Kufunika Kwa Dua 2

Dua Kupindulira Munthu Mnthawi ino ndi Mtsogolo

Olemekezeka Ibnu Umar (Radhwiyallahu anhuma) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Dua imapindulitsa pakalipano komanso mtsogolo. Choncho, inu akapolo a Allah, pirirani popempha.[1]

Yemwe amapanga Dua nthawi zonse Amapindula

Olemekezeka Abu Sa’iid Khudri (Radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Msilamu aliyense amene amapemphera kwa Allah ndi kum’pempha, ndipo duwa yake ilibe tchimo lililonse (ie kupempha chinthu choletsedwa) kapena kuthetsa ubale wakubanja. , Allah adzampatsa chimodzi mwa zinthu zitatu. adzampatsa zimene wapempha (padziko lapansi), kapena Adzamsungira malipiro a duwa ku Aakhirah, kapena adzamuchotsera tsoka.” Swahaabah adati: “Ngati ziri choncho, tidzichulukitsa kupempha.” Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) anayankha kuti: “Allah ndi oposa chilichonse (i.e, mphamvu Zake ndi chuma Chake nzoposa Zimene mukupempha).”.[2]

AUD-20240718-WA0002


[1] سنن الترمذي، الرقم: 3548، وقال: هذا حديث غريب لا نعرفه إلا من حديث عبد الرحمن بن أبي بكر القرشي وهو المكي المليكي وهو ضعيف في الحديث قد تكلم فيه بعض أهل الحديث من قبل حفظه

[2] مسند أحمد، الرقم: 11133، وقال العلامة الهيثمي رحمه الله في مجمع الزوائد، الرقم: 17210: رواه أحمد وأبو يعلى بنحوه والبزار والطبراني في الأوسط ورجال أحمد وأبي يعلى وأحد إسنادي البزار رجاله رجال الصحيح غير علي بن علي الرفاعي وهو ثقة

Check Also

Anthu Omwe Ma Duwa Awo Amayankhidwa 2

Munthu Yemwe Akudwala Olemekezeka Umar (Radhwiyallahu anahu) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Mukakumana …