Imaam Abu Hanifah Ndi Mafunso Atatu A Mfumu Ya Chiroma

Mfumu yachiroma ulendo wina inatumiza chuma chambiri kwa Khalifa (Mtsogoleri) wa asilamu. isanatumize nthumwi yake ndi chumacho, Mfumuyi inamulamula kuti akafunseko mafunso atatu kwa ma Ulama achisilamu. Nthumwi yachiromayi monga idauzidwira, idafunsa mafunso atatu aja kwa ma Ulama koma sanathe kumupatsa mayankho okhutira. Pa nthawiyo Imaam Abu Hanifah anali mnyamata …

Read More »

Qadah ndi Salaam

7. Ngati ili qa’dah yomaliza, werengani tashahhud, Salawaat Ebrahimiyyah (Durood Ebrahim) ndipo kenako pangani duwa. Duruud Ebrahimiyyah (Durood Ebrahim) ili motere: اَللّٰهُمَّ صَلِّ عَلٰى مُحَمَّدٍ وَّعَلٰى اٰلِ مُحَمَّدٍ كَمَا صَلَّيْتَ عَلٰى إِبْرَاهِيْمَ وَعَلٰى اٰلِ إِبْرَاهِيْمَ وَبَارِكْ عَلٰى مُحَمَّدٍ وَّعَلٰى اٰلِ مُحَمَّدٍ كَمَا بَارَكْتَ عَلٰى إِبْرَاهِيْمَ وَعَلٰى اٰلِ إِبْرَاهِيْمَ فِيْ الْعَالَمِيْنَ …

Read More »

Makhalidwe khumi apadera a Uthmaan (radhwiyallahu anhu)

Hazrat Abu Thawr (rahimahullah) akuti tsiku lina adadza kwa Uthmaan (radhwiyallah”anhu) ndipo adamumva akunena izi panthawi yomwe adaukiridwa. Adati: “Pali ntchito zabwino zokwana khumi zomwe ndadziteteza kwa Allah Taala, ndipo pa ntchito iliyonse ndikuyembekeza kudzalandira malipiro pa tsiku lomaliza; 1) Ndinali munthu wachinayi kuvomereza Chisilamu. 2) Sindinanenepo bodza moyo wanga …

Read More »

Rakaah Yachiwiri

1.Pamene mukudzuka kuchoka pa sajdah, choyamba kwezani chipumi ndi mphuno, kenako zikhato kenako mawondo. 2.Pamene mukuimirira Rakaah yachiwiri, gwirani pansi poika manja anu onse pansipo kuti muthandizikire kunyamuka. 3.Pempherani rakaah yachiwiri monga mwa nthawi zonse (kupatula Dua-ul Istiftaah). Qadah ndi Salaam 1. Pambuyo pa sajda yachiwiri ya rakaah yachiwiri, khalani …

Read More »

Mantha a Hazrat Uthmaan (radhiyallahu ‘anhu) kuliopa tsiku lachiweruzo

Sayyiduna Haani (rahimahullah), kapolo womasulidwa wa Sayyiduna “Uthmaan (radhiyallahu ‘anhu), akunena kuti: Hazrat ‘Uthmaan (radhiyallahu ‘anhu) ankati akayima pamanda, ankalira kwambiri moti ndevu zake zinkanyowa ndi misozi yake. Wina adamufunsa kuti: “Timakuwona kuti ukakumbukira Jannah ndi Jahanmum kapena kukambidwa  za izo, siumakhudzidwa kwambiri mpaka kuyamba kulira, pomwe ukayima pamanda timakuona …

Read More »

Jalsah

1. Nenani takbira ndipo khalani tsonga (jalsah). 2. Phazi lakumanja muliyimike ndi zala zake ndikuyang’anitsa ku qibla. phazi lakumanzere muligoneke ndikulikhalira. 3. Khalani mokumanitsa ntchafu zanu pamodzi (muzikumanitse). 4. Ikani manja anu pa ntchafu ndi zala pamodzi ndipo nsonga za zala zanu zikhale m’mphepete mwa mawondo. 5. Yang’anani malo omwe …

Read More »

Kutsatira Njira Yofewa ndi Yodekha Pochita zinthu ndi Anthu:

“Ataa bin Farrookh (rahimahullah) akufotokoza motere: Tsiku lina lake ‘Uthmaan (radhwiyallaahu ‘anhu) adagula malo kwa munthu wina. Atagula malowa ‘Uthmaan (radhwiyallahu ‘anhu) adadikira kuti munthuyo adzatenge ndalama zake. Komabe, munthuyo sanabwere. ‘Uthmaan (radhiyallahu ‘anhu) adakumana ndi munthuyo pambuyo pake ndipo adamufunsa: “Bwanji sunabwere kudzatenga ndalama zako?” Bamboyo anayankha. “Chomwe chinandipangitsa …

Read More »

Tafseer Ya Surah Falaq Ndi Surah Naas

بِسْمِ اللَّهِ الرَّحْمَٰنِ الرَّحِيمِ قُلْ أَعُوذُ بِرَبِّ الْفَلَقِ ‎﴿١﴾‏ مِن شَرِّ مَا خَلَقَ ‎﴿٢﴾‏ وَمِن شَرِّ غَاسِقٍ إِذَا وَقَبَ ‎﴿٣﴾‏ وَمِن شَرِّ النَّفَّاثَاتِ فِي الْعُقَدِ ‎﴿٤﴾‏ وَمِن شَرِّ حَاسِدٍ إِذَا حَسَدَ ‎﴿٥﴾‏ Nena (iwe Muhammad (Swallallaahu ‘alayhi wasallam): “Ndikudzitchinjiriza mwa Mbuye wa m’bandakucha, ku zoipa zonse zomwe Adazilenga, ndi ku zoipa za mumdima (wa usiku) pamene mdima wake ukufalikira; …

Read More »

Sajdah

1. Nenani takbira ndikupita pa sajdah. 2. Gwirani manja anu m’mawondo pamene mukupita pa sajdah 3. Choyamba ikani mawondo pansi, kenako zikhatho, ndipo pomalizira pake chipumi ndi mphuno pamodzi. 4. Siyani zala zotsekeka moyang’anitsa ku chibla. 5. Ikani zikhatho zanu pansi m’njira yoti zala zifanane ndi makutu ndipo mbali zigwirizane …

Read More »

Hayaa ya Hazrat ‘Uthmaan (Radhiyallahu ‘anhu)

Hazrat Aaishah (radhiya allahu ‘anha) akusimba motere: Nthawi ina, Mtumiki (swalla allaahu ‘alayhi wa aalihi wasallam) anali atagona kunyumba kwanga ndipo thupi lake linasunthidwa pang’ono kuchokera kudera la ntchafu zake zodalitsika kapena ntchafu yake yodalitsika, ngakhale ntchafu zodalitsidwa ndi shins zidakutidwa ndi lungi lake. Panthawi imeneyo, Abu Bakr (radhiyallahu ‘anhu) …

Read More »