Fudhail bun Iyaaz (Rahimahullah) aDali Muhaddith olemekezeka komanso oyera mtima wa m’nthawi yake.
Allah Talaa adamdalitsa ndi ulemelero wapamwamba kwambiri mu Hadith kotero kuti ambiri mwa ma Muhadith otsogola, monga Abdullah bin Mubaarak, Sufyaan bun Uyainah ndi Imaam Shaafi’e (Rahimahullah) adafotokoza Hadith kuchokera kwa iye.
Zanenedwa kuti Fudhail (Rahimahullah) asanadalitsidwe ndi udindo wapamwamba mchipembedzo, ankadziwika kuti anali wachifwamba odziwika bwino wa m’misewu. Komabe Allah Talaa adamdalitsa ndi tawfiiq (kuthekera) kuti alape machimo ake ndi kukonza moyo wake.
Nkhani yonse yokhudza kulapa Kwake
Nthaŵi ina, gulu lina la kalavani linkayenda mumsewu umene Fudhail ankabera anthu. Mwa anthu omwe adali paulendowo panali Qaari yemwe ankawerenga Quraan Majiid mwanthetemya kwambiri.
Gululi likudutsa pafupi ndi Fudhail, Qaariy ankawerenga ndime iyi ya Quraan:
Kodi siinafike nthawi yoti mitima ya Asilamu ikhale yamantha pokumbukira Allah…?
Atamva aya iyi, mtima wa Fudhail udakhudzidwa kwambiri moti nthawi yomweyo adatembenukira kwa Allah Talaa kulapa ndikusiya moyo wamachimo.
Pambuyo pake, Fudhail (Rahimahullah) adalimbikira kuchita Ibadah ndi kupeza maphunziro a dini, mpaka idafika nthawi yomwe ngakhale Haarun Rasheed (Rahimahullah) mfumu ya nthawiyo, adayamba kumamuyendera kuti apindule ndi malangizo ake.
Alislaam Yeretsani mtima wanu potsatira chisilamu