Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 5

13. Iwerengere Qur’an Majeed momveka bwino. Komabe, muyenera kupewa kutengera nyimbo ndi njira za oimba, ndi zina zotero.

Baraa bin Aazib (Radhwiyallah anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) anati: “Kongoletsani (kuwerenga kwanu) Qur’an Majeed kudzera m’mawu anu (poiwerenga momveka bwino).

Huzaifah (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) anati: “werengani Qur’an yolemekezeka m’mamvekedwe ndi kalembedwe Arabu, ndipo zisiyeni (kuwerenga) njira za Ahlul Kitaab ndi a anthu ochita zoipa. Posakhalitsa pambuyo panga adzabwera anthu amene adzawerengedwa Quraan ngati oimba, azibusa ndi anthu olira (ndi kulira). Kuwerenga kwawo sikungadutse m’mimero mwawo (siidzakwera kwa Allah ndi kulandiridwa chifukwa choiwerenga molakwika, kapena sikudzafika m’mitima mwawo ndi kukhudza mitima yawo), mitima yawo ndi mitima ya amene adzasangalatsidwe nawo adzadzazidwa (ndi chikondi cha dziko lapansi.

Abu Hurairah (Radhwiyallah anhu) akusimba kuti Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) adati: “Iye sali mwa ife amene samawerenga Qur’an momveka bwino.

Check Also

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 4

11.Werengani Quraan Majiid mwa tajwiid ndi matchulidwe olondola. Ngakhale mutamawerenga mwachangu, muyenera kuonetsetsa kuti mukuwerenga …