Kuti dziko liziyenda bwino komanso mogwirizana, ndikofunikira kuti munthu aliyense alemekeze ufulu wa anthu ena.
Ngati ufulu wa anthu siulemekezedwa ndi kukwaniritsidwa, ndiye kuti chisokonezo ndi mikangano zidzafalikira padziko lonse lapansi. Kuba ndi kulanda chuma kudzakhala paliponse ndipo kuponderezana ndi kuphwanya malamulo kudzakhala chinthu chotchuka kwambiri.
Anthu adzapondereza ufulu wa ofooka ndi okalamba, akazi ndi ana, ndikuwagwiritsa ntchito chifukwa sangakwanitse kudziteteza okha ndikuteteza ufulu wawo.
Pa chifukwa chimenechi shari’ah chafotokoza ufulu wa anthu komanso momwe ufulu wawo uyenera kulemekezedwera.
Lamulo la Quraan Majiid Lokhudza Anansi
Mu Quraan Majiid, Allah Taala akuti:
“Onetsani kukoma mtima pa makolo, achibale, ana amasiye, osowa, mnansi wapafupi, mnansi wakutali ndi mnzanu yemwe mukukhala naye pafupi “
Mu ndime yomwe ili pamwambayi, ufulu wa anthu omwe Allah akukamba ndi ufulu wa anansi. Mmahadith olemekezeka Mtumiki sawallhu alayhi wassallam watsindika kwambiri zolemekeza ndi kusamala ma ufulu a neba.
Mtumiki sawallhu alayhi wassallam adati:
“Okhulupirira weniweni samadya mpaka kukhuta pomwe akudziwa kuti mnansi wake ali ndi njala.”
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu