Tsiku linalake Munthu wina anafika kwa Zainul Aabidiin, Aliy bin Husain rahimahullah ndipo adafunsa: Oh chidzukulu cha Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) maganizo anu ndi otani pa nkhani ya Uthmaan (radhwiyallahu anhu)? Atazindikira za nkwiyo wa munthuyu pa Uthmaan (radhwiyallahu anhu, Olemekeza Zainul Aabidiin (rahimahullah)adamulongosolera munthuyo kuti: Oh m’bale wanga okondeka! …
Read More »Mphavu za Aliyy (radhiyallahu anhu) pa nkhondo ya Uhud
Pa nkhondo ya Uhud ma swahabah (radhwiyallahu anhum) adagonjetsedwa kwambiri ndi adani ndipo ambiri adaphedwa kumene, Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) Adazunguliridwa ndi adani ndikuvulazidwa kwambiri, nthawi imeneyi mphekesera idayamba kumveka kuti Mtumiki waphedwa, maswahabah atamva mphekesera imeneyi adasweka mitima ndikutaya chiyembekezo. Hazrat Ali (radhwiyallahu anhu) akufotokoza kuti: tidazunguliridwa ndi adani …
Read More »Olemekezeka Talhah (radhwiyallahu anhu) pa nkhondo ya Uhud
Olemekezeka Zubair bin Awwaam (radhwiyallahu anhu) akufotokoza kuti pa nkhondo ya Uhud Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) adaphatikiza zovala zozitetezera pa nkhondo. Mkatikati mwa nkhondo Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) adafuna kukwera miyala ikulu ikulu koma ankakanika chifukwa chakulemera kwa zovala za pa nkhondo.Choncho adamupempha Olemekezeka Talha (radhwiyallahu anhu) kuti akhale pansi …
Read More »Chikondi chopanda malire cha maswahabah pa Mtumiki (swallallahu alaih wasallam)
Munthu wina adabwera kwa Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) nati, Oh Mtumiki wa Allah (swallallahu alaih wasallam) chikondi changa pa inu chili ponena kuti ndikangokuganizani ndimazadzidwa ndi chikondi chopanda malire, ndipo mtima wanga siumakhala mmalo pokhapokha ndikuoneni, Oh Mthenga wa Allah, maganizo amandifika kuti ngati Allah anganditenge ndikukandilowetsa ku Jannah zidzakhala zovuta kwa ine kuti ndidzakuoneni popeza inu mudzakhala Jannah ya pamwamba kwambiri yomwe ine sindingakwanitse kuifika.
Read More »Chikondi Cha Sahabah wina pa Mtumiki (sallallahu alaih wasallam)
Sahabah wina adabwera kwa Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) ndikufuna kuti oh Mthenga wa Allah kodi Qiyamah idzafika liti? Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adayankha pomufunsa kuti ndichani chomwe wachita sochinyeza kuikonzekera tsikulo? Sahabah adayankha nati, Oh Mthenga wa Allah sindikudzitenga kuti ndiri ndi swalah Saum kapena sadaqah zochuluka zomwe ndapanga komanso …
Read More »Chikondi chomwe Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) ankamuonetsera Mtumiki (sallallahu alaih wasallam)
Makafiri ali pafupi kuti amuphe sahabah Olemekezeka Zaid bin Dhathinah (radhiyallahu anhu) adamufunsa kuti ungasangalale kuti m’malo mwako timuphe Muhammad ndikuti iweyo tikusiye udzikasangalala ndi banja lako? Yankho lake lodabwitsa lidali loti ndikulumbira mwa Allah sindingalore kuti ine ndikhale ndi banja langa kumasangalala ndipo Muhammad akuvutika ngakhale kutakhala kubaidwa ndi …
Read More »Sayyiduna Abu Ubaidah (radhiyallahu) anhu aluza mano ake
Pankhondo ya Uhud Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adavulazidwa kwambiri ndi adani ndipo zitsulo za chipewa chake chodzitetezera pa nkhondo zinabaya pankhope yake yolemekezeka. Sayyiduna Abu Bakr Siddiq komanso Abu Ubaidah (Radhiyallahu anhuma) adathamangira kukamuthandizira Rasulullah (sallallahu alaih wasallam). Sayyiduna abu Ubaidah (radhiyallahu anhu) atafika pamene panali Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) …
Read More »Kukhudzidwa Kwa Mzimayi Wachi Answaari Pa Nkhani Ya Nabi (Sallallahu Alaih Wasallam)
Ku nkhondo ya Uhud asilamu adavutika kwambiri ndi kugonja komanso asilamu ambiri adaphedwa. Pamene nkhani yokhudzana ndi asilikali akunkhondo aja inawapeza anthu a ku Madina, amayi adatuluka m’nyumba zawo kufuna kudziwa m’mene nkhondo imayendera. Pamene anthu ena adakasonkhana pa malo ena ake mzimayi m’modzi wachi Ansaar adafunsa modandaula kuti kodi …
Read More »Uthenga Wa Sayyiduna Sa’d (Radhwiyallahu Anhu) Kupita Kwa Asilamu Onse
Nkatikati mwa nkhondo ya Uhud, Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adafunsa, “kodi Sa’d Bin Rabee alikuti? Sindikudziwa m’mene alili. ’kenaka, m’modzi mwa masahabah adatumizidwa kuti akamuyang’ane Sa’d (radhwiyallahu anhu), adapita pa malo pomwe anthu ofera ku nkhondo adagonekedwa. Adaitana mokuwa uku akutchula dzina la Sa’d kuti mwina adakali moyo. malo ena …
Read More »Chikondi cha olemekezeka Ali radhwiyallahu anhu pa Mtumiki Muhammad (swallallahu alaih wasallam)
Usiku umene Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) ankasamuka kupita ku Madinah Munawwarah makafiri adazungulira nyumba yake ndicholinga choti amuphe. Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) asadasamuke adamuuza Ali (radhwiyallahu anhu) kuti akagone ku nyumba ya Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) ndicholinga choti makafiri aganize ngati Mtumiki (swallallahu alaih wasallam) adakali m’nyumba momwemo sadatuluke ndipo …
Read More »