بِسْمِ اللَّهِ الرَّحْمَٰنِ الرَّحِيمِ
عَبَسَ وَتَوَلَّىٰ ﴿١﴾ أَن جَاءَهُ الْأَعْمَىٰ ﴿٢﴾ وَمَا يُدْرِيكَ لَعَلَّهُ يَزَّكَّىٰ ﴿٣﴾ أَوْ يَذَّكَّرُ فَتَنفَعَهُ الذِّكْرَىٰ ﴿٤﴾ أَمَّا مَنِ اسْتَغْنَىٰ ﴿٥﴾ فَأَنتَ لَهُ تَصَدَّىٰ ﴿٦﴾ وَمَا عَلَيْكَ أَلَّا يَزَّكَّىٰ ﴿٧﴾ وَأَمَّا مَن جَاءَكَ يَسْعَىٰ ﴿٨﴾ وَهُوَ يَخْشَىٰ ﴿٩﴾ فَأَنتَ عَنْهُ تَلَهَّىٰ ﴿١٠﴾ كَلَّا إِنَّهَا تَذْكِرَةٌ ﴿١١﴾ فَمَن شَاءَ ذَكَرَهُ ﴿١٢﴾ فِي صُحُفٍ مُّكَرَّمَةٍ ﴿١٣﴾ مَّرْفُوعَةٍ مُّطَهَّرَةٍ
Iye (Mtumiki [swallallahu alaihi wasallam]) anachita tsinya natembenukira kumbali chifukwa chobwera kwa iye munthu wakhungu! Ndipo nchiyani chingakudziwitse (Iwe Muhammad [swallallahu alaihi wasallam] za momwe iye alili?) Mwina, (ngati utamusamalira,) akhoza kudziyeretsa, kapena angalandire uphunguwo, ndipo uphunguwo ukanamuthandiza. Kunena za amene sasamala (za imaan ndi deen), ndiye ukuwapatsa chidwi (chochulukirapo), pomwe palibe cholakwika pa iiwe atati asadziyeretse. (Koma) amene wabwera kwa iwe ndi molimba mtima, pamene akuopa (Allah Ta ‘ala ndi kudzayankha pa Tsiku Lomaliza), ndiye ukumusala! Sichoncho! (Siukuyenera kutero!) Ndithudi, (Qur’aan Majeed) ndi chikumbutso (ndi chenjezo). Basi, aliyense amene akufuna, aitsatire. (Qur’aan Majeed) yalembedwa m’mapepala olemekezeka, Apamwamba (ndi) oyeretsedwa, (yolembedwa) ndi manja a alembi (angelo omwe amailemba kuchokera ku Lawh-e-Mahfooz, angelo oterowo) omwe ndi olemekezeka (ndi) olungama.
Tsiku lina, Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) ankakambirana ndi atsogoleri ena a a Quraish, kuwaitanira ku Chisilamu. Mwa atsogoleriwa panali Utbah bin Rabee’ah, Abu Jahl bin Hishaam, ndi amalume ake olemekezeka, Olemekezeka Abbaas (radhwiyallahu ‘anhu), omwe mpaka nthawi imeneyo anali asanalowe Chisilamu.
Mkatikati mwa zokambiranazo, Olemekezeka Abdullah bin Ummi Makhtoom (radhwiyallahu ‘anhu), Sahaabi wakhungu wa Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam), anafika ndipo anayamba kumufunsa Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) mafunso ena okhudzana ndi deeni.
Mu nkhani ina yolembedwa ndi Allaamah Baghawi (rahimahullah), zatchuridwa kuti nkhani ya Hazrat Abdullah bin Ummi Makhtoom (radhiyallahu ‘anhu) pokhala wakhungu komanso osaona, sanazindikire kuti Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) akukambirana ndi atsogoleri achi Quraish. Kotero, atafika pa zokambiranazo, nthawi yomweyo anafunsa mafunso ake ndikusokoneza zokambiranazo.
Malinga ndi kunena kwa Haafiz Ibnu Katheer (rahimahullah), Ibnu Ummi Makhtoom (radhwiyallahu ‘anhu) ankafuna kuti Rasulullah (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) amuphunzitse ndime ya Qur’aan Majeed. Komabe, popeza kuti Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) adali atatanganidwa ndi kuwalalikira atsogoleri a ma Quraish ndikuwaitanira ku Deen, iye sadasonyeze chidwi pa Sahaabi ameneyu ndipo anapitiriza kuyankhulana ndi atsogoleriwo.
Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) adatsutsa kusokoneza kwa sahaabi, ndipo zisonyezo za kukana kwake ndi kuipidwa kwake zidawonekera pankhope yake yodalitsika.
Ndipamene Allah Ta’ala adavumbulutsa aya khumi ndi zinayi za kumayambiliro kwa surayi, kuti amukonzere Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) ndi kuulangiza ummah wake za momwe munthu angachitire zikamuchitikira zoterezi.
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu