Sayyiduna Umar (Radhwiyallahu ‘anhu) adafika kumalire a Shaam (Syria) atauzidwa za mliri omwe udawagwera anthu a ku Syria. Sayyiduna Umar (Radhiya Allaahu ‘anhu) adati: “Ngati imfa ingandifikire Abu ‘Ubaidah bin Jarraah (Radhiya Allaahu ‘anhu) akadali ndi moyo, ndiye kuti ndidzamuika kukhala Khalifa pambuyo panga, ndipo ngati Allah Ta’ala atafuna kundifunsa …
Read More »Kuwolowa manja ndi Zuhd (Kudzipatula padziko lapansi) kwa Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu)
Nthawi ina, Umar (Radhwiya Allahu ‘anhu) adatenga ndalama za golide mazana anayi, naziika m’thumba napereka kwa wantchito wake: “Pita kwa Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu) ndipo ukampatse ndalamazi. Ukakafika kumeneko ukadikire kwa kanthawi kuti ukawone zomwe akachite ndi ndalamazo (ndipo ukabwerere ndikundidziwitsa).” Kapoloyo anatenga thumba la ndalama za golide lija napita …
Read More »Zichitochito za Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu) Zigwirizana ndi Quraan Majiid
Pankhondo ya Badr, bambo a Abu Ubaidah Radhwiyallahu anhu adapitiriza kumulondora kufuna kuti amuphe. Komabe, iye anapitirizabe kuwapewa bambo akewo kuti asakumane nawo n’kuwapha. Komabe, iwowa atayesetsa ndikukumanizana naye maso ndi maso ndipo panalibe njira ina yopulumutsira moyo wake koma kuwapha, iye anapita patsogolo ndi kuwapha. Apa ndipamene Allah Taala …
Read More »Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu) aluza mano ake pa nkhondo ya Uhud
Pankhondo ya Uhud, Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adamenyedwa koopsa ndi adani ndipo mano awiri a chisoti chake chachitsulo chovala pankhondo adalowa mmatsaya ake odalitsika. Abu Bakr Siddiiq (Radhwiyallahu ‘anhu) ndi Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu) nthawi yomweyo anathamanga kukamuthandiza Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam). Abu Ubaidah (Radhwiyallahu ‘anhu) anayamba kuzula …
Read More »Khumbo la Umar (Radhwiyallahu ‘anhu) kudalitsidwa ndi Chipinda Chodzaza ndi Anthu monga Abu Ubaidah (radhiyallahu ‘anhu)
Umar (Radhwiyallahu ‘anhu) nthawi ina anakhala pansi ndi gulu la maswahabah pamene iye analankhula nawo ndipo kenako anafunsa funso lonena kuti, “Tandiuzani chimene anthu inu mukulakalaka” Munthu wina adati: “Chokhumba chomwe ndili nacho ndikuti chipinda chonsechi chitadzadza ndi ma dirham (ndalama zasiliva) ndikuti ndiwononge zonsezo panjira ya Allah Ta’ala.” Umar …
Read More »Kudalirika Kwenikweni Kwa Olemekezeka Abu Ubaidah bin Jarrah (Radhwiyallahu ‘anhu)
Anthu a ku Najraan atalowa Chisilamu, adadza kwa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) namupempha kuti awatumizire munthu odalirika (yemwe angakawaphunzitse Swalah). Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adati kwa iwo: لأبعثن إليكم رجلا أمينا حق أمين Ndidzatumizirani munthu okhulupirira ndi odalirika kwambiri. Pa nthawiyo, ma Swabsaabah (Radhwiyallahu anhum) omwe adalipo onse …
Read More »Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) Awapatsa ana ake aamuna maina pambuyo pa kuphedwa kwa ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum)
Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adanenapo kuti: “Ndithu, Talhah bin ‘Ubaidillah (Radhwiyallahu ‘anhu) amasunga mayina a Ambiyaa (‘alaihimus salaam) kwa ana ake, pomwe akudziwa kuti sipadzakhala Nabiy odzabwera pambuyo pa Mtumiki Muhammad (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam). Zubair (Radhwiya Allaahu ‘anhu) adati: “Ndimasungira ana anga maina a mashahidi (achi Swahaabah) kuti mwinanso …
Read More »Kulimba Mtima kwa Zubair (Radhiyallahu ‘anhu)
Patsiku la (nkhondo) ya Yarmuuk, ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) adati kwa Zubair (Radhiyallahu ‘anhu): “Bwanji siukupita ndi kukamenyana ndi adani, ndipo ife tidzakutsatira pokalimbana ndi adani.?” Zubair (Radhwiya Allahu ‘anhu) adayankha: “Ndikudziwa kuti ngati ndingapite anthu inu simungagwirizane nane.” Ma Swahaabah (Radhiyallahu ‘anhum) adati: “Ayi, ife tikugwirizana nawe ndipo tikutsatira.” …
Read More »Kuwolowa manja kwa Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu)
Hishaam bun Urwah akufotokoza kuti ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) okwana asanu ndi awiri adamusankha Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) kuti adzatenge udindo ogawa chuma chawo akadzamwalira. Ena mwa ma Swahaabawa anali Olemekezeka Abdur Rahmaan bin ‘Auf (Radhwiyallahu ‘anhu), Olemekezeka Miqdaad (Radhwiyallahu anhu) ndi Olemekezeka Abdullah bin Mas’uud (Radhwiyallahu ‘anhu) atamwalira, Zubair (Radhwiyallahu …
Read More »Kukhazikika pa Chisilamu
Abul Aswad akusimba motere. Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adamulandira Chisilamu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu, ndipo adapanga Hijrah ali ndi zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu. Amalume ake ankamukulunga munkeka ndikumampepelera utsi kuti abanike. Kenako ankamulamula kuti asiye Chisilamu ndipo iye ankayankha kuti: “Sindidzakhala Kaafir! Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) anali …
Read More »