Sahaabah

Kudalirika Kwenikweni Kwa Olemekezeka Abu Ubaidah bin Jarrah (Radhwiyallahu ‘anhu)

Anthu a ku Najraan atalowa Chisilamu, adadza kwa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) namupempha kuti awatumizire munthu odalirika (yemwe angakawaphunzitse Swalah). Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adati kwa iwo: لأبعثن إليكم رجلا أمينا حق أمين Ndidzatumizirani munthu okhulupirira ndi odalirika kwambiri. Pa nthawiyo, ma Swabsaabah (Radhwiyallahu anhum) omwe adalipo onse …

Read More »

Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) Awapatsa ana ake aamuna maina pambuyo pa kuphedwa kwa ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum)

Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adanenapo kuti: “Ndithu, Talhah bin ‘Ubaidillah (Radhwiyallahu ‘anhu) amasunga mayina a Ambiyaa (‘alaihimus salaam) kwa ana ake, pomwe akudziwa kuti sipadzakhala Nabiy odzabwera pambuyo pa Mtumiki Muhammad (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam). Zubair (Radhwiya Allaahu ‘anhu) adati: “Ndimasungira ana anga maina a mashahidi (achi Swahaabah) kuti mwinanso …

Read More »

Kulimba Mtima kwa Zubair (Radhiyallahu ‘anhu)

Patsiku la (nkhondo) ya Yarmuuk, ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) adati kwa Zubair (Radhiyallahu ‘anhu): “Bwanji siukupita ndi kukamenyana ndi adani, ndipo ife tidzakutsatira pokalimbana ndi adani.?” Zubair (Radhwiya Allahu ‘anhu) adayankha: “Ndikudziwa kuti ngati ndingapite anthu inu simungagwirizane nane.” Ma Swahaabah (Radhiyallahu ‘anhum) adati: “Ayi, ife tikugwirizana nawe ndipo tikutsatira.” …

Read More »

Kuwolowa manja kwa Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu)

Hishaam bun Urwah akufotokoza kuti ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) okwana asanu ndi awiri adamusankha Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) kuti adzatenge udindo ogawa chuma chawo akadzamwalira. Ena mwa ma Swahaabawa anali Olemekezeka Abdur Rahmaan bin ‘Auf (Radhwiyallahu ‘anhu), Olemekezeka Miqdaad (Radhwiyallahu anhu) ndi Olemekezeka Abdullah bin Mas’uud (Radhwiyallahu ‘anhu) atamwalira, Zubair (Radhwiyallahu …

Read More »

Kukhazikika pa Chisilamu

Abul Aswad akusimba motere. Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) adamulandira Chisilamu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu, ndipo adapanga Hijrah ali ndi zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu. Amalume ake ankamukulunga munkeka ndikumampepelera utsi kuti abanike. Kenako ankamulamula kuti asiye Chisilamu ndipo iye ankayankha kuti: “Sindidzakhala Kaafir! Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) anali …

Read More »

Kutengapo mbali pa Nkhondo ya Badr

Ismaa’eel bin Abi Khaalid akuti Bahiyy (Rahimahullah) adati: “Panali anthu apakavalo awiri okha omwe ankamenyana ndi adani pa nkhondo ya Badr. Wina adali Olemekezeka Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) yemwe ankalimbana ndi adani kudzanja lamanja, ndipo winayo adali Miqdaad bun Aswad (Radhwiyallahu ‘anhu), yemwe ankamenya nkhondo kumanzere. Hishaam bun Urwah akusimba kuti …

Read More »

Kusamalitsa pofotokoza Hadith yochokera kwa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam)

Abdullah bin Zubair (Radhwiya Allaahu ‘anhu) akuti nthawi ina adafunsa bambo ake (omwe ndi) Zubair radhwiyallahu ‘anhu kuti, “Bwanji simumafotokoza ma haadiith a Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam), monga momwe amachitira ma Swahaabah ena (Radhwiyallahu anhum)?” Olemekezeka Zubair (Radhwiya Allahu ‘anhu) anayankha kuti, “Sindinachokepo kumbali ya Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi …

Read More »

Kulandira dzina loti ‘Mthandizi Wapadera’ wa Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam)

Pankhondo ya Ahzaab, yomwe imadziwikanso kuti Nkhondo ya Khandaq (Nkhondo ya Ngalande), Asilamu adalandira uthenga kuti Banu Quraizah adaswa lonjezo lawo loti adzakhulupirika kwa Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) ndipo adajoina adani. Kuti atsimikize zomwe zamvekazi, Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) adawafunsa ma Swahaabah (Radhwiyallahu ‘anhum) kuti: “Ndani andibweretsere nkhani za anthu …

Read More »

Mabala owapeza munjira ya Allah Ta’ala

Hafs bin Khaalid (rahimahullah) akusimba kuti bambo wina wachikulire yemwe adafika kuchokera ku Mewsil adamuuza kuti ndidatsagana ndi Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) pa umodzi mwa maulendo ake. Pa nthawi ya ulendo. Pamene tinali malo otseguka, ouma, Zubair (Radhwiyallahu ‘anhu) ankafunika kusamba. Anatero kwa ine. “Ndibiseni (ndi nsalu kuti ndisambe).” Ndinamubisa motero, …

Read More »