Tafseer

Tafseer Ya Surah Ma’un

Kodi mwamuona amene akukana (za tsiku la) Chiweruzo? iye ndi Yemwe akukankha (ndi kutsekereza) wa masiye, ndipo salimbikitsa Kudyetsa osauka. Mavuto akulu ali kwa amene akuswali, amene akunyalanyaza Swalah yawo. Iwo amene (amachita zabwino) podzionetsera, ndipo amakana kupereka (kapena kubwereketsa) ziwiya zawo ngakhale zinthu zazing’ono (zomwe anthu akuzifuna).

Read More »

Tafseer Ya Surah Quraish

لِإِيلفِ قُرَيْشٍ ‎﴿١﴾‏ اِلٰفِهِمْ رِحْلَةَ الشِّتَآءِ وَالصَّيْفِ ‎﴿٢﴾‏ فَلْيَعْبُدُوا۟ رَبَّ هٰذَا الْبَيْتِ ‎﴿٣﴾‏ الَّذِىٓ أَطْعَمَهُم مِّن جُوْعٍ وَاٰمَنَهُمْ مِّنْ خَوْفِۭ ‎﴿٤﴾‏ Chifukwa cha chitetezo cha ma Quraishi, chitetezo chimene amasangalala nacho m’maulendo awo m’miyezi yachisanu ndi m’nyengo yachilimwe. Kotero akuyenera kupembedza Mbuye wa nyumba yopatulika (Ka’aba), yemwe adawapatsa chakudya chothetsa njala yawo ndi chitetezo ku …

Read More »

Tafseer Ya Surah Feel

Kodi siudaone momwe Mbuye wako adawachitira anthu a Njovu? Kodi sadawaononge chiwembu chawo? Ndipo adawatumizira magulu ambalame mmagulumagulu otsatizana, ndikumawagenda ndi miyala yamoto; ndipo adawachita kukhala ngati mmera otafunidwatafunidwa ndiye walavuridwa.

Read More »

Tafseer Ya Surah Humazah

Tsoka kwa aliyense ochita miseche, wonyoza, wodziunjikira chuma ndikuchiwerengera! Akuganiza kuti chuma chake chidzamkhazika muyaya. Ayi! Ndithu, adzaponyedwa ku Hutwamah (kumoto waukali). Ndipo nchiyani chingakudziwitse kuti 'Hutamah' ndi chiyani? Ndi moto wa Allah woyatsidwa umene uzidzalowa m’mitima mwawo. (Motowo) udzatchingidwa ndi zipupa zitalizitali, ndi mizati yotambasulidwa (yotambasuka).

Read More »

Tafseer Ya Surah Asr

Ndikulumbilira nthawi; ndithudi munthu ndioluza, kupatula amene akhulupilira namagwira ntchito zabwino ndipo amalimbikitsana wina ndimnzake kutsatira choonadi komanso namalimbikitsana kupilira (komanso kupewa uchimo)

Read More »

Tafseer Ya Surah Qaari’ah

Kugunda kwaphokoso (la qiyaamah). Kodi kugunda kwaphokoso ndichiyani?. Ndichiyani chingakudziwise zakugunda kwaphokoso?. (Kugunda kwaphokoso kudzachitika)Tsiku limene anthu adzakhala ngati agulugufe obalalika. Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya omwazidwa. Tsono munthu amene muyeso wazinthu zabwino udzalemere(ndikupepuka zoipa). Ndiye kuti adzakhala osangalala pa tsiku lachiwerudzo. Ndipo amene muyeso wake wazabwino udzapepuke(ndikulemera zoipa). Ndiye kuti kumalo ake ofikila kudzakhala ku Hawiya(dzenje lamoto wa jahannama). Chingakudziwitse mchiyani zamoto wa Hawiya. Umenewo ndimoto oyaka mwaukali.

Read More »

Tafseer Ya Surah ‘Aadiyaat

Ndikulumbilira akavalo othamanga ali ndi phuma, Ndi otulutsa moto ku zikhotwa (pomenyetsa miyendo m'miyala), Ndi othira nkhondo adani m'mawa (dzuwa lisadatuluke), Ndi kuulutsa fumbi lambiri (kwa adani) nthawi imeneyo, Ndikulowelera mkatikati mwa adani. Ndithu munthu ali okanira mbuye wake (sathokoza Allah pa zimene amdalitsa nazo). Ndithudi iye pa zimenezi ndi mboni (yodzichitira yekha kupyolera mzochitachita zake). Ndipo ndithu iye ndi okonda chuma kwambiri (ndiponso ngwansulizo). Kodi sakudziwa zikadzatulutsidwa za mmanda, Ndikudzasonkhanitsidwa ndikuonekera poyera zomwe zidali m'mitima? Ndithu tsiku limenelo Mbuye wawo adzawadziwa kwambiri (ndikuwalongosolera zonse zochita zawo).

Read More »

Tafseer Ya Surah Zilzaal

Pamene nthaka idzagwedezedwe kugwedezedwa kwenikweni. Ndipamene nthaka idzatuluse mitolo yake. ndipo munthu adzati; ´´Kodi nthaka Yatani? ``. Patsikulo limeneli nthaka idzaulula nkhani zake, Chifukwa choti Mbuye wake adzayiwuza kuti Itero. Patsiku limeneli anthu adzapita kumalo achiweruzo ali mmagulumagulu kukaonetsa ntchito zawo. Choncho amene angachite ntchito yabwino yolemera ngati njere yampiru adzaiwona. Ndipo amene angagwire ntchito yoipa yolemera ngati njere yampiru adzayiwona.

Read More »

Tafseer Ya Surah Bayyinah

Anthu okanira mwa eni bukhu komanso ma Mushrikiin (opembedza mafano) sadafune kusiyana ndi umbuli wawo komanso zikhalidwe zawo kufikira chisonyezo chidawafikira amene ndi Mtumiki wa Allah kwawerengera makalata oyeretsedwa. M'mene mukupezeka malamulo olongosoredwa mom eka bwino. Omwe adapatsidwa mabukhu sadalekane/sadasemphane ndikugawanikana kufikira pomwe zisonyezo zoonekera poyera zidawadzera. Ndipo adangolamuridwa kumpembedza Allah kuchokera pansi pa mtima kukupanga kupembedza kukhala kwa Allah yekha osamphatikiza ndi zina. Ndikuswali komanso kupeleka Zakaat nthawi zonse ndikuti imeneyo ndiye dini yoongoka komanso.

Read More »

Tafseer Ya Surah Qadr

بِسمِ اللّٰـهِ الرَّحمٰنِ الرَّحيمِ اِنَّا أَنزَلنٰهُ فى لَيْلَةِ القَدْرِ ﴿١﴾ وَما أَدرىٰكَ ما لَيلَةُ القَدرِ ﴿٢﴾ لَيلَةُ القَدرِ خَيرٌ مِن أَلفِ شَهرٍ ﴿٣﴾ تَنَزَّلُ المَلـٰئِكَةُ وَالرّوحُ فيها بِإِذنِ رَبِّهِم مِن كُلِّ أَمرٍ ﴿٤﴾ سَلـٰمٌ هِىَ حَتّىٰ مَطلَعِ الفَجرِ ﴿٥﴾ Ndithudi, Tayimvumbulutsa Qur’an mu usiku wa Qadr (olemekezeka kwambiri). Ndipo chingakudziwitse nchiyani za usiku olemekezeka kwambiriwu (Usiku wa qadar). Usiku …

Read More »