Sunnati Ndi Adaab 2

6. Pangani ma dua komanso azkaar musanagone;

اللَّهُمَّ بِاسْمِكَ أَمُوْتُ وَأَحْيٰ

O, Allah Talaa mdzina Lanu ndikufa komanso ndiuka

7. Gonerani kumanja ndikuika dzanja lanu lamanja pansi pa tsaya lanu lakumanja.

Bibi Hafsah (radiyallahu anha) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) akafuna kugona, ankaika dzanja lake lamanja pansi pa tsaya lake ndi kubwereza katatu mawu awa:

اللَّهُمَّ قِنِي عَذَابَكَ يَوْمَ تَبْعَثُ عِبَادَكَ

8. Osagona chafufumimba.

Olemekezeka Ya’eish Ghifaari (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti nthawi ina, ndinagona chafufumimba mu munzikiti chifukwa cha kuwawa kwa m’mimba. Mwadzidzidzi, munthu wina anabwera ndikundigwedeza ndi mwendo wake nati, “Kugona motere ( chamimba) n’kosasangalatsa kwa Allah Talaa) (ndinayang’ana kuti ndione amene ankandilankhula, kenako) ndinaona kuti ndi Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam).

9. Musagone maliseche kapena kuonetsa maliseche M’malo mwake, gonani mutavala zovala zomwe zingabise umaliseche wanu.

Anas (radhwiyallahu anhu) akunena kuti Abu Musah Ashari ankaphimba thupi lake (moyenera) akamagona kuonetsetsa kuti ziwalo zake zobisika sizikuonekera.

Check Also

Allah akuonetsera chisangalalo chake pa Olemekezeka Maswahabah (radhwiyallahu anhum) a Mtumiki (swallallahu alaih wasallam)

Ndipo amene adatsogolera poyamba, ochokera m'gulu la ma Muhajirina ndi Answari, ndi omwe adawatsatira Iwo mwaubwino, Allah adzakondwa Nawo. Naonso adzakondwera Naye (pa Zomwe adzapatsidwe ndi Allah.) Ndipo wawakonzera minda yomwe mitsinje lkuyenda pansipake; adzakhala M'menemo muyaya. Uko ndikupambana Kwakukulu.