6. Chukuchani mkamwa ndikuthira madzi mphuno nthawi imodzi katatu. Kachukuchidwe kamkamwa ndikuthira madzi mphuno kali motere, choyamba tengani madzi mdzanja lanu lamanja, kenako, pogwiritsa ntchito madzi ena, tsukani mkamwa kamodzi otsalawo gwiritsani ntchito kutsuka mphuno, mudzabwereza zimenezi kawiri kotsalako pogwiritsa ntchito madzi ena ulendo wina uliwonse.
Read More »Njira Ya Sunnah Yopangira Wudhu Gawo lachiwiri
4. Sambitsani m'manja katatu.
Sayyiduna Humraan (rahimahullah) kapolo omasuridwa wa Uthmaan (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti: Sayyiduna Uthman (radhwiiyallahu anhu) anapempha madzi (kuti awaonetse anthu kapangidwe ka wudhu. kenaka anayama kupanga wudhu posambitsa manja ake (mpaka molumikizanirana dzanja) katatu (izi zafotokozedwazi zomwe zikupezeka mu sahihul bukhari sayyiduna Uthman (Radhwyallahu anhu) anati: ndidamuona Mtumiki (sallallahu alaihi wasallam) akupanga wudhu motere)."
Read More »Njira Ya Sunnah Yopangira Wudhu – Gawo loyamba
1. Mukamapanga wudhu, yang’anani ku qiblah komanso mukhale malo okwera (e.g. pampando kuti madzi omwe agwiritsidwa kale ntchito asakudonthokereni), malo omwe mukupangira wudhu akhale oyera.
Read More »Ma Ubwino A Wudhu
1. Wudhu ndi chiyeretso chamachimo ang’ono ang’ono.
Sayyiduna Uthmaan (radhwiyallahu anhu) akuti; Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati: Amene angachite-wudhu, ndipo nawuchita wudhuwo mkachitidwe kabwino kwambiri, Machimo ake (ang´onoang´ono) amafudutidwa (ndipo amatsukidwa) kuchokera mthupi mwake mpakana amagwa machimo kudzera pansi pa-zikhadabo.
Read More »Masaail (Nfundo) Zina Zokhudza Kuzithandiza Kuchimbudzi
1. Funso: kodi ndizoloredwa munthu kuwerenga mabukhu monga nyuzi ndi magazini, kapena kugwiritsa ntchito foni, kapenanso kuseweretsa intaneti pamene ali m’nchimbudzi?
Yankho: Chimbudzi ndi malo amene munthu amazithandizirako, Choncho sizabwino kwa munthu kugwiritsa ntchito foni yake kapena kuwerenga uthenga uliwonse kapena kuwerenga nkhani m'nchimbudzi.
Read More »Kapangidwe Ka Istinja (Kutawasa) Ka Sunnah ~ Gawo La chisanu Nchiwiri
21. Mukamaliza kudzithandizako, dikirani madontho otsalira kunkodzo wanu kuti amalizike musanapange wuzu.
Read More »Kapangidwe Ka Istinja (Kutawasa) Ka Sunnah ~ Gawo Lachinayi
11. Musayankhule pamene mukudzithandiza, pokhapokha patafunikira kuti mulankhule.
Sayyiduna Abu Hurairah (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti, Nabi (sallallahu alaih wasallam) adati, anthu awiri asakadzithandizire malo amodzi komwe akakhale ndikumayankhulana maliseche awo ali pantetete (osavala) ndithudi Allah Ta'ala amadana ndi nchitidwe otelewu.’’
Read More »Kapangidwe Ka Istinja (Kutawasa) Ka Sunnah ~ Gawo Lachitatu
7. Lowani kuchimbudzi ndiphanzi lamanzere.
8. Musavule chovala chanu chakumusi muli chiimire, m’malo mwake, chotsani chovala chanu chakumusichi mukamayandikira kunjuta pansi kuti pasadutse nthawi yayitali muli chivulire.
Read More »Kapangidwe Ka Istinja (Kutawasa) Ka Sunnah ~ Gawo Lachiwiri
4. Tchingani kumutu kwanu musanalowe kuchimbudzi.
Sayyiduna Habib bin Saalih (rahimahullah) akusimba kuti, Nabi (sallallahu alaih wasallam) ankavala nsapato zake ndikutchinga kumutu (kuvala chisoti) akamalowa kuchimbudzi”
Read More »Kapangidwe Ka Istinja (Kutawasa) Ka Sunnah ~ Gawo Loyamba
1. Mudzithandizire pamalo a nokhanokha posaonedwa ndi anthu.
Sayyiduna Jaabir (radhwiyallahu anhu) akunena kuti, Nabi (sallallahu alaih wasallam) ankati akafuna kudzithandiza, ankapita malo amene sangaonedwe ndi Anthu (anthu sangamuone).
Read More »
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu