Yearly Archives: 2025

Olemekezeka Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) Msungichuma wa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam)

Olemekezeka Abdullah Al-Hawzani (rahimahullah) akufotokoza kuti nthawi ina adakumana ndi Bilaal (radhwiyallahu ‘anhu) ku Halab (mzinda wa Shaam). Atakumana ndi Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) adamufunsa kuti: “E, Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu)! Ndiuze momwe Nabiy (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) ankagwiritsira ntchito chuma chake (pa ntchito ya dini). Bilaal (Radhwiya Allaahu …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 8

26. Ndi adab (makhalidwe a usilamu) kuti pamene munthu wina akuyenda, wina wakhala pansi, ndiye kuti oyendayo ayambe kupereka salaamu ndi kupereka moni. Chimodzimodzinso, pamene wina ali m’sitima yapamadzi ndipo wina akuyenda, ndiye kuti okwerayo ayenera kuyamba kupereka salamu ndi kupereka moni. Chimodzimodzinso, achichepere ayenera kupereka moni kwa akuluakulu, ndipo …

Read More »

Kukhala Ndi Nkhawa Pa Maphunziro A Dini A Mwana

Fuko lodalitsidwa ndi maphunziroo a Dini ndi kumvetsetsa komveka bwino komanso ndi fuko lopita chitsogolo komanso lachitukuko lomwe lili ndi tsogolo labwino. Mbali inayi, mtundu opanda maphunziro a Dini ndi kuzindikira koyenera ndi mtundu omwe ukupita kuchiwonongeko ndi kulephera. Ndichifukwa chake Nabi aliyense akatumizidwa ku fuko linalake, ndiye kuti imodzi …

Read More »

Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) Aitana Azaan pa Ka’bah

Nthawi ya Fath-e-Makkah (Kugonjetsa kwa Makka), Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) adalowa mu Ka’bah Shariif pamodzi ndi Bilaal (radhwiyallahu ‘anhu) komanso Usaamah (radhwiyallahu ‘anhu). Pa nthawiyo, Mzikiti udali odzadza ndi ma Quraishi omwe adali mmizeremizere, akumuyang’ana Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) kuti aone zimene achite ndi momwe awachite …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 7

21. Pamene mukudzithandiza, musapereke salaamu kwa munthu aliyense kapena kuyankha salamu ya munthu aliyense. Chimodzimodzinso, ngati munthu akudzithandiza, musamupatse salaamu. 22. Muyenera kupereka salaamu kwa akulu akulu anu modzichepetsa komaso ndi motsitsa mawu. 23. Ngati mwalonjeza kupereka salaamu ya munthu kwa wina, zimakhala Waajib kwa iwe kukwaniritsa lonjezo ndi kupereka …

Read More »

Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wasallam) Amva kuyenda kwa Mapazi a Olemekezeka Bilaal (Radhwiya Allaahu ‘anhu) ku Jannah.

Olemekezeka Abu Hurairah (Radhwiya Allaahu ‘anhu) akusimba kuti nthawi ina, nthawi ya Swalah ya Fajr, Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) adati kwa Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu): “E, Bilaal! Pa ntchito zabwino zomwe umachita mchisilamu, ndi ntchito iti yomwe imakulimbikitsa kuti udzapindula nayo pa tsiku lachiweruzo,chifukwa usiku wapitawu ndamva kuyenda …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 6

14. Amene wayambilira kupereka salaam amalandira Malipiro ochuluka. Abu Umaamah radhwiyallahu anhu wanena kuti Mtumiki swallallahu alaihi wasallam adati: “Amene amayambilira kuwalonjera anthu ena popereka salaamu amadziyandikitsa chifupi kwambiri mwa iwo kwa Allah (amakhala pafupi kwambiri ndi chifundo cha Allah). 15. Munthu akakupatsirani salaamu ya munthu, muyankhe ponena kuti “Alaikum …

Read More »

Olemekezeka Bilal Radhwiyallahu anhu asankhidwa kukhala Muazin wa Rasulullah swallallahu alaihi wasallam

“Mtumiki (sallallahua alaih wasallam) atapanga Hijrah (atasamukira) kupita ku Madina Munawwarah adamanga nzikiti. Atamanga nzikiti adakambirana ndi ophunzira ake nkhani yopezera njira imene angamawaitanire anthu kuti adzaswali. Lidali Khumbo la Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) kuti anthu adzisonkhana ndikuswalira pamodzi munzikiti. Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) sankasangalatsidwa kuti masahabah adzaswali aliyense payekha …

Read More »

Sunnats Ndi Aadaab Za Salaam 5

12. Pangani salaam polowa m’nyumba. Ngati m’nyumba mulibe aliyense, muyenera kupereka salaamu ponena kuti: السَّلَامُ عَلَيْنَا وَعَلَى عِبَادِ اللَّهِ الصَّالِحِينَ Mtendere ukhale pa ife ndi pa akapolo abwino a Allah. Olemekezeka Anas radhwiyallahu anhu adati: nthawi ina Rasulullah swallallahu alaihi wasallam adandiuza kuti: “E iwe mwana wanga okondedwa,ukamalowa m’nyumba mwako, …

Read More »

Kukhanzikika kwa Hazrat Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) pa Chisilamu

Hazrat Bilaal (Radhwiyallahu ‘anhu) ndi Sahaabi otchuka pakati pa ma Swahaabah (radhwiyallahu ‘anhum), ndipo anali muazzin wa mzikiti wa Mtumiki (Swalla Allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam). Poyamba, iye anali kapolo wa ku Abyssinia wa osakhulupirira ku Makkah Mukarramah. Kutembenuka kwake kukhala Msilamu sikunali kokondedwa ndi bwana wake, kotero adazunzidwa mopanda …

Read More »