Yearly Archives: 2026

Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wa sallam) Kuyamikira Kuwerenga Quran kwa Abdullah bin Mas’uud (Radhwiyallahu ‘anhu)

Umar (radhwiyallahu ‘anhu) adafotokoza nkhani iyi: Rasulullah (swallallahu ‘alayhi wasallam) ankakonda kulankhula ndi Abu Bakr (radhwiyallahu ‘anhu) akamaliza kuswali Esha ndikukambirana naye zokhuza Asilamu. Usiku wina, atamilza swalah ya Esha, Rasulullah (sallallahu ‘alayhi wasallam) adayamba kuyankhula ndi Abu Bakr (radhwiyallahu ‘anhu) (zokhudza Asilamu) ndipo inenso ndidali nawo pomwepo. Pambuyo pokambirana, …

Read More »

Nabi Isah ‘alaihis salaaam

Isa (‘alaihis salaam) ndi Mtumiki wa Allah Ta‘ala ndipo ali m’gulu la Aneneri apamwamba. Allah Ta‘ala adamuvumbulutsira Injeel (Baibulo) ndipo adamudaritsa ndi Shari’ah. Iye ndi Nabi amene anatumizidwa padziko lapansi Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) asanabwere. Rasulullah (swallallahu ‘alaihi wasallam) adati, “Ambiyaa onse (‘alaihimus salaam) ali ngati ana a bambo m’modzi. …

Read More »

Kudya

Chisilamu ndi Dini ya padziko lonse. Ndi ya nthawi zonse, malo onse ndi anthu onse. Ndi yangwiro komanso yokwanira, kotero kuti yamuonetsa munthu njira yokwaniritsira malamulo a Allah ndi ufulu wa akapolo ake. Munthu asadafike m’dziko kufikira kumwalira, Chisilamu chakhazikitsa malamulo ndi ziletso zomwe zingamuchititse kuti akhale osangalala. Kupatura kupemphera …

Read More »

Abu Zar (radhiyallahu ‘anhu) Apereka Uphungu kwa Mtsogoleri wa Asilikali Kuti Atsatire Chilungamo

Imaam Bayhaqi (rahimahullah) akunena kuti: Yazid bin Abi Sufyaan (radhiyallahu ‘anhu) pamene adali bwanamkubwa wa Shaam, Asilamu adachita Jihaad ndipo adapambana, motero adapeza chuma cholanda kwa adani. Mkatikati mwa katundu ameneyo mudalinso mtsikana okongola yemwe adaperekedwa kwa msilikali wina wachisilamu ngati gawo lake. Msilikaliyu atangolandira gawo lakeli (mtsikananayu), Yazid bin …

Read More »