Sayyiduna Aws bin Aws (radhiyallahu anhu) akusimba kuti Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati, “tsiku lopambana kwambiri ndi tsiku la Jumuah/lachisanu, kotero, Chulukitsani kundiwerengera durood tsiku limeneli popeza durood yanu imabweretsedwa kwa ine, masahabah adafunsa kuti, “durood yathu idzakufikani bwanji mukadzamwalira poti mafupa anu adzakhala ataola?” Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adayankha nati, “ndithudi Allah adailetsa nthaka kudya matupi a aneneri.”
Read More »Nthawi Zomwe Ndi Sunnah Kusambanthawi Zomwe Ndi Sunnah Kusamba
Pali nthawi zambiri zimene kusamba ndisunnah, zina mwa nthawizi ndi izi:
1.Tsiku la Jumua (lachisanu).
Sayyiduna Abullah bin Umar (radhwiyallahu anhuma) akunena kuti Mtumiki (Sallallahu alaih Wasallam) anati,” pamene wina mwainu akubwera ku swala ya Jumua (lachisanu) ayenera kusamba.”
Read More »Zikhulupiliro zokhudza Allah – 2
6. Palibe chilichonse chofanana ndi Allah Taala mayina ake ndi mbiri zake. Iye ndiokwanilira ulemelero wake ndi mbiri zake, palibe chinachirichonse chofanana ndi Allah Ta'ala mphamvu kapena maonekedwe. Iye Allah Ta'ala alibe maonekedwe kapena mtundu ofanana ndicholengedwa chirichonse.
Read More »Kulandila Satifiketi Yomasuridwa Ku Unaafiq Komanso Ku Moto Wa Jahannam
Sayyiduna Anas (radhiyallahu anhu) akusimba kuti, Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati, “amene anganditumizire Durood kamodzi ngati malipiro ya Durood Allah adzamulipira munthu ameneyo sawabu ndikumuchitira chifundo ka 10, ndipo amene anganditumizire Durood kokwana ka 10 Allah adzamulipira munthu ameneyo sawabu zokwana 100, ndipo munthu amene anganditumizire Durood kokwana ka 100 Allah adzamulembera chiphaso pakati pa maso ake yommasura ku ukamberembere komanso ku chilango cha Jahannam, Ndiponso Allah adzamulemekeza munthu ameneyo pa tsiku la Qiyaamah pomudzutsa ndi gulu la anthu omwe adafera ku nkhondo”.
Read More »Kasambidwe Ka Sunnah Gawo 5
Zokakamiza Posamba
Pali zinthu ziwiri zomwe ndizokakamizidwa kuchita ukamasamba,
1. Kupanga niya yosamba musanayambe kusambitsa thupi lanu.
2. Kuthira madzi thupi lonse.
Read More »Zikhulupiliro zokhudza Allah
1. Allah Ta ‘ala yekha ndamene akuyenera kumpembedza.
2. China chilichonse chisadapezeke pano padziko, kunalibe chilichonse kupatula Allah yekha, kenaka Allah adalenga chilichonse. Kupatula Allah, palibe amene alindi mphanu zolenga chinachirichonse kapena kupeleka moyo ndi imfa.
Read More »Kuyesedwa Kwa Durood Pa Mlingo Wokwanira
Sayyiduna Abu Hurairah (radhiyallahu anhu) akufotokoza kuti Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati, amene akufuna kuti Durood yake ikaikidwe pa sikelo ndikukalemera kwambiri kuti munthu akalandire mphotho yochuluka akatiwerengera Durood adzichulukitsa kuwerenga Durood iyi:
Oh Allah! Tumizani Durood kwa Muhammad (sallallahu alaih wasallam), Mtumiki amene anali osatha kulemba ndi kuwerenga, akazi ake onse, amayi a anthu onse omwe ndi okhulupilira, akubanja kwake ndi fuko lake lonse monga munatumizira Durood ku banja la nabi Ibrahim alaih salaam, ndinthudi ndiinu otamandidwa komanso olemekezeka.
Read More »Kasambidwe Ka Sunnah-Gawo 4
14. Onetsetsani kuti madzi akufika pena paliponse pathupi lanu, nthawi ina iliyonse mukadzithira madzi dzinyureni ndicholinga chofuna kuonetsetsa kuti madziwo alowa pakhungu lonse, ngakhale kutangotsala malo ochepetsetsa kwambiri osathiridwa madzi, kusamba (kwa fardh) sikudzatheka, pamene mukusambitsa thupi, sambitsani kutsogolo kwake kenako kumbuyo.
Read More »Kufunika kokhala ndi chikhulupiliro chenicheni (choyenera)
Chipembedzo chachisilamu pamodzi ndi nsanamira zake chagona pa chikhulupiliro chenicheni, ngati zikhulupiliro za munthu ndizolakwika, ngakhale kuti sizingamutulutse m’chisilamu, ngakhale atachita ntchito zabwino zachisilamu, sangalandire malipiro amene Allah adalonjeza, chifukwa choti zikhulupiliro zake ndi tsinde lenileni lachisilamu ndizolakwika.
Read More »Angelo Okwana 70 Kulemba Zabwino Kwa Masiku 1000
Sayyiduna Ibnu Abbas (radhiyallahu anhuma) akusimba kuti, Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati, “amene angawerenge Durood iyi, adzakhala ndi mwayi oti angelo okwana 70 adzamulembera zabwino kwa masiku okwana 1000.
Read More »
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu