Anthu Omwe Ma Duwa Awo Amayankhidwa 1

Makolo, Wapaulendo ndi Oponderezedwa

Olemekezeka Abu Hurairah (Radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Ma dua atatu ndi otero kuti pangavute bwanji adzalandiridwa; dua ya bambo (kapena mayi, pa mwana wawo), dua ya musaafir (munthu wapaulendo) komanso dua ya oponderezedwa.”[1]

Munthu Osala kudya komanso Mtsogoleri Wachilungamo

Olemekezeka Abu Hurairah (Radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Anthu atatu maduwa awo sangakanidwe; osala kudya kufikira atamasura swaum yake, mtsogoleri wachilungamo, ndi dua ya munthu oponderezedwa imene Allah amaikweza m’mwamba kumitambo, ndi imene makomo akumwamba amatsegulidwa, ndipo Allah amanena kuti: ‘Ndikulumbilira ulemerero wanga! Ndithu ndikuthandiza ngakhale patapita nthawi!’[2]

Mujaahid (Nsilikali) komanso Yemwe akuchita Haji kapena Umrah

Olemekezeka Abu Hurairah (Radhwiyallahu anhu) adasimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Mujaahid komanso amene akuchita Haji ndi umrah ndi nthumwi za Allah. Ngati amupempha Allah Iye amayankha mapemphero awo ndipo ngati apempha kanthu kwa lye, amawapatsa.”[3]

AUD-20240731-WA0013


[1] سنن الترمذي، الرقم: 3448، وقال: هذا حديث حسن

ولم يذكر الوالدة لأن حقها أكثر فدعاؤها أولى بالإجابة (مرقاة المفاتيح 4/1535)

[2] سنن الترمذي، الرقم: 3598، وقال: هذا حديث حسن

[3] سنن أبي داود، الرقم: 1535، سنن الترمذي، الرقم: 1980، وقال: هذا حديث غريب لا نعرفه إلا من هذا الوجه والأفريقي يضعف في الحديث

Check Also

Nthawi Zomwe Ma Dua Amayankhidwa

Nthawi ya Azaan ndi Pamene Magulu Awiri Akumana Pankhondo Olemekezeka Sahl bin Sa’d (Radhwiyallahu anhu) …