binary comment

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 6

14. Pamene mwatanganidwa ndi kuwerenga Qur’an Majiid, onetsani chidwi chanu pa Qur’an Majiid. Musatanganidwe ndi zokambirana zapadziko lapansi pakati panu mkatikati mowerenga, makamaka pamene Quraan ili yovundukura. Ngati pakufunika kuyankhula, ndiye kuti mutsirize Aayah yomwe mukuiwerengayo, mutseke Quraan mwaulemu, kenako yankhulani.

Zanenedwa kuti Ibnu Umar (radhwiyallahu anhuma) akamawerenga Qur’aan Majiid, sankatanganidwa nawonso zokambirana (zadziko) kufikira atamaliza kuwerenga.[1]

15. Potembenuza masamba a Quraan yolemekezeka, musanyowetse chala chanu ndi malovu kuti mutembenuze tsambalo. Izi sizikugwirizana ndi ulemu umene tikuyenera kuusonyeza ku Quraan yolemekezeka.[2]

16. Mukamaliza kuwerenga Qur’aan, muyenera kuchita ma dua chifukwa iyi ndi nthawi yoyankhidwa maduwa.

Thaabit (Rahimahullah) akusimba kuti nthawi zonse Anas bun Maalik (Radhwiyallahu anhu) akamaliza kuwerenga Qur’an Majiid, ankalisonkhanitsa banja lake ndi ana ake ndipo pambuyo pake amawapangira duwa.[3]

Ebrahim Taimi (rahmatullahi alaihi) akusimba kuti Abdullah bin Masuud (Radhwiyallahu anhuma) adati: “Amene wamaliza kuwerenga Qur’an Majiid (ndikupanga dua) dua yake idzalandiridwa,” Ebrahim Taimi (rahmatullahi aliahi) adanenapo kuti nthawi iliyonse Abdullah bin Mas’uud (Rdhwiyallahu anhuma) akamaliza kuwerenga Quraan, ankasonkhanitsa banja lake ndikuchita dua, ndipo ankati Aameen ku dua yake.[4]

Humaid (Rahimahullah) adanena kuti: “Amene amawerenga Qur’an kenako n’kupempha dua, angelo zikwi zinayi amanena kuti Aamiin ku duwa yake.[5]


[1]  صحيح البخاري، الرقم: 4526

[2] تعظيم القرآن والفقه واجب (فتاوى قاضيخان 3/261)

وأطال الإمام الكلام في هذا المقام بما لا يخفى حاله على من راجعه نعم لا شك في دلالة الآية على عظم شأن القرآن ومقتضى ذلك الاعتناء بشأنه ولا ينحصر الاعتناء بمنع غير الطاهر عن مسه بل يكون بأشياء كثيرة كالإكثار من تلاوته والوضوء لها وأن لا يقرأه الشخص وهو متنجس الفم فإنه مكروه وقيل: حرام كالمس باليد المتنجسة وكون القراءة في مكان نظيف والقارئ مستقبل القبلة متخشعا بسكينة ووقار مطرقا رأسه والاستياك لقراءته والترتيل والتدبر والبكاء أو التباكي وتحسين الصوت بالقراءة وأن لا يتخذه معيشة وأن يحافظ على أن لا ينسى آية أوتيها منه فقد أخرج أبو داود وغيره: عرضت عليّ ذنوب أمتي فلم أر ذنبا أعظم من سورة القرآن أو آية أوتيها رجل ثم نسيها وأن لا يجامع بحضرته فإن أراد ستره وأن لا يضع غيره من الكتب السماوية وغيرها فوقه وأن لا يقلب أوراقه بأصبع عليها بزاق ينفصل منه شيء فقد قيل بكفر من يفعل ذلك إلى أمور أخر مذكورة في محالها (روح المعاني 14/154)

[3] المعجم الكبير للطبراني، الرقم: 674، وقال العلامة الهيثمي رحمه الله في مجمع الزوائد، الرقم: 11713: ورجاله ثقات

[4] فضائل القرآن للقاسم بن سلام صـ 108، فضائل القرآن لابن الضريس، الرقم: 76

[5] سنن الدارمي، الرقم: 3524، قال الحافظ في نتائج الأفكار (3/177): هذا أثر منقطع وسنده ضعيف من أجل قزعة وحميد

Check Also

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 4

11.Werengani Quraan Majiid mwa tajwiid ndi matchulidwe olondola. Ngakhale mutamawerenga mwachangu, muyenera kuonetsetsa kuti mukuwerenga …