Ulosi wa Rasulullah (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) okhudza Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) Kugonjetsa Qaadisiyyah

Pa mwambo wa Hajjatul Wadaa, Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) adadwala ku Makka Mukarramah ndipo ankaopa kuti amwalira. Rasulullah (Swallallaahu ‘alayhi wasallam) atabwera kudzamuona, adayamba kulira. Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adamfunsa: “Bwanji ukulira?” Sa’d (Radhwiyallaahu ‘anhu) adayankha: “Ndikuopa kuti ndingamwalilire m’dziko limene ndidachita Hijrah, ndipo kudzera mu kumwalilira kuno, malipiro …

Read More »

Ulaliki Oyamba Nzinda Wa Madinah Munawwarah Pambuyo Pa Nsamuko

Pa nthawi ya nsamuko Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) atalowa mu mzinda odalitsika wa Madina Munawwarah, anthu ambiri adali kuyembekezera mwachidwi kufika kwake. Ena mwa iwo ndi omwe ankamukonda kwambiri Mtumiki (swallallahu alaihi wasallam) monga ma Ansaar (radhwiyallahu anhum) a ku Madina Munawwarah komanso Ayuda ndi ena opembedza mafano omwe ankakhala …

Read More »

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 4

11.Werengani Quraan Majiid mwa tajwiid ndi matchulidwe olondola. Ngakhale mutamawerenga mwachangu, muyenera kuonetsetsa kuti mukuwerenga liwu lililonse momveka bwino ndi tajweed komanso katchulidwe koyenera. وَرَتِّلِ الْقُرْآنَ تَرْتِيلًا Ndipo werengani Qur’an momveka bwino ndi mwa tarteel (mwa pang’onopang’ono). Zanenedwa kuti nthawi ina munthu wina adadza kwa Abdullah bin Mas’uud nati: “Ndimawerenga Surah …

Read More »

Kukhazikika kwa Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) pa Imaan

Abu “Uthmaan (rahimahullah) anasimba kuti Sa’d (Radhwiyallahu ‘anhu) adati: “Ndime iyi ya Qur’aan idavumbulutsidwa ponena za ine. وَوَصَّيْنَا الْإِنسَانَ بِوَالِدَيْهِ حُسْنًا ۖ وَإِن جَاهَدَاكَ لِتُشْرِكَ بِي مَا لَيْسَ لَكَ بِهِ عِلْمٌ فَلَا تُطِعْهُمَا Ife tamulamula munthu kuchitira zabwino makolo ake. Ndipo (makolo Anu osakhulupirira) Akakukakamizani kuti Mundiphatikize (ndi chipembedzo Changa) …

Read More »

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 3

8. Umodzi mwa ma ufulu a Quraan Majiid ndi kulingalira zomwe zili mkati mwake ndi matanthauzo ake kuti uchite moyenera malamulo a Quraan Majiid. Choncho, pamodzi ndi kuwerenga Quraan Majiid, munthu ayesetsenso kuphunzira tanthauzo la ma surah osiyanasiyana a Quraan Majiid ndikofunikanso. Izi ziyenera kuchitika pansi pa Aalim oyenerera. Munthu …

Read More »

Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu) Kumuyang’anira Mtumiki (swallallaahu ‘alayhi wasallam)

Bibi ‘Aaishah (radhwiyallahu ‘anha) akufotokoza: Titasamuka kupita ku Madina Munawwarah, nthawi ina yake Rasulullah (swallallaahu ‘alayhi wasallam) sadagone usiku onse (kuopa kuti adani angamuchite chipongwe). Apa ndi pamene Mtumiki (swallallaahu ‘alayhi wasallam) adati: “Pakadakhala munthu owopa Allah kuti andidikilire usiku uno.” Tili chikhalire choncho, tinamva kulira kwa zida. Rasulullah (swallallaahu …

Read More »

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid 2

6. Ndi zoloredwa kuwerenga Quraan pafoni popanda wudhu. Komabe, munthu apewe kuyika dzanja lake kapena chala chake pa fonipo pomwe ndime za Qur’an zikuwonekera. Zindikirani: Tiyenera kukumbukira kuti ngakhale kuwerenga Qur’an pa foni nkoloredwa, kuwerenga Qur’an kuchokera m’bukhu monga m’mene ilili ndi zokondedwa kwambiri chifukwa kuteroko pali kutetezedwa kwa njira …

Read More »

Du’aa yapadera ya Mtumiki (Swallallaahu ‘alayhi wasallam)

Olemekezeka ‘Aaishah bint Sa’d (radhwiyallahu ‘anha), mwana wamkazi wa olemekezeka Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu), akufotokoza motere kuchokera kwa abambo ake, Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu): Pa nkhondo ya Uhud. (Pamene adani adaukira kumbuyo kwawo ndipo ma Swahaabah (radhwiyallahu ‘anhum) ambiri adaphedwa pabwalo lankhondo), ma Swahaabah (radhwiyallahu ‘anhum) sadathe kumpeza Mtumiki (swallallaahu ‘alayhi wasallam) …

Read More »

Sunnah komanso miyambo yoyenera kutsatira usanayambe Kuwerenga Quraan Majiid

1. Onetsetsani kuti mkamwa mwanu ndimoyera musanambe kuwerenga Qur’an Majiid. Kwanenedwa kuti Ali (radhwiyallahu anhu) adati: “Ndithu, pakamwa panu ndi njira ya Qur’an Majiid (pakamwa panu mumawerenga Qur’an Majiid). Pa chifukwa chimenechi, tsukani mkamwa mwanu pogwiritsa ntchito miswaak. 2. Inyamureni Quraan Majiid Mwaulemu kwambiri ndipo nthawi zonse iyikeni pamalo Olemekezeka …

Read More »

Maloto a Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu) Asanalowe Chisilamu

Sa’d (radhwiyallahu ‘anhu) anati: Ndisanalowe Chisilamu, ndinali ndi maloto omwe ndidawona ndili mumdima wandiweyani ndipo sanathe kuwona kalikonse. Mwadzidzidzi, panaoneka mwezi umene unayamba kuwala usiku. Kenako ndinatsatira kuwalako mpaka ndinakaufika mwezi M’malotowo, ndinaona ndithu anthu amene adanditsogolera kufikira mwezi. Ndidamuona Zaid bun Haarithah, Ali bun Abi Taalib ndi Abu Bakr …

Read More »