapeto pake idzatha pakadzapita nthawi.
Komabe, mu chitabu chotchedwa Ma’aariful Qur’aan, Hazrat Mufti Shafee Saheb (rahimahullah) anatchulapo kuti poyang’ana ma Ayah ena omveka bwino a Qur’aan Majeed, tikuona kuti mtsutso umene akuperekawu ndi olakwika. Mu Qur’aan Majeed Allah Ta’ala akunena momveka bwino za anthu a ku Jahannum:
خلدين فيها ابدا
(Iwo, anthu osakhulupilira) adzakhala kumeneko (ku moto wa Jahannanm) kwamuyaya
Choncho, Ummah wagwirizana kuti Jahannum siidzaonongeka, ndiponso osakhulupirira sadzatulutsidwa m’menemo nthawi iriyonse.
Imaam Suddi (Rahimahullah) akusimba kuchokera kwa Murrah bin Abdillah (rahimahullah) kuti ngati akaidi a ku Jahannum atati adziwitsidwa kuti adzakhala ku Jahannum kwa zaka zingapo zofanana ndi miyala yonse yapadziko lapansi, atha kukhala okondwa ngakhale atadziwa chifukwa miyalayi, ngakhale kuti chiwerengero chake chili mabiliyoni, chilango chawo chili ndi nthawi yoikika. kapena idzafika kumapeto.
Ngati uthenga omwewu utaperekedwa kwa aklnthu a ku Jannah, kuti adzakhala ku Jannah kwa zaka zochuluka ngati miyala yapadziko lonse lapansi, zikadawawawa kumva zimenezo, ngakhale atakhala nthawi yaitali bwanji ku Jannah, pamapeto pake adzatulutsidwa ku Jannah pambuyo pake.
Choncho, mfundo yoti osakhulupirira adzamasuridwa ku Jahannum pakadzapita nthawi, ndi zosemphana ndi mawu omveka bwino komanso owonekera bwino a Qur’aan Majiid pamodzi ndi mgwirizano wa Ummah. Choncho, maganizo amenewa ndi olakwika.
Zikuyenera kumveka bwino kuti aya iyi siikunena zomwe zidzachitike pambuyo pa kutha kwa ahqaab. Ikungonena kuti iwo adzakhala mu Jahannum kwa zaka zambiri (ahqaab). Izi sizikutanthauza kuti sipadzakhala Jahannum pambuyo pa ahqaab, kapena kuti akaidi ake osakhulupirira adzamasuridwa.
Choncho, Hasan (Rahimahullah) akunena kuti palibe nthawi yeniyeni yomwe yafotokozedwa kwa akaidi a ku Jahannum ndipo pambuyo pake adzatulutsidwa. Koma osakhulupirira aweruzidwa kukhala mu Jahannum muyaya.
Choncho, nthawi iliyonse hiqbah (nyengo) ikatha, hiqbah yatsopano idzayamba; ndipo ikadzatha nyengo yachiwiri, hiqba yachitatu idzayamba; ndipo hiqbah yachitatu ikadzatha, hiqba yachinayi idzayamba; ndipo kuzungulira uku kudzapitirira motere mpaka muyaya.
Olemekwzeka Sa’iid bun Jubair (Rahimahullah) akumasuliranso liwu lakuti ahqaab kuti likunena za nthawi imene ilibe mapeto ake. Nthawi iliyonse ikatha, nyengo yatsopano idzaitsatira mpaka muyaya.
جَزَاءً وِفَاقًا ﴿٢٦﴾
(Chilango ichi) Ndi malipiro oyenera (olingana ndi machimo awo ndi zochita zawo).
Chilangochi, chomwe adzapatsidwe anthu ku Jahannam, chidzakhanzikika pa chilungamo komanso malipiro oyenera – chifukwa cha zikhulupiriro zabodza ndi zoipa zawo. Sadzaponderezedwa ngakhale pang’ono, pakuti izi ndi zimene Ayenera kuchita.
فَذُوقُوا فَلَن نَّزِيدَكُمْ إِلَّا عَذَابًا ﴿٣٠﴾
Choncho Lawani (zipatso ndi zotsatira za zochita zanu), ndipo sitidzakuonjezerani koma Chilango
M’mawu ena, m’dziko lapansi, adapitirizabe kum’kana Allah Ta’ala ndipo adapitiriza kuchita ukafiri. Ikadapanda kuwapeza imfa, akadapitiriza kuonjezera miyoyo yawo m’kusakhulupirira. Choncho, tsiku limenelo Allah Ta’ala adzawaonjezera chilango chifukwa cha kukanira kwawo malamulo a Allah Ta’ala.
Kufikira pano, m’surayi muli kulongosora za chilango cha osakhulupirira. Potsutsana ndi izi, pambuyo pake kukambidwa za malipiro ndi madalitso a okhulupirira ndi ochita zabwino.
إِنَّ لِلْمُتَّقِينَ مَفَازًا ﴿٣١﴾ حَدَائِقَ وَأَعْنَابًا ﴿٣٢﴾ وَكَوَاعِبَ أَتْرَابًا ﴿٣٣﴾ وَكَأْسًا دِهَاقًا ﴿٣٤﴾
Ndithu, akapolo abwino ali ndi kupambana kwakukulu, minda yampesa ndi mphesa, Anzake amsinkhu ofanana, ndi zikho (za vinyo osasa) zodzadza mpaka Mlomo.
Ndithu, akapolo abwino ali ndi kupambana kwakukulu, minda yamphesa ndi mphesa, Anzake amsinkhu wokwanira, ndi zikho (za vinyo wosasa) zodzaza mpaka Mlomo.
M’ndime izi Allah Ta’ala akutiuza kuti anthu okhala ndi taqwa (akapolo olungama a Allah Ta’ala) ndi amene adzapeze kupambana ndi zabwino za ku Jannah monga minda ya mpesa ndi mpesa za ku Jannah, anamwali aku Jannah, ndi vinyo wa ku Jannah.
Zabwino izi zikutchuridwa ngati zitsanzo za zabwino za Jannah. Kupatura zimenezi, pali madalitso osawerengeka omwe asungidwira akapolo oopa Allah Ta’ala omwe ali opitirira kuzindikira ndi kuzindikira kwa munthu.
M’ Hadith yolemekezeka ya Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) wanena kuti Allah Ta’ala wati: “Ndawakonzera akapolo Anga zabwino zomwe diso silinaonepo, khutu silinamvepo, ndiponso mtima wake siudalingalireko (ndi maganizo).” Kenako Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adati: “Ngati mufuna (kupeza izi m’Qur’aan), werengani ndime iyi: ‘Palibe amene akudziwa kuti chitonthozo cha diso chili chobisidwa kwa iwo – monga malipiro a ntchito zawo (zabwino).’” (Swahiyh Bukhaariy #3244).
Malinga ndi kunena kwa Imaam Mujaahid ndi Imaam Qataadah (rahimahumallah), kupambana kumene Allah Ta’ala akukunena m’ndime iyi kukukamba za kupambana kwamuyaya kopeza chipulumutso chamuyaya kumoto wa Jahannam ndi kukalowa ku Jannah.
لَّا يَسْمَعُونَ فِيهَا لَغْوًا وَلَا كِذَّابًا ﴿٣٥﴾ جَزَاءً مِّن رَّبِّكَ عَطَاءً حِسَابًا ﴿٣٦﴾
M’menemo sakamva mawu achabe ngakhale bodza.
Kenako Allah Ta’ala akutchula kuti m’minda ya Jannat ndi m’minda ya zipatso zaku Jannah, simudzakhala nkhani zopanda pake, ndipo sipadzakhala bodza, popeza kuti Jannah ndi malo aukhondo ndi ungwiro. Choncho palibe cholakwika chilichonse, zofooka ndi zoipa zapadziko monga zolankhula zopanda pake ndi bodza, zomwe zidzapezeke ku Jannah.
جَزَاءً مِّن رَّبِّكَ عَطَاءً حِسَابًا ﴿٣٦﴾
(Adzapatsidwa zabwino zimenezi) ngati malipiro ochokera kwa Mbuye Wako (zabwino) – mphatso yowerengeka (kapena mphatso yochuluka).
Madalitso a Paradiso amene anthu aku Jannah akalandire adzakhala malipiro a ntchito zawo zabwino komanso mphatso yochokera kwa Allah Ta’ala.
Apa m’ndime iyi mwatchulidwa zinthu ziwiri. Choyamba, madalitso amenewa ndi malipiro a ntchito zawo zabwino. Chachiwiri, iwo ndi mphatso yochokera kwa Allah Ta’ala kwa iwo. Mwachionekere, mbali ziŵirizi zikuoneka kuti ndi zotsutsana, chifukwa malipiro zimatanthauza kulandira kanthu kena kake chifukwa cha ntchito inayake yomwe wagwira, pamene mphatso imatanthauza kulandira chinachake mongopatsidwa.
Qur’aan Majeed yaphatikiza mawu awiriwa ndi cholinga chosonyeza kuti madalitso a ku Paradiso akungotengedwa ngati malipiro oonekera pa ntchito zabwino za anthu a ku Paradiso. Koma zoona zake n’zakuti madalitso amenewa ndi mphatso yochokera kwa Allah Ta’ala yoperekedwa kwa iwo kuchokera mu chisomo ndi chifundo Chake.
Chifukwa chake n’chakuti ntchito za munthu sizingakhale malipiro a ngakhale zabwino ndi madalitso amene amapeza m’moyo wawo wapadziko lapansi, kusiyapo madalitso ndi zabwino za tsiku lomaliza zomwe zimadalira chisomo cha Allah Ta’ala monga momwe zatchulidwira mu Hadith ya Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam), “Palibe amene angalowe ku Jannah pokhapokha ndi zabwino zake, pokhapokha Allah atasonyeza ubwino wake.
Ma Swahaabah (Radhwiya Allahu ‘anhum) adafunsa kuti: “Kodi zimenezi zikugwiranso ntchito kwa inu Mtumiki wa Allah Ta’ala (i.e. simungathe kulowa ku Jannah chifukwa cha ntchito zako zabwino)?” Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adati: “Ndipo sindidzalowa ku Jannah chifukwa cha ntchito zanga.
Mawu akuti hisaaba ali ndi matanthauzo awiri: [1] mphatso yowerengeredwa bwino, kapena [2] mphatso yochuluka kwambiri.
Malinga ndi kumasulira koyambirira (mphatso yowerengedwa bwino), tanthauzo lomwe likutuluka ndiloti anthu a ku Jannah adzalandira malipiro amenewa ngati chokhazikika chowerengedwa bwino pa ntchito zabwino zomwe adachita pa dziko lapansi, ndipo kawerengedwe kake kadzakhala kolingana ndi mlingo wa ikhlaas yawo ndi kugwirizana ndi lamulo la Allah Ta’ala.
Malinga ndi kumasulira kwachiwiri (mphatso yomwe ili yochuluka kwambiri), tanthauzo lomwe likutuluka ndiloti anthu a ku Jannah adzapatsidwa malipiro ochuluka kwambiri kuposa omwe anali oyenera. Choncho akadzaona malipiro aakulu, zidzabweretsa chisangalalo chachikulu ndi chimwemwe m’mitima mwawo chifukwa adzazindikira kuti ichi ndi chisomo cha Allah Ta’ala chomwe chili pa iwo, ndikuti sadali oyenerera zabwino zonse zomwe adalandira.
لَا يَمْلِكُونَ مِنْهُ خِطَابًا ﴿٣٧﴾ يَوْمَ يَقُومُ الرُّوحُ وَالْمَلَائِكَةُ صَفًّا ۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنْ أَذِنَ لَهُ الرَّحْمَٰنُ وَقَالَ صَوَابًا ﴿٣٨﴾
adzaima m’mizere motsatana. Sadzayankhula koma amene Wamlola (Allah) Wachifundo Chambiri (Allah), ndipo adzanena zoona.
Ndime iyi (Palibe amene adzakhale ndi mphamvu yolankhula Naye) mwina yalumikizana ndi aya yapitayi imene Allah Ta’ala akufotokoza za malipiro amene adzawapatse anthu aku Jannah. Pamene Allah Ta’ala akufuna kupereka malipiro alionse kwa aliyense, palibe amene adzakhale ndi ufulu ofunsa chigamulo cha Allah Ta’ala.
Komabe ndime iyi (Palibe amene adzakhale ndi mphamvu zolankhula Naye) ingakhalenso ndime yosiyana, yosalumikizana ndi ndime yapitayi. Pamenepa tanthauzo la ndimeyo ndikuti palibe mwa amene adzakhale pa malo a Mahshar osonkhanirana adzakhale ndi mphamvu zoyankhula popanda chilorezo Chake. Choncho, palibe amene adzayankhule kapena kupembedzera munthu popanda chilorezo cha Allah Ta’ala. Ndi anthu okhawo amene adzatha kulankhula ndi kupembedzera amene adzapatsidwe chilorezo ndi Allah Ta’ala.
Ruuh (mzimu) watchuridwa m’ndime iyi akukamba za Jibra’iil (‘alaihis salaam). Jibra’iil (‘alaihis salaam) adatchulidwa pamaso pa angero ena pofuna kusonyeza ukulu wa udindo wake.
يَوْمَ يَنظُرُ الْمَرْءُ مَا قَدَّمَتْ يَدَاهُ
tsiku limene munthu adzaona zimene manja ake atsogoza
Tsikuli ndi tsiku lachiweruzo. Patsiku limenelo, munthu aliyense adzaona ntchito zake ndi maso ake pa bwalo la Qiyaamah.
Kuona zochita za munthu ndi maso ake zikhoza kuchitika m’njira ziwiri: [1] buku la zochita zake lidzaperekedwa kwa iye m’manja mwake, ndipo adzaliona; kapena [2] zochita zake zidzaonekera pa bwalo la Qiyaamah zili m’maonekedwe ooneka, monga momwe zanenedwera ma Hadith ena.
Tsikuli lingatanthauzenso tsiku limene munthu wamwalira, ndipo mawu akuti “munthu adzaona zimene manja ake adatsogoza” akukamba za kuona zochita za munthu m’manda atamwalira. Kufotokozera uku kwafotokozedwa mu Tafseer-e-Mazhari.
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu