14. Onesetsani kuti mwathimisa foni yanu pamene mukulowa mumzikiti ndicholinga choti musasokoneze nayo anthu amene ali otangwanika ndimapemphero ndi ma ibaada ena ndi ena.[1] 15. Osajambula mafoto kapena kupanga vidiyo pamene muli mumzikiti. Kujambula foto komanso kupanga vidiyo chinthu chamoyo ndi Haraam mchisilamu. ndipo kuchita zimenezi mumzikiti nditchimo lalikulu. عن …
Read More »Masunnah Ochita Mumzikiti
13. Osakweza mawu kapena kuphokosera mumzikiti komanso malo onse odzungulila mnzikiti.
Olemekezeka Saib bin Yazeed akusimba kuti; Nthawi ina yake ndinali kugona munzikiti ndipo munthu wina anandiponya timiyala ting´ononoting´ono (ndicholinga chondidzusa), ndidayang´ana ndiye ndidapeza kuti adali Umar (radiyallah anhu). Iye adati kwa inept; Pita undibweresere anthu awiri amenewa kwa ine (amene akutsokoserawa), Ndipo ndinawabweretsa kwa Umar (radiyallah anhu), ndipo anawafunsa nati, Inu ndiochokera kuti? Iwo adayankha nati ndife ochokera ku Taif. Olemekedzeka Umar (radiyallah anhu) adati Inuyo mukadakhala ngati anthu amumadinah muno ndikadakupasani chilango chokhwima kwambiri Mukukweza inuyo mawu mumzikiti wa Mtumiki (salallah alayhi wasallama).
Read More »Masunnah Ochita Mumzikiti
9. Pangani chitsimikizo kuti mukupanga itikafu ya sunnah (nafl itikaaf) panthawi imene mungakhalire mumzikitimo.
10. Pempherani maraka awiri a Tahiyyatul masjid (olemekedzera mzikiti) pamene mwangolowa mumzikiti kumene.
Read More »Masunnah Ochita Mumzikiti
7. Lowani mumzikiti ndimwendo wamanja.
Kwanenedwa kuti Olemekezeka Anas radhiyallahu anhu adati; ndipo ndi sunnah (njira yamtumiki sallallah alayhi wasallam) pamene ukulowa mumzikiti kulowa ndimwendo wamanja ndipo potuluka kutsogoza mwendo wamanzere.
Read More »Masunnah Ochita Mumzikiti
6. Werengani maduwa pamene mukupita kumzikiti. Ena mwa maduwawo ndi awa: Dua yoyamba Amene angawerenge duwa iyi pamene akunyamuka ulendo wakumzikiti amakhala ndichifundo cha Allah chapadera ndiponso angelo okwanira 70,000 amamuchitiranso maduwa.[1] اَللّٰهُمَّ إِنِّيْ أَسْأَلُكَ بِحَقِّ السَّائِلِيْنَ عَلَيْكَ وَأَسْأَلُكَ بِحَقِّ مَمْشَايَ هٰذَا فَإِنِّيْ لَمْ أَخْرُجْ أَشَرًا وَلَا بَطَرًا وَلَا رِيَاءً …
Read More »Masunnah Ochita Mumzikiti
6. Werengani maduwa pamene mukupita kumzikiti. Ena mwa maduwawo ndi awa:
Dua yoyamba
Amene angawerenge duwa iyi pamene akunyamuka ulendo wakumzikiti amakhala ndichifundo cha Allah chapadera ndiponso angelo okwanira 70,000 amamuchitiranso maduwa.
Read More »Masunnah Ochita Mumzikiti
4. Pitani kumzikiti modekha ndi mwa ulemu. musapite mukuthamanga.
Olemekezeka Abu Hurayrah (radhiyallah anhu) adati; ndinamumva Mtumiki wa Allah (sallallah alayhi wasallam) akunena kuti; Pamene iqqamah yachitidwa, musapite kukapemphera swala pamene mukuthamanga, Mmalo mwake, Mukuyenera kuyenda modekha ndi mwaulemu. Gawo laswalah limene mwalipeza ndi Imaam, pempherani. Ndipo gawo lomwe lakudutsani kwanirisani. (pamene imaam watsiriza swalah)
Read More »Masunnah Ochita Mumzikiti
1. Valani moyenera pamene mukupita kumnzikiti
Allah ta’ala akuyankhula kuti: Oh Inu ana Aadam (alyhi salaam), zikongoleseni (valani zovala zozikongoletsera) pamene mukupemphera swalah munzikiti
Read More »Ma ubwino omwe munthu yemwe amakaswalira kunzikiti amapeza
4. Kupitapita kumzikiti ndi njira yokhayo yomwe ingateteze Dini ya munthu.
Sayyiduna Mu’adh bin Jabal (radhiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati, ndithudi satana ndi nkhandwe ya munthu (yomwe imansaka munthu kuti idye) monga m'mene nkhandwe ya ziweto imachitira yomwe imapezelera mbuzi yomwe ili yokhayokha, Pewani kukhala panokhanokha (kapena kutsata maganizo a okha) ndipo gwiritsitsani gulu la Ahlus-sunnah wal jamaa'ah ndikukhala limodzi ndi ummah komanso kulumikizana ndi mzikiti".
Read More »Ma ubwino omwe munthu yemwe amakaswalira kunzikiti amapeza
1. Kupangira wudhu kunyumba komanso Kuyenda kupita kunzikiti ndi njira yokhululukidwa machimo ndikukwezedwa ulemelero.
Sayyiduna Abu Hurairah (radhiyallahu anhu) akufotokoza kuti Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati: Munthu amene angapange wudhu kunyumba ndi Kuyenda wapansi kupita kunzikiti kuti akakwaniritse lamulo la Allah phanzi lirilonse lomwe angaponye amakhulukidwa machimo, ndipo phanzi lina lomwe angaponye adzakwezedwa ulemelero wake.
Read More »