Zinthu Zomwe Zimachititsa Kuti Mdalitso Wa Allah Uchoke

Kuipa Kojambula Zithunzi

Tiku lina Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) kulibe ali koyenda, Bibi Aaishah adapachika katani yokhala ndi zithunzi za zinthu zamoyo pakhomo.

Nthawiyo Sayyidah Aaishah (radhwiyallahu anha) sankadziwa kuti zithunzi za zinthu zamoyo zinali zoletsedwa.

Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) atafika kunyumba kwake ndipo maso ake anagwera pa katanilo anakwiya kwambiri. Aaishah anamulonjera, koma Iye sanayankhe moni wake ndipo nthawi yomweyo anapita pa nsaluyo ndikuing’amba.

Ataona momwe wachitira Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) Aaishah (radhwiyallahu anha) adazindikira kuti walakwitsa kwambiri, zomwe zachititsa kuti Mtumiki wa Allah asakondwere naye.

Modzichepetsa ndi kulapa kwakukulu, Adati: “Eh Mtumiki wa Allah (swallallahu alaihiwasallam)! Ndikutembenukira kwa Allah kulapa pa tchimo limene ndachita.

Mtima wa Aaishah (radhwiyallahu anha) udali odzazidwa ndi chikondi cha Allah Ta‘ala ndi Mtumiki Wake kotero kuti sakanatha kupirira kuipidwa kwawo ngakhale kwa mphindi imodzi. Choncho, ngakhale kuti sankadziwa za tchimo lomwe adachita, adathamangira kupanga taubah ndipo kenako adamupempha Mtumiki (swallallah alaihi wasallam) kuti amufotokozere tchimo limene anachita kuti asadzabwerezenso mtsogolo.

Rasulullah (swallallahu alaihi wasallam) kenako adamufotokozera zotsatira kuipa kwa tchimo lomwe anachita lopanga zithunzi. Rasulullah adati, “Eh Aaishah! Ndithudi anthu omwe amatenga gawo kujambula zithunzi za zinthu zamoyo adzalandira chilango choipa kwambiri Tsiku la Qiyaamah.”

Tikuyenera kukumbukira kuti monga ziliri kuti kupanga zithunzi za zinthu zamoyo ndi haraam, momwemonso kusunga zithunzi zotere sikukuloledwa. Jaabir (radhwiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adaletsa kusunga zithunzi za zinthu zamoyo m’nyumba, komanso kupanga zithunzi zotere.

Check Also

Munthu Olungama Kwambiri – Fudhail Bin Iyaaz Rahimahullah

Fudhail bun Iyaaz (Rahimahullah) aDali Muhaddith olemekezeka komanso oyera mtima wa m’nthawi yake. Allah Talaa …