admin

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 5

12. Pangani salaam polowa m’nyumba. Ngati m’nyumba mulibe aliyense, muyenera kupereka salaamu ponena kuti: السَّلَامُ عَلَيْنَا وَعَلَى عِبَادِ اللَّهِ الصَّالِحِينَ Mtendere ukhale pa ife ndi pa akapolo abwino a Allah. Olemekezeka Anas radhwiyallahu anhu adati: nthawi ina Rasulullah swallallahu alaihi wasallam adandiuza kuti: “E iwe mwana wanga okondedwa,ukamalowa m’nyumba mwako, …

Read More »

Kukhanzikika kwa Hazrat Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) pa Chisilamu

Hazrat Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) ndi Sahaabi otchuka pakati pa ma Swahaabah (radhwiyallahu ‘anhum), ndipo anali muazzin wa mzikiti wa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam). Poyamba, iye anali kapolo wa ku Abyssinia wa osakhulupirira ku Makkah Mukarramah. Kutembenuka kwake kukhala Msilamu sikunali kokondedwa ndi bwana wake, kotero adazunzidwa mopanda …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 4

9. Mawu a salaam amathera ndi “Wa barakaatuhu”. Munthu asawonjezere mau ena pambuyo pa “Wa barakaatuhu” Muhammad bin Amr bin Ataa rahimahu-Allah adanena kuti: Nthawi ina ndidali chikhalire ndi Abdullah bin Abbaas radhwiyallahu anhu pamene munthu wina ochokera ku Yemen adafika pamalopa ndipo adapereka salaam kuti: “Assalaamu alaikum wa rahmatullahi …

Read More »

Olemekezeka Sa’d bin Abi Waqqaas (Radhiyallahu ‘anhu) atenga nawo gawo kusambitsa thupi la Hazrat Saiid bin Zaid (Radhwiyallahu ‘anhu)

Olemekezeka Saiid bun Zaid (Radhwiyallahu ‘anhu) atamwalira, Hazrat Sa’d bun Abi Waqqaas (Radhiyallahu ‘anhu) ndi Hazrat Abdullah bun Umar (Radhwiyallahu ‘anhuma) adali m’gulu la anthu omwe adasambitsa thupi lake. Mwambo osambitsa utatha Jenezah idanyamuridwa ndi anthu ochokera ku Aqeeq kupita nayo ku Madina Munawwarah kuti akaikidwe ku manda otchedwa Baqi’ …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 3

6.Ziri Makruhu kupereka salaam kwa munghu yemwe watangwanika ndi ntchito ina ya Dini kapena akudya. 7. Musapereke salaam kwa omwe sali Mahram (Siwachibale). Ngati mkazi yemwe sali Mahram wapereka salaamu kwa mwamuna, koma kuti okalamba, ndipo palibe kuopa fitnah, akhonza kuyankhidwa. Komabe, ngati ndi mtsikana akupanga salaam, ndiye kuti munthu …

Read More »

Kufunikira Koti Mwana Adzicheza Ndi Anthu Abwino

Mu kulera mwana, ndi zofunika kwambiri kuti makolo azionetsetsa kuti mwana wawo nthawi zonse apezeka m’gulu la anthu ochita zabwino ndipo ndikupezeka malo abwino. Malo abwino komanso anthu opembedza adzasiya chikoka chokhanzikika pamtima wa mwanayo zomwe pambuyo pake zidzaumba kaganizidwe kake ndi kawonedwe kake ka moyo. Zotsatira zake, mwanayo adzakula …

Read More »

Kukhudzika kwa olemekezeka Sa’iid bin Zaid (radhwiyallahu ‘anhu) pa kusankhidwa kwa Khalifah.

Olemekezeka Umar (Radhwiyallahu ‘anhu) adakhala pansi ndi mwana wake Abdullah bun Umar, msuweni wake, Said bun Zaid, ndi Abbaas (radhwiyallahu ‘anhum). Umar (Radhwiya Allaahu ‘anhu) adawauza kuti: “Ndaganiza kuti sindidzaika munthu wina aliyense kukhala Khalifah pambuyo panga.” Olemekezeka Sa’iid bin Zaid (Radhwiya Allaahu ‘anhu) pokhudzika za ubwino wa Asilamu ndi …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 2

3. Njira ya Sunnat yakaperekedwe ka salaam ndi kupereka moni kwa Asilamu onse, osati achibale ake, abwenzi ake ndi amene akuwadziwa okha. Olemekezeka Abdullah bin Amr radhwiyallahu anhu akusimba kuti munthu wina adamufunsa Mtumiki Swallallahu alaihi wasallam “Kodi ndi chikhalidwe chanji ndi mChisilamu chomwe chili choyamikirika komanso chabwino?” Adayankha Mtumiki …

Read More »

Kulemekezeka kwa Sa’iid bin Zaid (Radhwiyallahu ‘anhu) pamaso pa Abdullah bin Umar (radhwiyallahu ‘anhuma)

Tsiku lina Abdullah bin Umar (Radhwiyallahu ‘anhuma) akukonzekera kupita ku Swalaah, adamva kuti amalume ake, Sa’iid bin Zaid (radhiyallahu ‘anhu) akudwala kwambiri ndipo atha kumwalira. Nkhaniyi idamufika pa nthawi yomwe adali atadzola kale (mafuta onunkhiritsa) thupi lake ndipo ali pafupi kuchoka kwawo kupita ku Swalaah ya Jumuah. Koma atamva nkhani …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 1

1. Ukakumana ndi Msilamu nzako, mupatse salaamu. Olemekezeka Ali radhwiyallahu anhu akunena kuti Mtumiki (Swallallahu alaihi wasallam) adati: “Msilamu ali ndi ma ufulu asanu ndi umodzi pa Msilamu nzake. Akakumana naye amlonjere (ndi salamu); ngati amuitana avomere kuitana kwake; akayetsemula amupangire duwa ponena kuti. ‘Yarhamukallah’ akadwala azikamuona akamwalira aziperekeza nawo …

Read More »