Zikhulupiliro zokhudza Allah

1. Allah Ta ‘ala yekha ndamene akuyenera kumpembedza.

2. China chilichonse chisadapezeke pano padziko, kunalibe chilichonse kupatula Allah yekha, kenaka Allah adalenga chilichonse. Kupatula Allah, palibe amene alindi mphanu zolenga chinachirichonse kapena kupeleka moyo ndi imfa.

Read More »

Kuyesedwa Kwa Durood Pa Mlingo Wokwanira

Sayyiduna Abu Hurairah (radhiyallahu anhu) akufotokoza kuti Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) adati, amene akufuna kuti Durood yake ikaikidwe pa sikelo ndikukalemera kwambiri kuti munthu akalandire mphotho yochuluka akatiwerengera Durood adzichulukitsa kuwerenga Durood iyi:

Oh Allah! Tumizani Durood kwa Muhammad (sallallahu alaih wasallam), Mtumiki amene anali osatha kulemba ndi kuwerenga, akazi ake onse, amayi a anthu onse omwe ndi okhulupilira, akubanja kwake ndi fuko lake lonse monga munatumizira Durood ku banja la nabi Ibrahim alaih salaam, ndinthudi ndiinu otamandidwa komanso olemekezeka.

Read More »

Kasambidwe Ka Sunnah-Gawo 4

14. Onetsetsani kuti madzi akufika pena paliponse pathupi lanu, nthawi ina iliyonse mukadzithira madzi dzinyureni ndicholinga chofuna kuonetsetsa kuti madziwo alowa pakhungu lonse, ngakhale kutangotsala malo ochepetsetsa kwambiri osathiridwa madzi, kusamba (kwa fardh) sikudzatheka, pamene mukusambitsa thupi, sambitsani kutsogolo kwake kenako kumbuyo.

Read More »

Kufunika kokhala ndi chikhulupiliro chenicheni (choyenera)

Chipembedzo chachisilamu pamodzi ndi nsanamira zake chagona pa chikhulupiliro chenicheni, ngati zikhulupiliro za munthu ndizolakwika, ngakhale kuti sizingamutulutse m’chisilamu, ngakhale atachita ntchito zabwino zachisilamu, sangalandire malipiro amene Allah adalonjeza, chifukwa choti zikhulupiliro zake ndi tsinde lenileni lachisilamu ndizolakwika.

Read More »

Kasambidwe Ka Sunnah-Gawo 3

9. Pangani wudhu onse.

Sayyidatuna Aaishah (radhiyallahu anha) akunena kuti, Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) ankati akamakasamba (kusamba kwa fardh) ankayamba ndikusamba m’manja asanalowetse manjawo m’madzi, kenaka ankatsuka malo obisika kenaka ankapanga wudhu ngati m’mene ankapangira(wudhu) akafuna kuswali.

Read More »

Kufika Kwa Durood Ya Ummah Kwa Sayyiduna Rasulullaah (Sallallahu Alaih Wasallam)

Abu Hurairah (radhiyallahu anhu) akusimba kuti Rasulullah (sallallahu alaih wasallam) adanena kuti " nyumba zanu musazipange kukhala ngati ndi manda (zipangeni nyumba zanu kukhala za moyo popangilamo ntchito za bwino monga ngati swalah, kuwerenga Qur’aan majeed ndi zina zambiri. Choncho mukamatero nyumba zanu sizikhala ngati ndi manda kumene sikumachitikako ma aamaal abwino.) Ndipo manda anga musawatenge ngati ndi malo opangilapo zisangalalo, komanso mudziwerenga durood kwa ine, ndithudi mwa njira ina iliyonse Durood yo imandifika (kudzera mwa angelo) kuchokera kwina kuli konse komwe muli."

Read More »